Yeremiya 43 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 43:1-13

1Yeremiya atatsiriza kuwawuza anthuwo mawu onse a Yehova Mulungu wawo, amene Yehova anamutuma kuti akawawuze, 2Azariya mwana wa Hosayia ndi Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi anthu onse odzikuza anawuza Yeremiya kuti, “Ukunama iwe! Yehova Mulungu wathu sanakutume kuti unene kuti, ‘Musapite ku Igupto kukakhala kumeneko.’ 3Koma ndi Baruki mwana wa Neriya amene akukulimbikitsa kuti utiletse zopita ku Igupto ndi kuti mʼmalo mwake tidzipereke mʼmanja mwa Ababuloni, kuti iwo atiphe kapena kutitenga ukapolo ku Babuloni.”

4Motero Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi anthu onse sanamvere lamulo la Yehova loti akhale mʼdziko la Yuda. 5Mʼmalo mwake, Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo anatenga anthu onse otsala a ku Yuda amene anabwera kudzakhala mʼdziko la Yuda kuchokera ku mayiko onse kumene anabalakirako. 6Mʼgulu la anthu otengedwalo munali amuna onse, akazi ndi ana, ana aakazi a mfumu, ndiponso anthu amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anawasiya kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani pamodzinso ndi mneneri Yeremiya ndi Baruki mwana wa Neriya. 7Kotero anthuwo analowa mʼdziko la Igupto chifukwa anakana kumvera Yehova, nakafika ku Tapanesi.

8Ndipo Yehova anayankhula ndi Yeremiya ku Tapanesi kuti, 9“Tenga miyala inayi yayikulu ndipo uyikwirire mʼdothi pa chiwundo cha polowera ku nyumba yaufumu ya Farao ku Tapanesi. Uchite zimenezi Ayuda onse akuona. 10Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayitana mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzakhazika mpando wake waufumu pa miyala imene ndayikwirira apayi. Iye adzafunyulula tenti yake yaufumu pa miyala imeneyi. 11Iye adzabwera kudzathira nkhondo Igupto. Iwo oyenera kufa ndi mliri adzafa ndi mliri, iwo oyenera kutengedwa ukapolo adzatengedwa ukapolo, ndipo iwo oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga. 12Adzayatsa moto mʼnyumba zopembedzera milungu ya Igupto. Adzayeretsa dziko la Igupto monga momwe mʼbusa amayeretsera chovala chake pochotsamo nsabwe. Pambuyo pake adzachoka mʼdziko la Igupto mwa mtendere. 13Ku Iguptoko adzagwetsa zipilala zachipembedzo za ku nyumba yopembedzera mulungu wa dzuwa. Adzatentha ndi moto nyumba za milungu ya ku Igupto.’ ”

New International Reader’s Version

Jeremiah 43:1-13

1Jeremiah finished telling the people everything the Lord their God had said. Jeremiah told them everything the Lord had sent him to tell them. 2After that, Azariah, the son of Hoshaiah, and Johanan, the son of Kareah, spoke to Jeremiah. And all the proud men joined them. They said, “You are lying! The Lord our God hasn’t sent you to speak to us. He hasn’t told you to say, ‘You must not go to Egypt and make your homes there.’ 3But Baruch, the son of Neriah, is turning you against us. He wants us to be handed over to the Babylonians. Then they can kill us. Or they can take us away to Babylon.”

4So Johanan, the son of Kareah, disobeyed the Lord’s command. So did all the other army officers and all the people. They didn’t stay in the land of Judah. 5Instead Johanan, the son of Kareah, and all the other army officers led away all the people who were left in Judah. Those people had returned to Judah from all the nations where they had been scattered. 6Johanan and the other officers also led away many people Nebuzaradan had left at Mizpah. They included men, women and children. They also included the king’s daughters. Nebuzaradan had left them with Gedaliah, the son of Ahikam. They also took Jeremiah the prophet and Baruch son of Neriah along with them. Nebuzaradan was commander of the royal guard. Ahikam was the son of Shaphan. 7So the Jewish leaders disobeyed the Lord. They took everyone to Egypt. They went all the way to Tahpanhes.

8In Tahpanhes a message from the Lord came to Jeremiah. The Lord said, 9“Make sure the Jews are watching you. Then get some large stones. Go to the entrance to Pharaoh’s house in Tahpanhes. Bury the stones in the clay under the brick walkway there. 10Then tell the Jews, ‘The Lord who rules over all is the God of Israel. He says, “I will send for my servant Nebuchadnezzar, the king of Babylon. And I will set his throne over these stones that are buried here. He will set up his royal tent over them. 11He will come and attack Egypt. He will bring death to those I have appointed to die. He will take away as prisoners those I have appointed to be taken away. And he will kill with swords those I have appointed to be killed. 12He will set the temples of the gods of Egypt on fire. He will burn down their temples. He will take away the statues of their gods. Nebuchadnezzar will be like a shepherd who picks his coat clean of lice. Nebuchadnezzar will pick Egypt clean and then depart. 13At Heliopolis in Egypt he will smash the sacred pillars to pieces. And he will burn down the temples of the gods of Egypt.” ’ ”