Yeremiya 29 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 29:1-32

Kalata Yolembera Anthu a ku Ukapolo

1Yeremiya anatumiza kalata kuchokera ku Yerusalemu kupita kwa akuluakulu amene anali ku ukapolo, ndiponso kwa ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse amene Nebukadinezara anawatenga ku Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni. 2Zimenezi zinachitika mfumu Yekoniya, amayi a mfumu, nduna za mfumu ndiponso atsogoleri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, anthu aluso ndi amisiri atatengedwa ku Yerusalemu kupita ku ukapolo. 3Yeremiya anapatsira kalatayo Eleasa mwana wa Safani ndi Gemariya mwana wa Hilikiya, amene Zedekiya mfumu ya Yuda anawatumiza kwa Mfumu Nebukadinezara ku Babuloni. Mʼkalatamo analembamo kuti:

4Anthu onse amene anatengedwa ukapolo kuchokera ku Yerusalemu kupita ku Babuloni, Yehova akuwawuza kuti, 5“Mangani nyumba ndipo muzikhalamo. Limani minda ndipo mudye zipatso zake. 6Kwatirani ndipo mubereke ana aamuna ndi aakazi. Ana anu aamuna muwasankhire akazi ndipo muwasankhire amuna ana anu aakaziwo, kuti nawonso abale ana aamuna ndi aakazi. Muchulukane kumeneko. Chiwerengero chanu chisachepe. 7Ndiponso muzifunafuna mtendere ndi ubwino wa mzinda umene ndinakupirikitsirani ku ukapoloko. Muzipempherera mzindawo kwa Yehova, kuti zikuyendereni bwino.” 8Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, “Musalole kuti aneneri ndi owombeza amene ali pakati panu akunyengeni. Musamvere maloto awo. 9Iwo akunenera zabodza kwa inu mʼdzina langa ngakhale Ine sindinawatume,” akutero Yehova.

10Yehova akuti, “Zaka 70 za ku Babuloni zikadzatha, ndidzabwera kudzakuchitirani zabwino zonse zimene ndinakulonjezani zija, ndipo ndidzakubwezerani ku malo ano. 11Pakuti Ine ndikudziwa zimene ndinakukonzerani,” akutero Yehova, “ndimalingalira zabwino zokhazokha za inu osati zoyipa, ayi. Ndimalingalira zinthu zokupatsani chiyembekezo chenicheni pa za mʼtsogolo. 12Nthawi imeneyo mudzandiyitana, ndi kunditama mopemba ndipo ndidzakumverani. 13Mudzandifunafuna ndipo mudzandipeza. Mukadzandifuna ndi mtima wanu wonse 14mudzandipezadi,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubwezerani zabwino zanu. Ndidzakusonkhanitsani kuchokera ku mayiko onse ndi kumalo konse kumene munali,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubweretsani kumalo kumene munali ndisanakuchotseni kukupititsani ku ukapolo.”

15Inu mumati, “Yehova watiwutsira aneneri athu ku Babuloni,” 16koma zimene Yehova akunena za mfumu imene ikukhala pa mpando waufumu wa Davide pamodzi ndi anthu onse amene anatsala mu mzinda muno, abale anu amene sanapite nanu ku ukapolo ndi izi, 17Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawapha ndi nkhondo, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa ngati nkhuyu zowola kwambiri, zosati nʼkudya. 18Ndidzawalondola ndi lupanga, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa anthu amayiko onse a pa dziko lapansi. Adzakhala otembereredwa, ochititsa mantha, onyozeka ndiponso ochitidwa chipongwe pakati pa anthu a mitundu yonse kumene ndawapirikitsirako. 19Zidzatero chifukwa sanamvere mawu anga amene ndinkawatumizira kudzera mwa atumiki anga, aneneri. Ngakhale inu amene muli ku ukapolo simunamverenso,” akutero Yehova.

20Choncho, imvani mawu a Yehova, inu akapolo nonse amene ndinakuchotsani mu Yerusalemu ndi kukupititsani ku Babuloni. 21Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti zokhudza Ahabu mwana wa Kolaya ndi Zedekiya mwana wa Maseya, amene akulosera zabodza kwa inu mʼdzina langa: “Taonani ndidzawapereka kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzawapha inu mukupenya. 22Chifukwa cha anthu awiriwo, akapolo onse ochokera ku Yuda amene ali ku Babuloni adzagwiritsa ntchito mawu awa potemberera: ‘Yehova achite nawe monga mmene anachitira ndi Zedekiya ndi Ahabu, amene mfumu ya ku Babuloni inawatentha.’ 23Pakuti anthu amenewa achita zoyipa kwambiri mu Israeli; achita chigololo ndi akazi a eni ake ndipo mʼdzina langa ankayankhula zabodza zimene sindinawawuze kuti atero. Ine ndikuzidziwa ndipo ndine mboni ya zimenezi,” akutero Yehova.

Kalata ya Semaya

24Ukamuwuze Semaya wa ku Nehelamu kuti, 25“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Iwe unatumiza kalata mʼdzina lako kwa anthu onse a mu Yerusalemu, kwa Zefaniya mwana wa wansembe Maseya, ndi kwa ansembe onse. Unalemba mu kalatayo kuti, 26‘Yehova wakusankha kukhala wansembe mʼmalo mwa Yehoyada kuti ukhale wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Yehova. Munthu aliyense wamisala amene akudziyesa kuti ndi mneneri uzimuponya mʼndende ndi kumuveka goli lachitsulo. 27Nanga tsono chifukwa chiyani simunamuchitire zimenezi Yeremiya wa ku Anatoti, amene amakhala ngati mneneri pakati panu? 28Yeremiyayo watitumizira uthenga uwu kuno ku Babuloni: Ukapolo wanu ukhala wa nthawi yayitali. Choncho mangani nyumba ndipo muzikhalamo; limani minda ndipo mudye zipatso zake.’ ”

29Koma wansembe Zefaniya anayiwerenga kalatayo pamaso pa mneneri Yeremiya. 30Ndipo Yehova anawuza Yeremiya kuti, 31“Tumiza uthenga uwu kwa akapolo onse: ‘Yehova akuti zokhudza Semaya wa ku Nehelamu: Semaya wakuloserani, ngakhale kuti Ine sindinamutume, ndipo wakunyengani kuti muzikhulupirira bodza. 32Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti: Mʼbanja lakelo sipadzakhala munthu pakati pa mtundu uno wa anthu amene adzaone zinthu zabwino zimene ndidzachitira anthu anga chifukwa analalika zondiwukira,’ ” akutero Yehova.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米书 29:1-32

致信给被掳的人

1-2耶哥尼雅王、太后、宫廷侍臣、犹大耶路撒冷的官员、技工和工匠被尼布甲尼撒王掳到巴比伦后,耶利米先知从耶路撒冷寄信给被掳之人中幸存的长老、先知和众民。 3犹大西底迦沙番的儿子以利亚萨希勒迦的儿子基玛利把这封信送给巴比伦尼布甲尼撒。以下是信的内容:

4以色列的上帝——万军之耶和华对所有从耶路撒冷被掳到巴比伦的人说: 5“你们要建造房子住下来,要耕种田园,吃田中的出产。 6你们要娶妻生子,也要给你们的儿女娶妻选夫,使他们生儿育女,你们好在那里人丁兴旺,不致人口减少。 7你们要为所住的城市谋求福祉,向耶和华祷告,因为你们的福祉有赖于那城的福祉。” 8以色列的上帝——万军之耶和华说:“不要被你们中间的先知和占卜者欺骗,不要听信他们做的梦。 9他们以我的名义对你们说假预言,其实我并没有差遣他们。这是耶和华说的。”

10耶和华说:“你们被掳到巴比伦七十年期满后,我就要眷顾你们,成就我充满恩典的应许,把你们带回这地方。 11因为我知道我为你们安排的计划。我的计划不是要降祸给你们,而是要赐福给你们,使你们的未来充满希望。这是耶和华说的。 12那时,你们必呼求我,向我祷告,我也必垂听。 13你们寻求我,就必寻见。只要你们全心寻求我, 14我必让你们寻见。这是耶和华说的。我必把你们从流放之地招聚起来,使你们回到故土。这是耶和华说的。

15“你们说耶和华在巴比伦为你们选立了先知, 16但论到坐在大卫宝座上的君王和这城里的百姓,就是没有与你们一同被掳的同胞, 17万军之耶和华这样说,‘看啊,我必使战争、饥荒和瘟疫临到他们,使他们像烂得不能吃的无花果。 18我要使他们饱受战争、饥荒和瘟疫之灾,使他们的遭遇令天下万国惊惧。在我流放他们去的地方,他们必受凌辱、嘲笑、讥讽和咒诅。 19这都是因为他们不听我的话。这是耶和华说的。我曾屡次差遣我的仆人——众先知去警告他们,他们却不肯听。’这是耶和华说的。 20因此,你们这些从耶路撒冷被掳到巴比伦的人啊!要听耶和华的话。 21以色列的上帝——万军之耶和华说,‘哥赖雅的儿子亚哈玛西雅的儿子西底迦以我的名义说假预言,我要把他们交在巴比伦尼布甲尼撒的手中,让他当着你们的面处死他们。 22被掳到巴比伦犹大人咒诅人的时候会说,“愿耶和华使你的下场像被巴比伦王烧死的西底迦亚哈一样!” 23因为他们二人在以色列做了恶事,与他人的妻子通奸。我没有差派他们,他们却奉我的名说假预言。我知道他们的所作所为,我对这一切了如指掌。’这是耶和华说的。”

24耶和华吩咐我对尼希兰示玛雅说: 25以色列的上帝——万军之耶和华说,你曾以自己的名义写信给住在耶路撒冷的众民、玛西雅的儿子西番雅祭司及其他祭司。你在信中对西番雅说, 26‘耶和华已立你为祭司代替耶何耶大,管理耶和华的殿,负责拘捕妄自发预言的狂人,给他们戴上铁链枷锁。 27现在,亚拿突耶利米在你们当中自称为先知,你为什么不斥责他呢? 28他甚至寄信给我们这些在巴比伦的人,说被掳的日子还很长久,要我们建房子住下来,耕种田园,吃田中的出产。’”

29西番雅祭司就把示玛雅的信读给耶利米先知听。 30耶和华对耶利米说: 31“你派人送信给所有被掳的人,说,‘耶和华说祂没有差遣尼希兰示玛雅,他却说预言,诱使你们听信谎言, 32所以耶和华必惩罚他和他的后代,使他断子绝孙,看不到耶和华赐给祂子民的福祉,因为他说了悖逆耶和华的话。这是耶和华说的。’”