Rute 1 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Rute 1:1-22

Naomi ndi Rute

1Mu nthawi imene oweruza ankalamulira Israeli, munali njala mʼdziko, ndipo munthu wina wa ku Betelehemu mʼdziko la Yuda anapita pamodzi ndi mkazi wake ndi ana ake aamuna awiri, kukakhala ku Mowabu kwa nthawi yochepa. 2Dzina la munthuyo linali Elimeleki, dzina la mkazi wake linali Naomi, ndipo mayina a ana awo aamuna anali Maaloni ndi Kiliyoni. Iwo anali Aefurati ochokera ku Betelehemu ku Yuda. Ndipo anapita kukakhala ku Mowabu.

3Kenaka Elimeleki, mwamuna wake wa Naomi anamwalira ndipo Naomiyo anatsala ndi ana ake aamuna awiri aja.

4Iwo anakwatira akazi a Chimowabu; wina dzina lake Oripa ndi wina Rute. Atakhala kumeneko pafupifupi zaka khumi, 5Maloni ndi Kiliyoni anamwaliranso kotero kuti Naomi anatsala yekha wopanda ana ake awiri aja ndi mwamuna wake.

6Naomi ndi apongozi ake awiri aja ananyamuka kubwerera kwawo kuchokera ku Mowabu popeza anali atamva ali ku Mowabuko kuti Yehova anakomera mtima anthu ake ndi kuwapatsa chakudya.

7Naomi pamodzi ndi apongozi ake awiri aja anachoka kumene ankakhala ndi kuyamba ulendo obwerera kwawo ku Yuda.

8Kenaka Naomi anati kwa apongozi ake awiri aja, “Bwererani, aliyense kwa amayi ake. Yehova akukomereni mtima, monga munachita ndi malemu aja ndi ine ndemwe.

9“Yehova akuthandizeni kuti aliyense wa inu apeze pokhala pabwino komanso mwamuna.” Kenaka anawapsompsona koma awiriwo analira mokweza.

10Ndipo anati kwa Naomi, “Ife tipita nawo kwa anthu akwanu.”

11Koma Naomi anati, “Bwererani kwanu ana anga. Chifukwa chiyani mukufuna kupita ndi ine? Kodi ine ndingaberekenso ana ena kuti akhale amuna anu? 12Bwererani kwanu ana anga muzipita kwanu. Ine ndakalamba kwambiri kotero kuti sindingakwatiwenso. Ngakhale ndikananena kuti ndili nacho chikhulupiriro, ngakhale ndikanakhala ndi mwamuna usiku uno, ndipo nʼkubala ana aamuna, 13kodi inu mukanadikira kuti akule? Kodi mukanakhalabe osakwatiwa kudikira iwowo? Ayi ana anga. Zimenezi zikundiwawa kwambiri kuposa inu, chifukwa ndi ineyo amene Yehova wafuna kuti ndizunzike.”

14Atamva zimenezi analiranso kwambiri, ndipo Oripa anapsompsona apongozi ake nawatsanzika, koma Rute anakakamirabe.

15Naomi anati “Taona, mʼbale wako wabwerera kwawo kwa anthu ake ndi kwa milungu yake. Bwerera nawenso umulondole mʼbale wako.”

16Koma Rute anayankha kuti, “Musandikakamize kuti ndikusiyeni kapena kuti ndibwerere osakutsatani. Kumene inu mupite ine ndipita komweko, ndipo kumene mukakhale inenso ndikakhala komweko. Abale anu adzakhala abale anga ndipo Mulungu wanu adzakhala Mulungu wanga. 17Kumene mukafere inenso ndidzafera komweko ndipo komweko ndikayikidwa mʼmanda. Yehova andichite choyipa chingakule motani, ngati china chingatirekanitse ife kupatula imfa.”

18Naomi atazindikira kuti Rute watsimikiza kupita naye, analeka kumukakamiza.

19Choncho amayi awiriwo anapitiriza ulendo wawo mpaka anakafika ku Betelehemu. Pamene ankafika mu Betelehemu, anthu onse a mʼmudzimo anatekeseka chifukwa cha iwowo ndipo amayi ambiri ankanena kuti, “Kodi uyu nʼkukhala Naomi?”

20Iye anawawuza kuti, “Musanditchenso Naomi. Muzinditchula ine kuti Mara, chifukwa Wamphamvuzonse wandizunza kwambiri. 21Ine ndinapita wolemera, koma Yehova wabwera nane wopanda kanthu. Nanga munditchulirenji Naomi pamene Yehova wandisautsa. Wamphamvuzonse uja wandigwetsera mavuto owawa.”

22Naomi anabwerera kuchoka ku dziko la Mowabu pamodzi ndi Rute mpongozi wake. Ndipo anafika ku Betelehemu nthawi yoyamba kukolola barele.

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Ruthu 1:1-22

Naomi Na Ruthu

11:1 Amu 2:16-18; Mwa 12:10; 35:19; 36:35; 47:4; 2Fal 6:25; Hag 1:11; Za 105:16; Kum 28:38; 1Fal 18:2; Mik 5:2Wakati Waamuzi walipotawala Israeli, kulikuwa na njaa katika nchi. Mtu mmoja kutoka nchi ya Bethlehemu ya Yuda, pamoja na mke wake na wanawe wawili, akaenda kuishi katika nchi ya Moabu. 21:2 Rut 2:1; 4:3; Amu 3:30; 1Sam 16:18; Mwa 35:16-19Mtu huyu aliitwa Elimeleki, mkewe aliitwa Naomi, na hao wanawe wawili waliitwa Maloni na Kilioni. Walikuwa Waefrathi kutoka Bethlehemu ya Yuda. Wakaenda katika nchi ya Moabu, wakaishi huko.

3Elimeleki mumewe Naomi akafa, hivyo Naomi akabaki na wanawe wawili. 41:4 1Fal 11:1; Mt 1:5; Rut 4:13; Ezr 9:2; Neh 13:23Nao wakaoa wanawake Wamoabu, jina la mmoja aliitwa Orpa, na wa pili aliitwa Ruthu. Baada ya kama miaka kumi, 51:5 Rut 2:11Maloni na Kilioni pia wakafa. Basi Naomi akabaki hana mume wala wanawe wawili.

61:6 Mwa 11:31; 36:35; 38:16; 50:24; Kut 4:31; Yer 29:10; Sef 2:7; Za 80:14; Zek 10:3; Lk 1:68; 7:16; Mwa 28:20; 48:15; Mit 30:8; Isa 55:10; Mt 6:11; Za 132:15Aliposikia akiwa huko Moabu kwamba Bwana amewasaidia watu wake kwa kuwapa chakula, Naomi na wakweze wakajiandaa kurudi nyumbani. 7Yeye na wakweze wawili wakaondoka pale walipokuwa wakiishi na kushika njia kurudi nchi ya Yuda.

81:8 Mwa 38:11; 19:19; Yos 24:25; 2Tim 1:16Ndipo Naomi akawaambia wale wakwe zake wawili, “Rudini, kila mmoja wenu nyumbani kwa mama yake. Bwana na awatendee fadhili kama mlivyowatendea hao waliofariki, na pia mimi. 91:9 Rut 3:1; Mwa 27:27, 38; 29:11; Hes 25:6Bwana na amjalie kila mmoja wenu maisha mema nyumbani kwa mume mwingine.”

Kisha akawabusu, nao wakalia kwa sauti kubwa, 10wakamwambia, “Tutarudi pamoja na wewe nyumbani kwa watu wako.”

111:11 Mwa 38:11; Kum 25:5Lakini Naomi akasema, “Rudini nyumbani, binti zangu. Kwa nini mnifuate? Je, mimi nitaweza tena kuwa na wana wengine ambao wataweza kuwaoa ninyi? 12Rudini nyumbani, binti zangu; mimi ni mzee kiasi kwamba siwezi kumpata mume mwingine. Hata kama ningefikiria kuwa bado kuna tumaini kwangu, hata kama ningekuwa na mume usiku huu na kuwazaa wana, 131:13 Mwa 38:11; Kut 1:14; 15:23; 1Sam 30:6; Ay 19:21; Za 32:4; 38:2; Amu 2:15; 4:5je, mngesubiri mpaka wakue? Mngebakia bila kuolewa mkiwasubiri? La, hasha, binti zangu. Nimepata uchungu kuliko ninyi, kwa sababu mkono wa Bwana umekuwa kinyume nami!”

141:14 Rut 2:11; 3:1; Mik 7:6; Mit 17:17; 18:24; Yn 6:66-69; Ebr 10:39; Mwa 31:28; Kum 10:20Kisha wakalia tena kwa sauti. Orpa akambusu mama mkwe wake, akaenda zake, lakini Ruthu akaambatana naye.

151:15 Kum 25:7; Yos 24:14; Amu 11:24Naomi akamwambia, “Tazama, mwenzako anarejea kwa watu wake na kwa miungu yake. Rudi pamoja naye.”

161:16 2Fal 2:2; Yos 24:15; Mwa 24:58; Za 45:10; Rut 2:11-12Lakini Ruthu akajibu, “Usinisihi nikuache au niache kukufuata. Utakakokwenda nami nitakwenda, na wewe utakapoishi nitaishi. Watu wako watakuwa watu wangu, na Mungu wako atakuwa Mungu wangu. 171:17 1Sam 3:17; 14:44; 20:13; 25:22; 1Fal 2:23; 19:2; 20:10; 2Sam 3:9; 19:13; 2Fal 6:31; 15:21Pale utakapofia nami nitafia hapo, na papo hapo nitazikwa. Bwana na aniadhibu vikali, kama kitu kingine chochote kitanitenga nawe isipokuwa kifo.” 181:18 Mdo 21:14Naomi alipotambua kwamba Ruthu amenuia kufuatana naye, hakuendelea kumsihi tena.

191:19 Amu 17:7; Isa 23:7; Mt 21:10; Mao 2:15Kwa hiyo hao wanawake wawili wakaondoka, wakafika Bethlehemu. Walipofika Bethlehemu, mji mzima ulitaharuki, wanawake wakashangaa, wakasema, “Huyu aweza kuwa ni Naomi?”

201:20 Mwa 15:1; 17:1; Za 91:1; Kut 6:3; Ay 6:4Akawaambia, “Msiniite tena Naomi,1:20 Naomi maana yake Wa Kupendeza, Wa Kufurahisha. niiteni Mara,1:20 Mara maana yake Chungu. kwa sababu Mwenyezi1:20 Mwenyezi hapa ina maana ya Shaddai kwa Kiebrania. amenitendea mambo machungu sana. 211:21 Ay 1:21; 30:11; Za 88:7; Isa 53:4Mimi niliondoka hali nimejaa, lakini Bwana amenirudisha mtupu. Kwa nini kuniita Naomi? Bwana amenitendea mambo machungu; Mwenyezi ameniletea msiba.”

221:22 Rut 2:2-6, 21; 4:5, 10; Kut 9:31; Mwa 11:31; Law 19:9; 2Sam 21:9Kwa hiyo Naomi alirudi pamoja na Ruthu Mmoabu mkwe wake, nao wakafika Bethlehemu mwanzoni mwa kuvuna shayiri.