Nyimbo ya Solomoni 8 – CCL & AKCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 8:1-14

1Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga,

amene anayamwa mawere a amayi anga!

Ndikanakumana nawe pa njira,

ndikanakupsompsona,

ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.

2Ndikanakutenga

ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,

amayi amene anandiphunzitsa,

ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe,

zotsekemera za makangadza.

3Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere

ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.

4Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani:

musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

Abwenzi

5Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo,

atatsamira wokondedwa wakeyo?

Mkazi

Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi,

pamenepo ndi pamene amayi anachirira,

pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.

6Undiyike pamtima pako ngati chidindo,

ngati chidindo cha pa dzanja lako;

pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa,

nsanje ndiyaliwuma ngati manda.

Chikondi chimachita kuti lawilawi

ngati malawi a moto wamphamvu.

7Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi,

mitsinje singachikokolole chikondicho.

Ngati wina apereka chuma chonse

cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi,

adzangonyozeka nazo kotheratu.

Abwenzi

8Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono,

koma alibe mawere,

kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu

pa tsiku limene adzamufunsire?

9Ngati iye ndi khoma,

tidzamumangira nsanja ya siliva.

Ngati iye ndi chitseko,

tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.

Mkazi

10Ine ndili ngati khoma,

ndipo mawere anga ndi nsanja zake.

Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa

ndine wobweretsa mtendere.

11Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni;

iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi,

aliyense mwa iwo ankayenera kupereka

ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.

12Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha.

Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000

ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.

Mwamuna

13Iwe amene umakhala mʼminda

uli pamodzi ndi anzako,

ndilole kuti ndimve liwu lako!

Mkazi

14Fulumira wokondedwa wanga,

ndipo ukhale ngati gwape

kapena mwana wa mbawala

wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom Mu Dwom 8:1-14

1Sɛ anka woyɛɛ me nuabarima

a wunum me na nufu ano,

na mihuu wo wɔ abɔnten so a,

anka mefew wʼano,

a obiara rentumi mmu me animtiaa.

2Anka medi wʼanim

na mede wo aba me na fi,

ɔno a wakyerɛkyerɛ me.

Anka mɛma wo bobesa a wɔde pɛprɛ afra mu,

me ntunkum mu nsu dɔkɔdɔkɔ no bi.

3Ne nsa benkum da mʼatiko

na ne nsa nifa aka me afam ne bo.

4Yerusalem mmabea, mehyɛ mo sɛ,

morennyan na morenhwanyan ɔdɔ mu

kosi bere a ɛsɛ mu.

Nnamfonom:

5Hena na ofi sare so reba a

otweri ne dɔfo koko mu yi?

Ababaa:

Mekanyan wo wɔ aprɛ dua no ase;

ɛhɔ na wo na nyinsɛnee wo,

ɛhɔ na nea ɔkoo awo no woo wo.

6Fa me to wo koma so sɛ nsɔwanode,

sɛ nsɔwanode wɔ wʼabasa so,

efisɛ ɔdɔ ano yɛ den sɛ owu,

ne ninkutwe tim hɔ sɛ ɔda.

Ɛhyehye sɛ ogyatannaa,

sɛ ogyatannaa a ano yɛ den pa ara.

7Nsu dodow rentumi nnum ɔdɔ;

nsubɔnten rentumi nhohoro nkɔ.

Sɛ obi de ne fi ahonya nyinaa bɛsesa ɔdɔ a

anka wɔremmu no ade a ɛsom bo.

Nnamfonom:

8Yɛwɔ nuabea akumaa bi a,

ne nufu mmobɔɔ ɛ.

Dɛn na yɛbɛyɛ ama yɛn nuabea yi

wɔ da a wobebisa no ase?

9Sɛ ɔyɛ ɔfasu a,

yebesi dwetɛ abantenten abɔ ne ho ban.

Sɛ ɔyɛ ɔpon a,

yɛde sida besiw ne pon ano kwan.

Ababaa:

10Meyɛ ɔfasu,

na me nufu te sɛ abantenten.

Enti nʼani so no mayɛ sɛ obi a

ɔde nea ɛsɔ ani reba.

11Na Salomo wɔ bobeturo wɔ Baal-Hamon;

ɔde ne bobeturo no maa apaafo.

Na ɛsɛ sɛ wɔn mu biara tua no

nnwetɛbona apem.

12Nanso me bobeturo yi yɛ me de.

Me de, meremfa mma;

Salomo de ne de gye nnwetɛbona apem,

na otua nʼapaafo nnwetɛbona ahannu ma wɔhwɛ ne nnuaba no so.

Aberante:

13Wo a wote turo no mu

ne nnamfonom a wɔka wo ho,

ma mente wo nne.

Ababaa:

14Bra ma yɛnkɔ, me dɔfo,

na yɛ wo ho sɛ ɔdabɔ ba

anaasɛ ɔforote ba a

ɔwɔ mmepɔw a nnuhuam ahyɛ so ma so.