Yeremiya 2 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 2:1-37

Aisraeli Asiya Mulungu

1Yehova anandiwuza kuti, 2“Pita ukalengeze kwa anthu a ku Yerusalemu kuti Yehova akuti,

“ ‘Ine ndikukumbukira mmene umakhulupirikira pa unyamata wako,

mmene unkandikondera ngati momwe amachitira mkwatibwi,

mmene unkanditsata mʼchipululu muja;

mʼdziko losadzalamo kanthu.

3Israeli anali wopatulika wa Yehova,

anali ngati zipatso zake zoyamba kucha pa nthawi yokolola;

onse amene anamuzunza anapezeka kuti ndi olakwa

ndipo mavuto anawagwera,’ ”

akutero Yehova.

4Imvani mawu a Yehova, inu zidzukulu za Yakobo,

inu mafuko onse a Israeli.

5Yehova akuti,

“Kodi makolo anu anandipeza nʼcholakwa chanji,

kuti andithawe?

Iwo anatsata milungu yachabechabe,

nawonso nʼkusanduka achabechabe.

6Iwo sanafunse nʼkomwe kuti, ‘Kodi Yehova ali kuti,

amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto

natitsogolera mʼchipululu mʼdziko lowuma

ndi lokumbikakumbika,

mʼdziko lopanda mvula ndi la mdima,

dziko limene munthu sadutsamo ndipo simukhala munthu aliyense?’

7Ndinakufikitsani ku dziko lachonde

kuti mudye zipatso zake ndi zabwino zake zina.

Koma inu mutafika munaliyipitsa dziko langa

ndi kusandutsa cholowa changa kukhala chonyansa.

8Ansembe nawonso sanafunse kuti,

‘Yehova ali kuti?’

Iwo amene amaphunzitsa malamulo sanandidziwe;

atsogoleri anandiwukira.

Aneneri ankanenera mʼdzina la Baala,

ndi kutsatira mafano achabechabe.

9“Chifukwa chake Ine ndidzakuyimbaninso mlandu,”

akutero Yehova.

“Ndipo ndidzayimbanso mlandu zidzukulu zanu.

10Pitani kumadzulo ku chilumba cha Kitimu, ndipo mukaone,

tumizani anthu ku Kedara kuti akafufuze bwino;

ndipo muona kuti zinthu zoterezi sizinachitikepo nʼkale lomwe:

11Kodi ulipo mtundu wa anthu uliwonse umene unasinthapo milungu yake?

(Ngakhale kuti si milungu nʼkomwe).

Koma anthu anga asinthitsa Mulungu wawo waulemerero

ndi mafano achabechabe.

12Inu mayiko akumwamba, dabwani ndi zimenezi,

ndipo njenjemerani ndi mantha aakulu,”

akutero Yehova.

13“Popeza anthu anga achita machimo awiri:

Andisiya Ine

kasupe wa madzi a moyo,

ndi kukadzikumbira zitsime zawo,

zitsime zongʼaluka, zomwe sizingathe kusunga madzi.

14Israeli si wantchito kapena kapolo wobadwira mʼnyumba, ayi.

Nanga nʼchifukwa chiyani amuwononga chotere?

15Adani ake abangulira

ndi kumuopseza ngati mikango.

Dziko lake analisandutsa bwinja;

mizinda yake anayitentha popanda wokhalamo.

16Ndiponso Aigupto a ku Mefisi ndi a ku Tapanesi

akuphwanyani mitu.

17Zimenezitu zakuchitikirani

chifukwa munasiya Yehova Mulungu wanu

pamene Iye ankakutsogolerani pa njira yanu?

18Tsopano mudzapindula chiyani mukapita ku Igupto,

kukamwa madzi a mu Sihori?

Ndipo mudzapindulanji mukapita ku Asiriya,

kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?

19Kuyipa kwanuko kudzakulangani;

kubwerera mʼmbuyo kwanuko kudzakutsutsani.

Tsono ganizirani bwino,

popeza ndi chinthu choyipa

kundisiya Ine Yehova Mulungu wanu;

ndi chinthu chowawa ndithu kusandiopa Ine Mulungu wanu.

Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.

20“Kuyambira kalekale inu munathyola goli lanu

ndi kudula msinga zanu;

munanena kuti, ‘Sitidzakutumikirani!’

Ndithudi, inu mwakhala ngati mkazi wachiwerewere.

Mukupembedza milungu ina pa phiri lililonse lalitali

ndiponso pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.

21Ine ndinakudzala iwe ngati mtengo wampesa wosankhika;

unali mpesa wabwino kwambiri ndi wodalirika.

Nanga nʼchifukwa chiyani wasanduka mpesa

wachabechabe wonga wa kutchire?

22Ngakhale utasamba ndi soda

kapena kusambira sopo wambiri,

kuthimbirira kwa machimo ako kumaonekabe pamaso panga,”

akutero Ambuye Yehova.

23“Iwe ukunena bwanji kuti, ‘Ine sindinadziyipitse;

sindinatsatire Abaala’?

Takumbukira mmene unkandichimwira mʼchigwa muja;

zindikira bwino zomwe wachita.

Iwe uli ngati ngamira yayikazi yaliwiro

yomangothamanga uku ndi uku,

24wakhala ngati mbidzi yozolowera mʼchipululu,

yonka ninunkhiza pa nthawi yachisika.

Ndani angayiretse chilakolako chakecho?

Mphongo iliyonse yoyikhumba sidzavutika.

Pa nthawi yachisika chakecho mphongoyo idzayipeza.

25Iwe usathamange, nsapato zingakuthere kuphazi

ndi kukhosi kwako kuwuma ndi ludzu.

Koma unati, ‘Zamkutu!

Ine ndimakonda milungu yachilendo,

ndipo ndidzayitsatira.’

26“Monga momwe mbala imachitira manyazi pamene yagwidwa,

moteronso nyumba ya Israeli idzachita manyazi;

Aisraeliwo, mafumu ndi akuluakulu awo,

ansembe ndi aneneri awo.

27Iwo amawuza mtengo kuti, ‘Iwe ndiwe abambo athu,’

ndipo amawuza mwala kuti, ‘Iwe ndiye amene unatibala.’

Iwo andifulatira Ine,

ndipo safuna kundiyangʼana;

Koma akakhala pa mavuto amati,

‘Bwerani mudzatipulumutse!’

28Nanga ili kuti milungu yanu imene munadzipangira nokha?

Ibweretu ngati ingathe kukupulumutsani

pamene muli pamavuto!

Inu anthu a ku Yuda,

milungu yanu ndi yambiri kuchuluka kwake ngati mizinda yanu.

29“Kodi mukundizengeranji mlandu?

Nonse mwandiwukira,”

akutero Yehova.

30“Ine ndinalanga anthu ako popanda phindu;

iwo sanaphunzirepo kanthu.

Monga mkango wolusa,

lupanga lanu lapha aneneri anu.

31“Inu anthu a mʼbado uno, ganizirani bwino mawu a Yehova:

“Kodi Ine ndinakhalapo ngati chipululu kwa Israeli

kapena ngati dziko la mdima wandiweyani?

Chifukwa chiyani anthu anga akunena kuti, ‘Ife tili ndi ufulu omayendayenda;

sitidzabweranso kwa Inu’?

32Kodi namwali amayiwala zokongoletsera zake,

kapena kuyiwala zovala zake za ukwati?

Komatu anthu anga andiyiwala

masiku osawerengeka.

33Mumadziwa bwino njira zopezera zibwenzi!

Choncho ngakhale akazi oyipa omwe mumawaphunzitsa njira zanu.

34Ngakhale pa zovala zako anthu amapezapo

magazi a anthu osauka osalakwa.

Anthuwo simunawapeze akuthyola nyumba.

Komabe ngakhale zinthu zili chomwechi,

35inu mukunena kuti, ‘Ndife osalakwa,

sadzatikwiyira.’

Ndidzakuyimbani mlandu

chifukwa mukunena kuti, ‘Ife sitinachimwe.’

36Chifukwa chiyani

mukunkabe nimusinthasintha njira zanu?

Aigupto adzakukhumudwitsani

monga momwe Asiriya anakuchititsani manyazi.

37Mudzachokanso kumeneko

manja ali kunkhongo.

Popeza Ine Yehova ndawakana anthu amene munkawadalira,

choncho sadzakuthandizani konse.

New International Reader’s Version

Jeremiah 2:1-37

Israel Deserts the Lord

1A message from the Lord came to me. The Lord said, 2“Go. Announce my message to the people in Jerusalem. I want everyone to hear it. Tell them,

“Here is what the Lord says.

“ ‘I remember how faithful you were to me when you were young.

You loved me as if you were my bride.

You followed me through the desert.

Nothing had been planted there.

3Your people were holy to me.

They were the first share of my harvest.

All those who destroyed them were held guilty.

And trouble came to their enemies,’ ”

announces the Lord.

4People of Jacob, hear the Lord’s message.

Listen, all you tribes of Israel.

5The Lord says,

“What did your people of long ago find wrong with me?

Why did they wander so far away from me?

They worshiped worthless statues of gods.

Then they themselves became worthless.

6They did not ask, ‘Where is the Lord?

He brought us up out of Egypt.

He led us through a dry and empty land.

He guided us through deserts and deep valleys.

It was a land of total darkness where there wasn’t any rain.

No one lived or traveled there.’

7But I brought you into a land that has rich soil.

I gave you its fruit and its finest food.

In spite of that, you made my land impure.

You turned it into something I hate.

8The priests did not ask,

‘Where is the Lord?’

Those who taught my law did not know me.

The leaders refused to obey me.

The prophets prophesied in the name of Baal.

They worshiped worthless statues of gods.

9“So I am bringing charges against you again,”

announces the Lord.

“And I will bring charges against your children’s children.

10Go over to the coasts of Cyprus and look.

Send people to the land of Kedar and have them look closely.

See if there has ever been anything like this.

11Has a nation ever changed its gods?

Actually, they are not even gods at all.

But my people have traded away their glorious God.

They have traded me for worthless statues of gods.

12Sky above, be shocked over this.

Tremble with horror,”

announces the Lord.

13“My people have sinned twice.

They have deserted me,

even though I am the spring of water that gives life.

And they have dug their own wells.

But those wells are broken.

They can’t hold any water.

14Are you people of Israel servants?

You were not born as slaves, were you?

Then why have you been carried off like stolen goods?

15Lions have roared.

They have growled at you.

They have destroyed your land.

Your towns are burned and deserted.

16The men of Memphis and Tahpanhes

have cracked your skulls.

17Haven’t you brought this on yourselves?

I am the Lord your God, but you deserted me.

You left me even while I was leading you.

18Why do you go to Egypt

to drink water from the Nile River?

Why do you go to Assyria

to drink from the Euphrates River?

19You will be punished because you have sinned.

You will be corrected for turning away from me.

I am the Lord your God.

If you desert me, bad things will happen to you.

If you do not respect me, you will suffer bitterly.

I want you to understand that,”

announces the Lord who rules over all.

20“Long ago you broke off the yoke I put on you.

You tore off the ropes I tied you up with.

You said, ‘I won’t serve you!’

In fact, on every high hill

you lay down like a prostitute.

You worshiped other gods under every green tree.

21You were like a good vine when I planted you.

You were a healthy plant.

Then how did you turn against me?

How did you become a bad, wild vine?

22You might wash yourself with soap.

You might use plenty of strong soap.

But I can still see the stains your guilt covers you with,”

announces the Lord and King.

23“You say, ‘I am “clean.”

I haven’t followed the gods that are named Baal.’

How can you say that?

Remember how you acted in the valley.

Consider what you have done.

You are like a female camel running quickly here and there.

24You are like a wild donkey that lives in the desert.

She smells the wind when she longs for a mate.

Who can hold her back?

The males that run after her do not need to wear themselves out.

At mating time they will easily find her.

25Do not run after other gods

until your sandals are worn out and your throat is dry.

But you said, ‘It’s no use!

I love those gods.

I must go after them.’

26“A thief is dishonored when he is caught.

And you people of Israel are filled with shame.

Your kings and officials are dishonored.

So are your priests and your prophets.

27You say to a piece of wood, ‘You are my father.’

You say to a stone, ‘You are my mother.’

You have turned your backs to me.

You refuse to look at me.

But when you are in trouble, you say,

‘Come and save us!’

28Then where are the gods you made for yourselves?

Let them come when you are in trouble!

Let them save you if they can!

Judah, you have as many gods

as you have towns.

29“Why do you bring charges against me?

All of you have refused to obey me,”

announces the Lord.

30“I punished your people. But it did not do them any good.

They did not pay attention when they were corrected.

You have killed your prophets by swords.

You have swallowed them up like a hungry lion.

31“You who are now living, consider my message. I am saying,

“Have I been like a desert to Israel?

Have I been like a land of deep darkness?

Why do my people say, ‘We are free to wander.

We won’t come to you anymore’?

32Does a young woman forget all about her jewelry?

Does a bride forget her wedding jewels?

But my people have forgotten me

more days than anyone can count.

33You are very skilled at chasing after love!

Even the worst of women can learn from how you act.

34The blood of those you have killed is on your clothes.

You have destroyed poor people who were not guilty.

You did not catch them in the act of breaking in.

In spite of all this,

35you say, ‘I’m not guilty of doing anything wrong.

The Lord isn’t angry with me.’

But I will judge you.

That’s because you say, ‘I haven’t sinned.’

36Why do you keep on

changing your ways so much?

Assyria did not help you.

And Egypt will not help you either.

37So you will also leave Egypt

with your hands tied together above your heads.

I have turned my back on those you trust.

They will not help you.