Oweruza 15 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 15:1-20

Samsoni Abwezera Afilisti

1Patapita nthawi, mu nyengo yodula tirigu, Samsoni anatenga kamwana kambuzi ndipo anapita kukacheza kwa mkazi wake. Iye anati, “Ndikufuna kukalowa ku chipinda cha mkazi wanga.” Koma abambo a mkaziyo anamuletsa kutero.

2Abambo a mkaziyo anati, “Ine ndimaganiza kuti umamuda kwambiri nʼchifukwa chake ndinamupereka kwa mnzako. Kodi mngʼono wake uja sindiye wokongola kupambana iye? Ingotengani ameneyo mʼmalo mwake.”

3Samsoni anawawuza kuti, “Pano sindikhala wochimwa ndikawachita choyipa chachikulu Afilistiwa.” 4Choncho Samsoni anapita nakagwira nkhandwe 300 nazimangirira michira ziwiriziwiri ndipo pa fundo iliyonse ya michirayo anamangirira nsakali. 5Anayatsa nsakalizo kenaka ndi kuzitayira nkhandwe zija mʼminda ya tirigu ya Afilisti, ndipo zinatentha milu ya tirigu, ndi wosadula yemwe pamodzi ndi mitengo ya mpesa ndi ya olivi.

6Tsono Afilisti anayamba kufunsana kuti, “Ndani wachita izi?” Ena anati, “Ndi Samsoni mkamwini wa munthu wa ku Timna uja chifukwa Mtimunayo anatenga mkazi wake ndi kumupereka kwa mnzake.”

Choncho Afilisti anapita kukatentha mtsikanayo pamodzi ndi abambo ake. 7Samsoni anawawuza kuti, “Ngati mumachita zangati zimenezi, ndiye ine sindileka mpaka nditakulipsirani.” 8Choncho Samsoni anamenyana nawo koopsa ndipo anapha ambiri a iwo. Kenaka anakalowa mʼphanga la Etamu, nakhala momwemo.

9Pambuyo pake Afilisti anakamanga misasa ya nkhondo mʼdziko la Yuda, ndi kuthira nkhondo mʼdera la Lehi. 10Anthu a fuko la Yuda anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwabwera kudzamenyana nafe?”

Iwo anayankha kuti, “Tabwera kudzamanga Samsoni ndi kuti timuchite zofanana ndi zimene anatichita.”

11Ndipo anthu 3,000 a ku Yuda anapita ku phanga la Etamu, ndi kukamufunsa Samsoni kuti, “Kodi iwe sudziwa kuti ife amatilamulira ndi Afilisti? Tsono ndi chiyani chimene watichitachi?”

Iye anayankha kuti, “Ine ndinachita zomwe iwo anandichita.”

12Iwo anati kwa iye, “Ife tabwera kuti tikumange ndi kukupereka kwa Afilisti.”

Ndipo Samsoni anati, “Lonjezani mwa lumbiro kuti simundipha ndinu.”

13Iwo anamuyankha kuti, “Ayi, ife sitikupha. Koma tingokumanga ndi kukupereka mʼmanja mwa Afilisti.” Choncho anamumanga ndi zingwe ziwiri zatsopano namutulutsa mʼphanga muja. 14Samsoni anafika ku Lehi, ndipo Afilisti anamuchingamira akufuwula. Nthawi yomweyo Mzimu wa Yehova unatsika pa iye mwamphamvu ndipo zingwe zimene anamumanga nazo zinasanduka ngati thonje lopsa mʼmoto, zinachita ngati zasungunuka nʼkuchoka mʼmanja mwake. 15Anapeza chibwano cha bulu amene anali atangofa kumene. Anachitola ndi kuphera nacho anthu 1,000.

16Ndipo Samsoni anati,

“Ndi chibwano cha bulu,

milu ndi milu ya anthu.

Ndi chibwano cha bulu,

ndapha anthu 1,000.”

17Atatsiriza kuyankhula, anataya chibwanocho, ndipo malowo anawatcha Ramati-Lehi.

18Pambuyo pake anamva ludzu kwambiri ndipo anayitana Yehova mopempha kuti, “Inu mwapatsa mtumiki wanu chipulumutso chachikulu chotere. Kodi tsopano ndife ndi ludzu ndi kugwidwa ndi anthu osachita mdulidwewa?” 19Pamenepo Mulungu anangʼamba nthaka ku Lehi, ndipo madzi anatuluka mʼdzenjemo. Samsoni anamwa madziwo, ndipo mphamvu zake zinabwerera nakhalanso monga analili. Choncho chitsimecho chinatchedwa Eni-Hakore, ndipo chilipobe ku Lehiko mpaka lero.

20Samsoni anatsogolera Israeli pa nthawi ya Afilisti kwa zaka makumi awiri.

New International Version – UK

Judges 15:1-20

Samson’s vengeance on the Philistines

1Later on, at the time of wheat harvest, Samson took a young goat and went to visit his wife. He said, ‘I’m going to my wife’s room.’ But her father would not let him go in.

2‘I was so sure you hated her,’ he said, ‘that I gave her to your companion. Isn’t her younger sister more attractive? Take her instead.’

3Samson said to them, ‘This time I have a right to get even with the Philistines; I will really harm them.’ 4So he went out and caught three hundred foxes and tied them tail to tail in pairs. He then fastened a torch to every pair of tails, 5lit the torches and let the foxes loose in the standing corn of the Philistines. He burned up the shocks and standing corn, together with the vineyards and olive groves.

6When the Philistines asked, ‘Who did this?’ they were told, ‘Samson, the Timnite’s son-in-law, because his wife was given to his companion.’

So the Philistines went up and burned her and her father to death. 7Samson said to them, ‘Since you’ve acted like this, I swear that I won’t stop until I get my revenge on you.’ 8He attacked them viciously and slaughtered many of them. Then he went down and stayed in a cave in the rock of Etam.

9The Philistines went up and camped in Judah, spreading out near Lehi. 10The people of Judah asked, ‘Why have you come to fight us?’

‘We have come to take Samson prisoner,’ they answered, ‘to do to him as he did to us.’

11Then three thousand men from Judah went down to the cave in the rock of Etam and said to Samson, ‘Don’t you realise that the Philistines are rulers over us? What have you done to us?’

He answered, ‘I merely did to them what they did to me.’

12They said to him, ‘We’ve come to tie you up and hand you over to the Philistines.’

Samson said, ‘Swear to me that you won’t kill me yourselves.’

13‘Agreed,’ they answered. ‘We will only tie you up and hand you over to them. We will not kill you.’ So they bound him with two new ropes and led him up from the rock. 14As he approached Lehi, the Philistines came towards him shouting. The Spirit of the Lord came powerfully upon him. The ropes on his arms became like charred flax, and the bindings dropped from his hands. 15Finding a fresh jawbone of a donkey, he grabbed it and struck down a thousand men.

16Then Samson said,

‘With a donkey’s jawbone

I have made donkeys of them.15:16 Or made a heap or two; the Hebrew for donkey sounds like the Hebrew for heap.

With a donkey’s jawbone

I have killed a thousand men.’

17When he finished speaking, he threw away the jawbone; and the place was called Ramath Lehi.15:17 Ramath Lehi means jawbone hill.

18Because he was very thirsty, he cried out to the Lord, ‘You have given your servant this great victory. Must I now die of thirst and fall into the hands of the uncircumcised?’ 19Then God opened up the hollow place in Lehi, and water came out of it. When Samson drank, his strength returned and he revived. So the spring was called En Hakkore,15:19 En Hakkore means caller’s spring. and it is still there in Lehi.

20Samson led15:20 Traditionally judged Israel for twenty years in the days of the Philistines.