Yeremiya 23 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 23:1-40

Nthambi Yolungama

1“Tsoka kwa abusa amene akuwononga ndi kubalalitsa nkhosa za pabusa panga!” akutero Yehova. 2Nʼchifukwa chake Yehova, Mulungu wa Israeli, ponena za abusa amene akuweta anthu anga akuti, “Mwabalalitsa ndi kumwaza nkhosa zanga. Komanso simunazisamale bwino. Choncho ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu,” akutero Yehova. 3“Pambuyo pake Ine mwini wakene ndidzasonkhanitsa nkhosa zanga zotsala, kuzichotsa ku mayiko onse kumene ndinazibalalitsira ndi kuzibweretsanso ku msipu wawo. Kumeneko zidzaswana ndi kuchulukana. 4Ndidzazipatsa abusa amene adzaziweta, ndipo sizidzaopanso kapena kuchita mantha, ndipo palibe imene idzasochera,” akutero Yehova.

5Yehova akuti, “Masiku akubwera,

pamene ndidzaphukitsira Davide Nthambi yowongoka.

Imeneyi ndiye mfumu imene idzalamulira mwanzeru, mwachilungamo ndi mosakondera mʼdziko.

6Pa masiku a ulamuliro wake Yuda adzapulumuka

ndipo Israeli adzakhala pamtendere.

Dzina limene adzamutcha ndi ili:

Yehova ndiye Chilungamo Chathu.

7Choncho, masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene anthu sadzanenanso polumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku Igupto,’ 8koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa zidzukulu za Israeli ku dziko lakumpoto ndi ku mayiko konse kumene anawabalalitsira.’ Ndipo iwo adzawabweretsa ku dziko lawolawo.”

Aneneri Onyenga

9Kunena za aneneri awa:

Mtima wanga wasweka;

mʼnkhongono mwati zii.

Ndakhala ngati munthu woledzera,

ngati munthu amene wasokonezeka ndi vinyo,

chifukwa cha Yehova

ndi mawu ake opatulika.

10Dziko ladzaza ndi anthu achigololo;

lili pansi pa matemberero.

Dziko lasanduka chipululu ndipo msipu wawuma.

Aneneri akuchita zoyipa

ndipo akugwiritsa ntchito mphamvu zawo molakwika.

11“Mneneri ngakhale wansembe onse sapembedza Yehova.

Amachita zoyipa ngakhale mʼnyumba yanga,”

akutero Yehova.

12“Nʼchifukwa chake njira zawo zidzakhala zoterera;

adzawapirikitsira ku mdima

ndipo adzagwera kumeneko.

Adzaona zosaona

mʼnthawi ya chilango chawo,”

akutero Yehova.

13“Pakati pa aneneri a ku Samariya

ndinaona chonyansa ichi:

Ankanenera mʼdzina la Baala

ndipo anasocheretsa anthu anga, Aisraeli.

14Ndipo pakati pa aneneri a ku Yerusalemu

ndaonapo chinthu choopsa kwambiri:

amachita chigololo, amanena bodza

ndipo amalimbitsa mtima anthu ochita zoyipa.

Choncho palibe amene amasiya zoyipa zake.

Kwa Ine anthu onsewa

ali ngati a ku Sodomu ndi Gomora.”

15Choncho ponena za aneneriwa Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Ndidzawadyetsa zakudya zowawa

ndi kuwamwetsa madzi a ndulu,

chifukwa uchimo umene wafalikira mʼdziko lonse

ndi wochokera kwa aneneri a ku Yerusalemuwa.”

16Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Musamvere zimene aneneri amenewa akulosera kwa inu;

zomwe aloserazo nʼzachabechabe.

Iwo akungoyankhula za masomphenya a mʼmitima mwawo basi,

osati zochokera kwa Yehova.

17Iwo amapita ndi kumakawuza amene amandinyoza Ine kuti,

‘zinthu zidzakuyenderani bwino.’

Kwa iwo amene amawumirira kutsata zofuna za mitima yawo amakawawuza kuti,

‘palibe choyipa chimene chidzakugwereni.’ ”

18Ine ndikuti, “Koma ndani wa iwo amene anakhalapo mu msonkhano wa Yehova?

Ndani anaonapo kapena kumvapo mawu ake?

Ndani mwa iwo analabadirako za mawu ake ndi kuwamvera?

19Taonani ukali wa Yehova

uli ngati chimphepo chamkuntho,

inde ngati namondwe.

Ndipo adzakantha mitu ya anthu oyipa.

20Mkwiyo wa Yehova sudzaleka

mpaka atachita zonse zimene

anatsimikiza mu mtima mwake.

Mudzazizindikira bwino zimenezi

masiku akubwerawa.”

21Yehova anati, “Ine sindinatume aneneri amenewa,

komabe iwo athamanga uku ndi uku kulalikira uthenga wawo;

Ine sindinawayankhule,

komabe iwo ananenera.

22Iwo akanakhala pa msonkhano wanga

ndiye kuti akanamayankhula mawu anga kwa anthu anga.

Komanso bwenzi atawachotsa anthu anga mʼnjira zawo zoyipa

kuti aleke machimo awo.”

23Yehova akuti, “Kodi ndimakhala Mulungu pokhapokha ndikakhala pafupi,

ndiye sindine Mulungu?

24Kodi wina angathe kubisala

Ine osamuona?”

“Kodi Ine sindili ponseponse kumwamba ndi dziko lapansi?”

Akutero Yehova.

25“Ndamva zimene aneneri akuyankhula. Iwo amalosera zabodza mʼdzina langa nʼkumati, ‘Ndalota! Ndalota!’ 26Kodi zabodzazi zidzakhalabe mʼmitima ya aneneriwa mpaka liti? Iwotu amalosera zonyenga za mʼmitima yawo. 27Aneneriwa amakhulupirira kuti anthu anga adzayiwala mawu anga akamamva za maloto awo amene amayankhulana ngati mmene anachitira makolo awo popembedza Baala. 28Mneneri amene ali ndi maloto afotokoze malotowo. Koma iye amene ali ndi mawu anga alalikire mawuwo mokhulupirika. Kodi phesi lingafanane ndi chimanga? 29Kodi suja mawu anga amatentha ngati moto? Suja mawu anga amaphwanya monga ichitira nyundo kuphwanya miyala?” Akutero Yehova.

30Yehova akuti, “Nʼchifukwa chake, Ine ndikudana nawo aneneri amene amaberana okhaokha mawu nʼkumati mawuwo ndi a Yehova.” 31Yehova akuti, “Inde, Ine ndikudana ndi aneneri amene amakonda kuyankhula zabodza nʼkumanena kuti, ‘Amenewa ndi mawu a Yehova.’ ” 32Yehova akuti, “Ndithudi, Ine ndikudana ndi aneneri a maloto abodzawa. Iwo amafotokoza malotowo nʼkumasocheretsa anthu anga ndi bodza lawo losachita nalo manyazilo, chonsecho Ine sindinawatume kapena kuwalamula. Iwo sathandiza anthuwa ndi pangʼono pomwe,” akutero Yehova.

Uthenga Wabodza ndi Aneneri Abodza

33Yehova anawuza Yeremiya kuti, “Anthu awa, kapena mneneri, kapenanso wansembe, akakufunsa kuti, ‘Kodi uthenga wolemetsa wa Yehova ukuti chiyani?’ uwawuze kuti, ‘Inuyo ndinu katundu wolemetsa Yehova, ndipo adzakutayani.’ 34Ngati mneneri kapena wansembe kapenanso munthu wina aliyense anena kuti, ‘Uthenga wolemetsa wa Yehova ndi uwu,’ Ine ndidzalanga munthu ameneyo pamodzi ndi banja lake. 35Koma chimene aliyense wa inu azifunsa kwa mnzake kapena mʼbale wake ndi ichi: ‘Kodi Yehova wayankha chiyani?’ kapena ‘Yehova wayankhula chiyani?’ 36Koma musanenenso kuti ‘nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ chifukwa mawu a munthu aliyense ndiwo uthenga wa iye mwini, kotero kuti inu mumakhotetsa mawu a Mulungu wamoyo, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wathu. 37Tsono iwe Yeremiya udzamufunse mneneri kuti, ‘Kodi Yehova wakuyankha chiyani?’ kapena, ‘Kodi Yehova wayankhula chiyani?’ 38Ngati mudzanena kuti, ‘Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ ndiye tsono Yehova akuti, ‘Popeza mwagwiritsa ntchito mawu akuti: Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova, mawu amene ndinakuletsani kuti musawatchule, 39ndiye kuti Ine ndidzakunyamulani ngati katundu nʼkukuponyani kutali. Ndidzakuchotsani pamaso panga, inuyo pamodzi ndi mzinda umene ndinakupatsani inu ndi makolo anu. 40Ndidzakunyozani mpaka muyaya. Ndidzakuchititsani manyazi osayiwalika.’ ”

Korean Living Bible

예레미야 23:1-40

오실 메시아

1여호와께서 말씀하신다. “내 목장의 양떼를 해치고 흩어 버리는 목자 들에게 화가 있을 것이다.

2이스라엘의 하나님 나 여호와가 내 백성을 기르는 목자들에게 말한다. 너희는 나의 양떼를 흩어 버리고 몰아내며 돌보지 않았다. 그러므로 너희가 행한 악에 대하여 내가 너희에게 벌을 내리겠다.

3내가 세계 여러 나라로 흩어 버린 남은 내 백성을 다시 모아 고국으로 돌아오게 할 것이니 그들이 많은 자녀를 낳고 번성할 것이다.

4내가 그들을 돌볼 목자들을 세워 그들이 다시는 두려워하거나 놀라거나 그 수가 줄어드는 일이 없도록 하겠다. 이것은 나 여호와의 말이다.”

5여호와께서 다시 말씀하신다. “때가 되면 내가 다윗의 후손 가운데 한 23:5 원문에는 ‘의로운 가지’의로운 자를 일으킬 것이다. 그가 왕이 되어 지혜롭게 다스리며 세상에서 공정하고 옳은 일을 행할 것이다.

6그때 유다는 구원을 얻고 이스라엘은 안전하게 살 것이며 그의 이름은 ‘여호와 우리의 의’ 라고 불려질 것이다.

7“그때 사람들은 ‘이스라엘 백성을 이집트에서 인도해 내신 살아 계신 여호와’ 란 말로 맹세하지 않고

8‘이스라엘 백성을 북쪽 땅과 그들이 쫓겨간 모든 나라에서 인도해 내신 살아 계신 여호와’ 란 말로 맹세할 것이며 그들은 자기들의 땅에서 살게 될 것이다.”

거짓 예언자들

9거짓 예언자들 때문에 내 마음이 상하고 내 모든 뼈가 떨리는구나. 내가 여호와와 그의 거룩한 말씀 때문에 술취한 사람처럼 되었고 포도주에 사로잡힌 사람처럼 되었다.

10이 땅에 간음하는 자들이 가득하구나. 여호와의 저주로 땅이 슬퍼하고 광야의 푸른 풀들이 마르고 있으니 이것은 예언자들이 악을 행하고 그들의 권력을 남용하기 때문이다.

11여호와께서 말씀하신다. “예언자들과 제사장들이 다 더럽혀졌으니 내가 성전에서도 그들의 악을 발견하였다.

12그러므로 그들의 길이 미끄럽고 어두워서 그들은 넘어지고 말 것이다. 그들을 벌할 때가 되면 내가 그들에게 재앙을 내리겠다. 이것은 나 여호와의 말이다.

13“내가 사마리아 예언자들 가운데서도 역겨운 일을 보았다. 그들이 바알의 이름으로 예언하고 내 백성 이스라엘을 잘못된 길로 인도하였다.

14나는 또 예루살렘 예언자들 가운데서도 끔찍한 일을 보았다. 그들은 간음하고 거짓말할 뿐만 아니라 악을 행하는 자를 그 죄에서 돌아서게 하지 않고 오히려 그들을 격려하고 칭찬하였다. 그래서 그들은 나에게 소돔 사람과 같고 예루살렘 주민은 고모라 사람과 같다.

15그러므로 전능한 나 여호와가 그 예언자들에 대하여 말한다. 보라, 내가 그들에게 쓴 것을 먹이고 독물을 마시게 하겠다. 이것은 이 땅을 악으로 물들게 한 것이 바로 그들이기 때문이다.”

16전능하신 여호와께서 말씀하신다. “너희는 예언자들이 하는 말을 듣지 말아라. 그들은 너희에게 헛된 희망을 불어넣어 주고 있다. 그들의 예언은 자기들 멋대로 생각해 낸 것이며 나 여호와의 입에서 나온 것이 아니다.

17그들은 나를 멸시하는 자들에게 언제나 ‘여호와께서 말씀하셨다. 너희는 평안할 것이다’ 하며 또 자기 마음의 악한 고집대로 행하는 자들에게는 ‘아무런 해도 너희에게 미치지 않을 것이다’ 하고 말한다.

18그러나 이 예언자들 중에 누가 나 23:18 또는 ‘여호와의 회의에 참예하여’여호와의 은밀한 생각을 알며 내 말을 귀담아 듣고 이해하였는가?

19보라, 나 여호와가 폭풍과 회오리바람 같은 분노로 악인들의 머리를 칠 것이다.

20나 여호와의 분노는 내 마음에 뜻한 것을 다 이룰 때까지 그치지 않을 것이니 앞으로 너희가 이것을 분명히 깨달을 것이다.

21이 예언자들은 내가 보내지도 않았는데 돌아다니며, 내가 그들에게 아무 말도 하지 않았는데 예언하였다.

22그들이 만일 23:22 또는 ‘나의 회의에 참예하였더면’나의 은밀한 생각을 알았더라면 내 백성들에게 내 말을 선포하여 그들을 악한 길과 악한 행위에서 돌아서게 했을 것이다.”

23여호와께서 말씀하신다. “나는 한 곳에만 있는 하나님이 아니라 어디든지 있는 하나님이다.

24내가 볼 수 없도록 은밀한 곳에 숨을 자가 누구냐? 23:24 또는 ‘나는 천지에 충만하지 아니하냐?’나는 하늘과 땅 어느 곳에나 존재한다는 것을 모르느냐?

25나는 내 이름으로 거짓을 예언하는 자들이 ‘내가 꿈을 꾸었다. 내가 꿈을 꾸었다’ 하고 말하는 소리를 들었다.

26이 거짓 예언자들이 언제까지 이런 식으로 예언할 것인가? 그들은 자기들 멋대로 지어낸 거짓말로 예언하는 자들이다.

27그들은 자기 조상들이 바알 때문에 나를 잊어버린 것처럼 자기들이 서로 말하는 꿈 이야기로 내 백성들이 나를 잊도록 하려고 한다.

28꿈을 꾼 예언자는 그 꿈을 말하게 하고 내 말을 받은 예언자는 내 말을 성실히 말하게 하라. 겨와 알곡이 어찌 같겠느냐?

29내 말이 불 같지 않은가? 바위를 쳐서 부수는 망치 같지 않은가?

30-31그러므로 자기들끼리 서로 말을 받아 ‘여호와께서 말씀하셨다’ 하고 혀를 놀리는 예언자들을 내가 치겠다.

32나 여호와가 말한다. 보라, 거짓된 꿈을 말하고 거짓말과 헛된 자랑으로 내 백성을 미혹하는 자를 내가 칠 것이다. 나는 그들을 보내지도 않았고 명령하지도 않았다. 그들은 이 백성들에게 아무런 도움도 되지 않는다. 이것은 나 여호와의 말이다.”

33여호와께서 나에게 말씀하셨다. “이 백성이나 예언자나 제사장이 너에게 ‘여호와의 엄한 말씀이 무엇이냐?’ 하고 묻거든 너는 그들에게 이렇게 대답하라: 너희가 여호와께 짐이 되므로 여호와께서 너희를 버리실 것이다.

34예언자나 제사장이나 그 밖에 누구든지 ‘여호와의 엄한 말씀’ 이란 말을 함부로 사용하면 여호와께서 그 사람과 그의 가족을 벌하실 것이다.

35너희는 자기 친구들과 친척들에게 ‘여호와께서 무엇이라고 대답하셨는가? 여호와께서 무엇이라고 말씀하셨는가?’ 하고 서로 물을 수는 있다.

36그러나 너희는 ‘여호와의 엄한 말씀’ 이란 말을 입 밖에 내서는 안 된다. 만일 너희가 그렇게 하면 각자 자기가 한 말이 여호와께서 하신 말씀처럼 되어 살아 계시는 하나님, 곧 전능하신 여호와 우리 하나님의 말씀을 그르치게 될 것이다.

37“예레미야야, 너는 예언자들에게 ‘여호와께서 너희에게 무엇이라고 대답하셨으며 너희에게 무엇이라고 말씀하셨는가?’ 하고 물어 보아라.

38내가 그들에게 ‘여호와의 엄한 말씀’ 이란 말을 사용하지 말라고 명령하였으나 그들은 계속 그 말을 쓰고 있다.

39그러므로 내가 그들을 아주 잊어버리고 그들과 그 조상들에게 준 이 성과 함께 그들을 내 앞에서 내쫓아

40영원히 씻을 수 없는 수치와 모욕을 당하게 하겠다.”