Yeremiya 31 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 31:1-40

1“Pa nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “Ndidzakhala Mulungu wa mafuko onse a Israeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.”

2Yehova akuti,

“Anthu amene anapulumuka ku nkhondo

ndinawakomera mtima mʼchipululu;

pamene Aisraeli ankafuna kupumula.”

3Ine ndinawaonekera ndili chapatali ndipo ndinati,

“Ine ndakukondani ndi chikondi chopanda malire.

Nʼchifukwa chake ndipitiriza kukukondani.

4Ndidzakusamaliraninso, inu anthu a Israeli;

mudzasangalala poyimba tizitoliro tanu,

ndipo mudzapita kukavina nawo

anthu ovina mwachimwemwe.

5Mudzalimanso minda ya mpesa

pa mapiri a Samariya;

alimi adzadzala mphesa

ndipo adzadya zipatso zake.

6Lidzafika tsiku pamene alonda adzafuwula

pa mapiri a Efereimu nati,

‘Tiyeni tipite ku Ziyoni,

kwa Yehova Mulungu wathu.’ ”

7Yehova akuti,

“Imbani mosangalala chifukwa cha Yakobo,

fuwulani chifukwa cha mtundu wopambana mitundu yonse.

Matamando anu amveke, ndipo munene kuti,

‘Yehova wapulumutsa anthu ake

otsala a Israeli.’

8Taonani, ndidzabwera nawo kuchokera ku dziko la kumpoto,

ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku malekezero a dziko lapansi.

Anthu osaona, olumala, amayi oyembekezera

ndi amene ali pa nthawi yawo yochira adzabwera nawo pamodzi.

Chidzakhala chikhamu cha anthu obwerera kuno.

9Adzabwera akulira;

koma Ine ndikuwatonthoza mtima, ndidzawaperekeza.

Ndidzawatsogolera ku mitsinje yamadzi

mʼnjira yosalala mmene sadzapunthwamo.

Chifukwa ndine abambo ake a Israeli,

ndipo Efereimu ndi mwana wanga woyamba.

10“Imvani mawu a Yehova inu anthu a mitundu ina;

lalikirani mawuwa kwa anthu a mayiko akutali a mʼmbali mwa nyanja;

‘Iye amene anabalalitsa Israeli adzawasonkhanitsanso

ndipo adzayangʼanira nkhosa zake ngati mʼbusa.’

11Pakuti Yehova wawombola fuko la Yakobo

anawapulumutsa mʼdzanja la anthu owaposa mphamvu.

12Anthuwo adzabwera akuyimba mofuwula pa mapiri a Ziyoni;

adzasangalala ndi zinthu zabwino zochokera kwa Yehova.

Zinthu zabwinozo ndi izi: tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta,

ana ankhosa ndi ana angʼombe.

Iwo adzakhala ngati munda wothiriridwa bwino,

ndipo sadzamvanso chisoni.

13Pamenepo anamwali adzavina ndi kusangalala.

Anyamata ndi okalamba nawonso adzasangalala.

Kulira kwawo ndidzakusandutsa chisangalalo;

ndidzawasangalatsa nʼkuchotsa chisoni chawo.

14Ansembe ndidzawadyetsa chakudya chabwino,

ndipo anthu anga adzakhuta ndi zabwino zanga,”

akutero Yehova.

15Yehova akuti,

“Kulira kukumveka ku Rama,

kulira kwakukulu,

Rakele akulirira ana ake.

Sakutonthozeka

chifukwa ana akewo palibe.”

16Yehova akuti,

“Leka kulira

ndi kukhetsa misozi

pakuti udzalandira mphotho ya ntchito yako,”

akutero Yehova.

“Iwo adzabwerako ku dziko la adani.

17Tsono chiyembekezo chilipo pa zamʼtsogolo,”

akutero Yehova.

“Ana ako adzabwerera ku dziko lawo.

18“Ndithu ndamva Efereimu akubuwula kuti,

‘Ife tinali ngati ana angʼombe osamva.

Koma inu mwatiphunzitsa kumvera.

Mutibweze kuti tithe kubwerera,

chifukwa ndinu Yehova Mulungu wanga.

19Popeza tatembenuka mtima,

ndiye tikumva chisoni;

popeza tazindikira

ndiye tikudziguguda pachifukwa.

Tachita manyazi ndipo tanyazitsidwa

chifukwa tinachimwa paubwana wathu.’

20Kodi Efereimu si mwana wanga wokondedwa,

mwana amene Ine ndimakondwera naye?

Ngakhale nthawi zambiri ndimamudzudzula,

ndimamukumbukirabe.

Kotero mtima wanga ukumufunabe;

ndimamumvera chifundo chachikulu kwambiri,”

akutero Yehova.

21“Muyike zizindikiro za mu msewu;

muyimike zikwangwani.

Yangʼanitsitsani msewuwo,

njira imene mukuyendamo.

Bwerera, iwe namwali wa Israeli,

bwerera ku mizinda yako ija.

22Udzakhala jenkha mpaka liti,

iwe mwana wa mkazi wosakhulupirika?

Yehova walenga chinthu chatsopano pa dziko lapansi; mkazi ndiye tsopano aziteteza mwamuna.”

23Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndikadzabwera nawo anthuwa kuchokera ku ukapolo, anthu a mʼdziko la Yuda ndi amene akukhala mʼmizinda yake adzayankhulanso mawu akuti, ‘Yehova akudalitse, iwe malo achilungamo, iwe phiri lopatulika.’ 24Anthu adzakhala ku Yuda ndi ku mizinda yake pamodzi ndi alimi ndi oweta nkhosa. 25Ndidzatsitsimutsa anthu otopa ndipo ndidzadyetsa anthu anjala.”

26Pamenepo ndinadzuka nʼkuyangʼana uku ndi uku. Tulo tanga tinali tokoma.

27“Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachulukitsa anthu pamodzi ndi ziweto mʼdziko la Israeli ndi la Yuda. 28Monga momwe ndinasamalira powazula, powagwetsa, powagumula, powawononga ndi powachita zoyipa, momwemonso ndidzasamala powamanga ndi powadzala” akutero Yehova. 29“Mʼmasiku amenewo anthu sadzanenanso kuti,

“Makolo adya mphesa zosapsa,

koma mano a ana ndiye achita dziru.

30Mʼmalo wake, munthu aliyense adzafa chifukwa cha tchimo lake. Iye amene adzadye mphesa zosapsazo ndiye amene mano ake adzachite dziru.”

31“Masiku akubwera,” akutero Yehova,

“pamene ndidzachita pangano latsopano

ndi Aisraeli

ndiponso nyumba ya Yuda.

32Silidzakhala ngati pangano

limene ndinachita ndi makolo awo

pamene ndinawagwira padzanja

nʼkuwatulutsa ku Igupto;

chifukwa anaphwanya pangano langa,

ngakhale ndinali mwamuna wawo,”

akutero Yehova.

33“Ili ndi pangano limene ndidzachita ndi Aisraeli

atapita masiku amenewo,” akutero Yehova.

“Ndidzayika lamulo langa mʼmitima mwawo

ndi kulilemba mʼmaganizo mwawo.

Ine ndidzakhala Mulungu wawo

ndipo iwo adzakhala anthu anga.

34Sipadzafunikanso kuti wina aphunzitse mnzake,

kapena munthu wina kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, ‘Mudziwe Yehova,’

chifukwa onse adzandidziwa Ine,

kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,”

akutero Yehova.

“Ndidzawakhululukira zoyipa zawo

ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”

35Yehova akuti,

Iye amene amakhazikitsa dzuwa

kuti liziwala masana,

amene amalamula kuti mwezi ndi nyenyezi

ziziwala usiku,

amene amavundula nyanja

kuti mafunde akokome,

dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:

36Ngati zimenezi zilekeka pamaso panga, akutero Yehova, pamenepo padzakhala pamathero a fuko la Israeli pamaso panga.

37Yehova akuti,

“Ndidzataya fuko la Israeli chifukwa cha machimo awo.

Ngati patapezeka munthu

amene angathe kupima zakuthambo

nʼkufufuza maziko a dziko lapansi.”

38“Taonani masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene mzinda wa Yehova udzamangidwanso kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku Chipata cha Ngodya. 39Malire ake adzayambira pamenepo kupita ku phiri la Garebu, nʼkudzakhota kuloza ku Gowa. 40Chigwa chonse mʼmene amatayiramo mitembo ndi phulusa, ndiponso minda yonse kuyambira ku Chigwa cha Kidroni mpaka ku ngodya ya Chipata cha Akavalo mbali ya kummawa, adzakhala malo opatulika a Yehova. Mzindawu sadzawuzulanso kapena kuwuwononga.”

New International Reader’s Version

Jeremiah 31:1-40

1“At that time I will be the God of all the families of Israel,” announces the Lord. “And they will be my people.”

2The Lord says,

“Some of my people will live through

everything their enemies do to them.

They will find help in the desert.

I will come to give peace and rest to Israel.”

3The Lord appeared to us in the past. He said,

“I have loved you with a love that lasts forever.

I have kept on loving you with a kindness that never fails.

4I will build you up again.

Nation of Israel, you will be rebuilt.

Once again you will use your tambourines to celebrate.

You will go out and dance with joy.

5Once again you will plant vineyards

on the hills of Samaria.

Farmers will plant them.

They will enjoy their fruit.

6There will be a day when those on guard duty will cry out.

They will stand on the hills of Ephraim.

And they will shout,

‘Come! Let’s go up to Zion.

Let’s go up to where the Lord our God is.’ ”

7The Lord says,

“Sing for joy because the people of Jacob are blessed.

Shout because the Lord has made them the greatest nation.

Make your praises heard.

Say, ‘Lord, save your people.

Save the people who are left alive in Israel.’

8I will bring them from the land of the north.

I will gather them from one end of the earth to the other.

Even those who are blind and those who can’t walk

will be among them.

Pregnant women and women having their babies

will be among them also.

Many of them will return.

9Their eyes will be filled with tears as they come.

They will pray as I bring them back.

I will lead them beside streams of water.

I will lead them on a level path

where they will not trip or fall.

I am Israel’s father.

And Ephraim is my oldest son.

10“Listen to my message, you nations.

Announce it on shores far away.

Say, ‘He who scattered Israel will gather them.

He will watch over his flock like a shepherd.’

11I will set the people of Jacob free.

I will save them from those who are stronger than they are.

12They will come and shout for joy on Mount Zion.

They will be joyful because of everything I give them.

I give them grain, olive oil and fresh wine.

I give them the young animals in their flocks and herds.

Israel will be like a garden that has plenty of water.

And they will not be sad anymore.

13Then young women will dance and be glad.

And so will the men, young and old alike.

I will turn their mourning into gladness.

I will comfort them.

And I will give them joy instead of sorrow.

14I will satisfy the priests. I will give them more than enough.

And my people will be filled with the good things I give them,”

announces the Lord.

15The Lord says,

“A voice is heard in Ramah.

It is the sound of weeping and deep sadness.

Rachel is weeping for her children.

She refuses to be comforted,

because they are gone.”

16The Lord says,

“Do not weep anymore.

Do not let tears fall from your eyes.

I will reward you for your work,”

announces the Lord.

“Your children will return from the land of the enemy.

17So there is hope for your children,”

announces the Lord.

“Your children will return to their own land.

18“I have heard the groans of Ephraim’s people. They say,

‘You corrected us like a calf you were training.

And we have been trained.

Bring us back to you, and we will come back.

You are the Lord our God.

19After we wandered away from you,

we turned away from our sins.

After we learned our lesson,

we beat our chests in sorrow.

We were full of shame.

What we did when we were young brought dishonor on us.’

20Aren’t the people of Ephraim my dear children?

Aren’t they the children I take delight in?

I often speak against them.

But I still remember them.

So my heart longs for them.

I love them with a tender love,”

announces the Lord.

21The Lord says, “Put up road signs.

Set up stones to show the way.

Look carefully for the highway.

Look for the road you will take.

Return, people of Israel.

Return to your towns.

22How long will you wander,

my people Israel, who are not faithful to me?

I will create a new thing on earth.

The woman will return to the man.”

23The Lord who rules over all is the God of Israel. He says, “I will bring them back from the place where they were taken. Here is what the people in Judah and its towns will say once again. ‘May the Lord bless you, you successful city. Sacred mountain, may he bless you.’ 24People will live together in Judah and all its towns. Farmers and shepherds will live there. 25I will give rest to those who are tired. I will satisfy those who are weak.”

26When I heard this, I woke up and looked around. My sleep had been pleasant to me.

27Here is what the Lord announces. “The days are coming when I will plant the kingdoms of Israel and Judah again. I will plant them with children and young animals. 28I watched over Israel and Judah to pull them up by the roots. I tore them down. I crushed them. I destroyed them. I brought horrible trouble on them. But now I will watch over them to build them up and plant them,” announces the Lord. 29“In those days people will no longer say,

“ ‘The parents have eaten sour grapes.

But the children have a bitter taste in their mouths.’

30Instead, everyone will die for their own sin. The one who eats sour grapes will taste how bitter they are.

31“The days are coming,” announces the Lord.

“I will make a new covenant

with the people of Israel.

I will also make it with the people of Judah.

32It will not be like the covenant

I made with their people of long ago.

That was when I took them by the hand.

I led them out of Egypt.

But they broke my covenant.

They did it even though I was like a husband to them,”

announces the Lord.

33“This is the covenant I will make with Israel

after that time,” announces the Lord.

“I will put my law in their minds.

I will write it on their hearts.

I will be their God.

And they will be my people.

34They will not need to teach their neighbor anymore.

And they will not need to teach one another anymore.

They will not need to say, ‘Know the Lord.’

That’s because everyone will know me.

From the least important of them to the most important,

all of them will know me,”

announces the Lord.

“I will forgive their evil ways.

I will not remember their sins anymore.”

35The Lord speaks.

He makes the sun

shine by day.

He orders the moon and stars

to shine at night.

He stirs up the ocean.

He makes its waves roar.

His name is the Lord Who Rules Over All.

36“Suppose my orders for creation disappear from my sight,”

announces the Lord.

“Only then will the people of Israel stop being

a nation in my sight.”

37The Lord says,

“Suppose the sky above could be measured.

Suppose the foundations of the earth below could be completely discovered.

Only then would I turn away the people of Israel.

Even though they have committed many sins,

I will still accept them,”

announces the Lord.

38“The days are coming,” announces the Lord. “At that time Jerusalem will be rebuilt for me. It will be rebuilt from the Tower of Hananel to the Corner Gate. 39The measuring line will reach out from there. It will go straight to the hill of Gareb. Then it will turn and reach as far as Goah. 40There is a valley where dead bodies and ashes are thrown. That whole valley will be holy to me. The side of the Kidron Valley east of the city will be holy to me. It will be holy all the way to the corner of the Horse Gate. The city will never again be pulled up by the roots. It will never be destroyed.”