Masomphenya a Obadiya
1Masomphenya a Obadiya.
Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti,
Tamva uthenga wochokera kwa Yehova:
Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti,
“Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”
2“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina;
udzanyozedwa kwambiri.
3Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,
iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe
ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali,
iwe amene umanena mu mtima mwako kuti,
‘Ndani anganditsitse pansi?’
4Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga
ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi,
ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”
akutero Yehova.
5“Anthu akuba akanabwera kwa iwe,
kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku,
aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe!
Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
Ngati anthu othyola mphesa akanafika,
kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
6Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse,
chuma chake chobisika chidzabedwa!
7Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire;
abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa;
amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha,
koma iwe sudzazindikira zimenezi.”
8Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo,
kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu,
anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
9Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha,
ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau
adzaphedwa pa nkhondo.
10Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo,
udzakhala wamanyazi;
adzakuwononga mpaka muyaya.
11Pamene adani
ankamulanda chuma chake
pamene alendo analowa pa zipata zake
ndi kuchita maere pa Yerusalemu,
pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
12Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako
pa nthawi ya tsoka lake,
kapena kunyogodola Ayuda
chifukwa cha chiwonongeko chawo,
kapena kuwaseka pa nthawi ya
mavuto awo.
13Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga
pa nthawi ya masautso awo,
kapena kuwanyogodola
pa tsiku la tsoka lawo,
kapena kulanda chuma chawo
pa nthawi ya masautso awo.
14Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu
kuti uphe Ayuda othawa,
kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka
pa nthawi ya mavuto awo.”
15“Tsiku la Yehova layandikira
limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu.
Adzakuchitira zomwe unawachitira ena;
zochita zako zidzakubwerera wekha.
16Iwe unamwa pa phiri langa loyera,
koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza;
iwo adzamwa ndi kudzandira
ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
17Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso;
phirilo lidzakhala lopatulika,
ndipo nyumba ya Yakobo
idzalandira cholowa chake.
18Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto
ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto;
nyumba ya Esau idzasanduka chiputu,
ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza.
Sipadzakhala anthu opulumuka
kuchokera mʼnyumba ya Esau.”
Yehova wayankhula.
19Anthu ochokera ku Negevi adzakhala
ku mapiri a Esau,
ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri
adzatenga dziko la Afilisti.
Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya,
ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
20Aisraeli amene ali ku ukapolo
adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati;
a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi
adzalandira mizinda ya ku Negevi.
21Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni
ndipo adzalamulira mapiri a Esau.
Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.
Авдијина визија
1Виђење Авдијино:
Овако Господ Бог каже о Едому:
Чули смо вест од Господа
и гласник је послан међу народе:
„Устаните! Дигнимо се у бој против њега!“
2„Ево, учинио сам те незнатним међу народима
и врло презреним.
3Дрскост срца твога те је обманула,
ти што живиш у раселини стене,
становниче горских висина.
Говориш у срцу своме:
’Ко да ме доле, на земљу сруши?!’
4Све и да се ко орао винеш,
своје гнездо међу звезде свијеш,
стровалићу те ја и оданде
– говори Господ.
5Ако ти лопови дођу
и по ноћи затирачи,
зар неће накрасти колико им треба?
Ако ти дођу берачи грожђа,
зар неће оставити за пабирчење?
Али ти ћеш бити похаран!
6О, како ће Исава да претресу!
Наћи ће му сва скривена блага.
7Све до границе потерали те сви твоји савезници.
Обманули су те, надвладали те твоји вајни пријатељи.
Ти што твој хлеб једу, испод тебе копају ти јаму,
а ти о томе појма немаш.
8Нећу ли оног дана – говори Господ –
сатрти мудраце едомске
и учене с горе Исавове?
9О, Темане, препашће се твоји ратници,
сви са горе Исавове биће побијени.
10Због насиља над Јаковом, братом твојим,
прекриће те стид
и довека сатрвен ћеш бити.
11Оног дана када си стајао по страни,
од дана кад су му туђинци благо заробили,
кад незнанци грунуше на врата његова
и за Јерусалим жреб бацаше,
ти си био као један од њих.
12Ниси смео да посматраш дан брата свога,
дан његове коби;
ниси смео да ликујеш над народом Јуде,
оног дана кад су разорени,
и злурадо да се цериш
на дан њиног јада.
13Ниси смео да прођеш кроз врата мог народа
у онај дан њихове пропасти.
Ниси смео да посматраш зло њихово
у тај кобни дан,
да се пружаш за њиховим благом
на дан њиног јада.
14Ниси смео да стојиш на раскршћима,
бегунце његове да убијаш,
да његове издајеш преживеле
у том дану јада.
15Близу је дан Господњи
свим народима.
Шта си чинио, чиниће се теби.
Обиће ти се о главу дела твоја.
16Јер, као што сте пили на мојој светој гори
и сви народи ће истрајно пити.
И пиће и гутаће
и биће као да их није било.
17А на гори Сион спасење ће бити
и биће она светиња,
а дом ће Јаковљев запосести поседе своје.
18Ватра ће постати дом Јаковљев,
дом Јосифов биће пламен,
а дом Исавов постаће стрњика.
И спалиће их, прогутаће их,
и неће се спасти нико
из дома Исавовог.“
Јер тако каже Господ.
19Они из Негева ће освојити гору Исавову,
а они из равнице Филистеју.
Освојиће и подручје Јефремово и подручје Самарије,
а Венијамин ће освојити Галад.
20И изгнаници са бедема народа израиљског
наследиће земљу Хананаца до Сарепте.
А изгнаници из Јерусалима,
који су у Сефарду, запосешће градове Негева.
21И изаћи ће избављени на гору Сион
да суде гори Исавовој
и Царство ће припадати Господу.