Numeri 7 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 7:1-89

Zopereka Popatula Chihema

1Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. 2Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka. 3Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.

4Yehova anawuza Mose kuti, 5“Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”

6Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi. 7Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo 8ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe. 9Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.

10Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo. 11Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”

12Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.

13Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya; 14mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 15mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza; 16mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo; 17ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.

18Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.

19Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya. 20Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani; 21mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza: 22mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo; 23ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.

24Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.

25Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya; 26mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 27mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza; 28mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 29ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.

30Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.

31Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya. 32Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 33mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza; 34mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 35ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.

36Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.

37Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya; 38mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani; 39mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza; 40mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 41ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.

42Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.

43Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya; 44mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 45mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza: 46mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 47ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.

48Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.

49Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya; 50mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 51mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza; 52mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 53ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.

54Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.

55Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya; 56mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani, 57mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza; 58mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 59ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.

60Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.

61Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya; 62mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 63mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza; 64mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 65ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.

66Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.

67Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya; 68mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 69mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza; 70mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 71ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.

72Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.

73Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya; 74mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 75mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza; 76mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo; 77ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.

78Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.

79Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya; 80mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 81mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza; 82mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 83ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.

84Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri. 85Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. 86Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka. 87Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo. 88Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.

89Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

民數記 7:1-89

各首領的奉獻

1摩西支好聖幕後,便用膏油抹聖幕和其中的器具、祭壇和壇上的器具,使它們聖潔。 2然後,以色列各支派的首領,就是負責人口統計的各族長,都來奉獻。 3他們把供物帶到聖幕前獻給耶和華:每兩位首領奉獻一輛篷車,每位首領奉獻一頭公牛,共六輛篷車和十二頭公牛。

4耶和華對摩西說: 5「你要收下這些供物,按利未人的工作分配給他們,供會幕使用。」 6於是,摩西收下車和牛,交給利未人。 7他分給革順的子孫兩輛車和四頭牛, 8分給米拉利的子孫四輛車和八頭牛。他們都在祭司亞倫的兒子以他瑪的領導下任職。 9摩西沒有把供物分給哥轄的子孫,因為他們要用肩扛所負責的聖物。

10膏抹祭壇時,各首領都為獻壇之禮帶來供物,放在祭壇前。 11耶和華對摩西說:「每天要有一位首領為獻壇之禮獻上供物。」

12第一天來獻供物的是猶大支派亞米拿達的兒子拿順13他的供物是一個重一公斤半的銀盤,一個重八百克的銀碗,重量都以聖所的秤為準,都盛滿作素祭的調了油的細麵粉; 14一個重一百一十克盛滿香的金碟子; 15作燔祭的一頭公牛犢、一隻公綿羊和一隻一歲公羊羔; 16一隻作贖罪祭的公山羊; 17作平安祭的兩頭公牛、五隻公綿羊、五隻公山羊和五隻一歲的公羊羔。

18第二天來獻供物的是以薩迦支派的首領、蘇押的兒子拿坦業19他的供物是一個重一公斤半的銀盤,一個重八百克的銀碗,重量都以聖所的秤為準,都盛滿作素祭的調了油的細麵粉; 20一個重一百一十克盛滿香的金碟子; 21作燔祭的一頭公牛犢、一隻公綿羊和一隻一歲公羊羔; 22一隻作贖罪祭的公山羊; 23作平安祭的兩頭公牛、五隻公綿羊、五隻公山羊和五隻一歲的公羊羔。

24第三天來獻供物的是西布倫支派的首領、希倫的兒子以利押25他的供物是一個重一公斤半的銀盤,一個重八百克的銀碗,重量都以聖所的秤為準,都盛滿作素祭的調了油的細麵粉; 26一個重一百一十克盛滿香的金碟子; 27作燔祭的一頭公牛犢、一隻公綿羊和一隻一歲公羊羔; 28一隻作贖罪祭的公山羊, 29作平安祭的兩頭公牛、五隻公綿羊、五隻公山羊和五隻一歲的公羊羔。

30第四天來獻供物的是呂便支派的首領、示丟珥的兒子以利蘇31他的供物是一個重一公斤半的銀盤,一個重八百克的銀碗,重量都以聖所的秤為準,都盛滿作素祭的調了油的細麵粉; 32一個重一百一十克盛滿香的金碟子; 33作燔祭的一頭公牛犢、一隻公綿羊和一隻一歲公羊羔; 34一隻作贖罪祭的公山羊; 35作平安祭的兩頭公牛、五隻公綿羊、五隻公山羊和五隻一歲的公羊羔。

36第五天來獻供物的是西緬支派的首領、蘇利沙代的兒子示路蔑37他的供物是一個重一公斤半的銀盤,一個重八百克的銀碗,重量都以聖所的秤為準,都盛滿作素祭的調了油的細麵粉; 38一個重一百一十克盛滿香的金碟子; 39作燔祭的一頭公牛犢、一隻公綿羊和一隻一歲公羊羔; 40一隻作贖罪祭的公山羊; 41作平安祭的兩頭公牛、五隻公綿羊、五隻公山羊和五隻一歲的公羊羔。

42第六天來獻供物的是迦得支派的首領、丟珥的兒子以利雅薩43他的供物是一個重一公斤半的銀盤,一個重八百克的銀碗,重量都以聖所的秤為準,都盛滿作素祭的調了油的細麵粉; 44一個重一百一十克盛滿香的金碟子; 45作燔祭的一頭公牛犢、一隻公綿羊和一隻一歲公羊羔; 46一隻作贖罪祭的公山羊; 47作平安祭的兩頭公牛、五隻公綿羊、五隻公山羊和五隻一歲的公羊羔。

48第七天來獻供物的是以法蓮支派的首領、亞米忽的兒子以利沙瑪49他的供物是一個重一公斤半的銀盤,一個重八百克的銀碗,重量都以聖所的秤為準,都盛滿作素祭的調了油的細麵粉; 50一個重一百一十克盛滿香的金碟子; 51作燔祭的一頭公牛犢、一隻公綿羊和一隻一歲公羊羔; 52一隻作贖罪祭的公山羊; 53作平安祭的兩頭公牛、五隻公綿羊、五隻公山羊和五隻一歲的公羊羔。

54第八天來獻供物的是瑪拿西支派的首領、比大蘇的兒子迦瑪列55他的供物是一個重一公斤半的銀盤,一個重八百克的銀碗,重量都以聖所的秤為準,都盛滿作素祭的調了油的細麵粉; 56一個重一百一十克盛滿香的金碟子; 57作燔祭的一頭公牛犢、一隻公綿羊和一隻一歲公羊羔; 58一隻作贖罪祭的公山羊; 59作平安祭的兩頭公牛、五隻公綿羊、五隻公山羊和五隻一歲的公羊羔。

60第九天來獻供物的是便雅憫支派的首領、基多尼的兒子亞比但61他的供物是一個重一公斤半的銀盤,一個重八百克的銀碗,重量都以聖所的秤為準,都盛滿作素祭的調了油的細麵粉; 62一個重一百一十克盛滿香的金碟子; 63作燔祭的一頭公牛犢、一隻公綿羊和一隻一歲公羊羔; 64一隻作贖罪祭的公山羊; 65作平安祭的兩頭公牛、五隻公綿羊、五隻公山羊和五隻一歲的公羊羔。

66第十天來獻供物的是支派的首領、亞米沙代的兒子亞希以謝67他的供物是一個重一公斤半的銀盤,一個重八百克的銀碗,重量都以聖所的秤為準,都盛滿作素祭的調了油的細麵粉; 68一個重一百一十克盛滿香的金碟子; 69作燔祭的一頭公牛犢、一隻公綿羊和一隻一歲公羊羔; 70一隻作贖罪祭的公山羊; 71作平安祭的兩頭公牛、五隻公綿羊、五隻公山羊和五隻一歲的公羊羔。

72第十一天來獻供物的是亞設支派的首領、俄蘭的兒子帕結73他的供物是一個重一公斤半的銀盤,一個重八百克的銀碗,重量都以聖所的秤為準,都盛滿作素祭的調了油的細麵粉; 74一個重一百一十克盛滿香的金碟子; 75作燔祭的一頭公牛犢、一隻公綿羊和一隻一歲公羊羔; 76一隻作贖罪祭的公山羊; 77作平安祭的兩頭公牛、五隻公綿羊、五隻公山羊和五隻一歲的公羊羔。

78第十二天來獻供物的是拿弗他利支派的首領、以南的兒子亞希拉79他的供物是一個重一公斤半的銀盤,一個重八百克的銀碗,重量都以聖所的秤為準,都盛滿作素祭的調了油的細麵粉; 80一個重一百一十克盛滿香的金碟子; 81作燔祭的一頭公牛犢、一隻公綿羊和一隻一歲公羊羔; 82一隻作贖罪祭的公山羊; 83作平安祭的兩頭公牛、五隻公綿羊、五隻公山羊和五隻一歲的公羊羔。

84以上是膏抹祭壇時以色列各首領為獻壇之禮所獻的供物,共計有銀盤、銀碗和金碟子各十二個, 85以聖所的秤為準,每個銀盤重一公斤半,每個銀碗重八百克,共重二十七點六公斤; 86以聖所的秤為準,盛滿香的十二個金碟子每個重一百一十克,共重一點三二公斤; 87作燔祭的牲畜共有公牛犢、公綿羊、一歲的公羊羔各十二隻,還有一起獻上的素祭以及作贖罪祭的公山羊十二隻; 88作平安祭的牲畜共有公牛二十四頭,公綿羊、公山羊、一歲的公羊羔各六十隻。

以上是在膏抹祭壇後所收到的供物。

89每當摩西走進會幕要與耶和華說話時,便聽見耶和華從約櫃的施恩座上、兩個基路伯天使中間對他說話。