Oweruza 17 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 17:1-13

Mafuno a Mika

1Munthu wina dzina lake Mika wochokera ku dziko la mapiri la Efereimu anawuza amayi ake kuti 2“Ndinamva inu mukutemberera munthu amene anaba ndalama zanu zasiliva 1,100. Ndalamazo zili ndi ine, ndinatenga ndine.”

Pamenepo amayi akewo anati, “Yehova akudalitse mwana wanga!”

3Choncho Mika anabweza ndalama 1,100 za siliva kwa amayi ake, ndipo amayi akewo anati, “Ine ndapatulira Yehova ndalama za silivazi kuti mwana wanga aseme fano ndi kulikuta ndi siliva. Ndiye tsopano ndikubwezera ndalamazo.”

4Tsono Mika atabweza ndalama zija kwa amayi ake, iwo anatengapo ndalama za siliva 200 namupatsa mmisiri wosula siliva. Iye anakonza fano, nasungunula siliva uja ndi kulikutira fano lija. Ndipo Mika anayika fanolo mʼnyumba mwake.

5Mikayu anali ndi kachisi, ndipo anapanga efodi ndi mafano otchedwa terafimu. Anapatula mwana wake mmodzi kuti akhale wansembe. 6Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense amachita zomwe zinamukomera.

7Ku Betelehemu mʼdziko la Yuda kunali mnyamata wina amene anali wa fuko la Levi. 8Iyeyu anachoka mu mzinda wa Betelehemu uja ku Yuda kukafuna malo ena okhala. Akuyenda, anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ku nyumba ya Mika.

9Tsono Mika anamufunsa kuti, “Mukuchokera kuti?”

Ndipo iye anayakha kuti, “Ndine Mlevi wochokera ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Ndikufunafuna malo okhala.”

10Tsono Mika anati kwa iye, “Khalani ndi ine. Mukhale ngati mlangizi wanga ndi wansembe, ndipo ine ndizikupatsani ndalama za siliva khumi pa chaka komanso zovala ndi zakudya.” 11Choncho Mleviyo anavomera kuti azikhala naye, ndipo mnyamatayo anakhala ngati mmodzi mwa ana ake aamuna. 12Pambuyo pake Mika anapatula Mleviyo ndipo mnyamatayu anakhala wansembe. Tsono ankakhala mʼnyumba ya Mika. 13Ndipo Mika anati, “Tsopano ndadziwa kuti Yehova adzandikomera mtima chifukwa Mleviyu ndiye wakhala wansembe wanga.”

New International Version

Judges 17:1-13

Micah’s Idols

1Now a man named Micah from the hill country of Ephraim 2said to his mother, “The eleven hundred shekels17:2 That is, about 28 pounds or about 13 kilograms of silver that were taken from you and about which I heard you utter a curse—I have that silver with me; I took it.”

Then his mother said, “The Lord bless you, my son!”

3When he returned the eleven hundred shekels of silver to his mother, she said, “I solemnly consecrate my silver to the Lord for my son to make an image overlaid with silver. I will give it back to you.”

4So after he returned the silver to his mother, she took two hundred shekels17:4 That is, about 5 pounds or about 2.3 kilograms of silver and gave them to a silversmith, who used them to make the idol. And it was put in Micah’s house.

5Now this man Micah had a shrine, and he made an ephod and some household gods and installed one of his sons as his priest. 6In those days Israel had no king; everyone did as they saw fit.

7A young Levite from Bethlehem in Judah, who had been living within the clan of Judah, 8left that town in search of some other place to stay. On his way17:8 Or To carry on his profession he came to Micah’s house in the hill country of Ephraim.

9Micah asked him, “Where are you from?”

“I’m a Levite from Bethlehem in Judah,” he said, “and I’m looking for a place to stay.”

10Then Micah said to him, “Live with me and be my father and priest, and I’ll give you ten shekels17:10 That is, about 4 ounces or about 115 grams of silver a year, your clothes and your food.” 11So the Levite agreed to live with him, and the young man became like one of his sons to him. 12Then Micah installed the Levite, and the young man became his priest and lived in his house. 13And Micah said, “Now I know that the Lord will be good to me, since this Levite has become my priest.”