Numeri 5 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 5:1-31

Ukhondo wa pa Msasa

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Lamula Aisraeli kuti achotse mu msasa aliyense amene ali ndi matenda opatsirana a pa khungu kapena matenda otuluka madzi mʼthupi a mtundu uliwonse, kapena aliyense wodetsedwa chifukwa cha munthu wakufa. 3Muchotse amuna komanso amayi ndipo muwatulutsire kunja kwa msasa kuti asadetse msasa wawo kumene Ine ndimakhala pakati pawo.” 4Aisraeli anachitadi zimenezi. Anawatulutsira kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.

Kukonza Zolakwika

5Yehova anati kwa Mose, 6“Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene mwamuna kapena mayi walakwira mnzake mwa njira iliyonse, ndiye kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Munthuyo ndi wochimwa ndithu ndipo 7ayenera kuwulula tchimo limene anachitalo. Ayenera kubweza zonse zimene anawononga, ndipo awonjezerepo chimodzi mwa magawo asanu ndi kuzipereka kwa munthu amene anamulakwirayo. 8Ngati wolakwiridwayo alibe mʼbale komwe kungapite zinthu zobwezedwazo, zinthuzo zikhale za Yehova ndipo azipereke kwa wansembe, pamodzi ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopepesera tchimo lake. 9Zopereka zonse zopatulika zomwe Aisraeli abwera nazo kwa wansembe zikhale za wansembeyo. 10Mphatso zilizonse zopatulika ndi za munthuyo, koma zomwe wapereka kwa wansembe ndi za wansembeyo.’ ”

Mkazi Wosakhulupirika

11Kenaka Yehova anawuza Mose kuti, 12“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mkazi wa munthu wina ayenda njira yosayenera nakhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, 13nakagonana ndi mwamuna wina koma mwamuna wake wosadziwa, ndipo palibe wina aliyense wadziwa za kudzidetsa kwake (pakuti palibe mboni yomuneneza chifukwa sanagwidwe akuchita), 14mwamuna wake ndi kuyamba kuchita nsanje ndi kukayikira mkazi wakeyo kuti ndi wodetsedwa, komanso ngati amuchitira nsanje ndi kumukayikira ngakhale asanadzidetse, 15apite naye mkaziyo kwa wansembe. Ndipo popita atengenso gawo lakhumi la chopereka chaufa wa barele wokwana kilogalamu imodzi mʼmalo mwa mkaziyo. Asathire mafuta pa nsembeyo kapena lubani, chifukwa ndi nsembe ya chopereka ya chakudya yopereka chifukwa cha nsanje, nsembe yozindikiritsa tchimo.’ ”

16“ ‘Wansembe abwere naye mkaziyo ndi kumuyimitsa pamaso pa Yehova. 17Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano. 18Wansembe atayimika mkaziyo pamaso pa Yehova, amumasule tsitsi lake, ndipo ayike mʼmanja mwake nsembe yozindikiritsa tchimo, nsembe yachakudya ya nsanje, wansembeyo atanyamula madzi owawa omwe amabweretsa temberero.’ 19Kenaka wansembeyo alumbiritse mkaziyo ndi kuti, ‘Ngati mwamuna wina aliyense sanagonane ndi iwe ndipo sunayende njira yoyipa ndi kukhala wodetsedwa pomwe uli pa ukwati ndi mwamuna wako, madzi owawa awa omwe amabweretsa temberero asakupweteke. 20Koma ngati wayenda njira yoyipa uli pa ukwati ndi mwamuna wako ndi kudzidetsa pogonana ndi mwamuna amene si mwamuna wako,’ 21pamenepo wansembe alumbiritse mkaziyo ndi mawu a matemberero ndi kumuwuza kuti, ‘Yehova achititse anthu ako kukutemberera ndi kukunyoza pamene awononga ntchafu yako ndi kutupitsa mimba yako. 22Madzi awa obweretsa temberero alowe mʼthupi mwako ndi kutupitsa mimba yako ndi kuwononga ntchafu yako.’ ”

“Pamenepo mkaziyo anene kuti, ‘Ameni, ameni.’ ”

23“ ‘Wansembe alembe matemberero amenewa mʼbuku ndi kuwanyika mʼmadzi owawa aja. 24Amwetse mkaziyo madzi owawawo omwe amabweretsa temberero, ndipo madzi amenewo adzalowa mʼmimba mwake ndi kuyambitsa ululu woopsa. 25Wansembe achotse mʼmanja mwa mkaziyo nsembe yachakudya ya nsanje ija, nayiweyula pamaso pa Yehova ndi kuyipereka pa guwa lansembe. 26Tsono wansembeyo atapeko ufa dzanja limodzi kuti ukhale wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa lansembe. Atatha izi, amwetse mkaziyo madzi aja. 27Ndipo ngati mkaziyo anadzidetsadi ndi kukhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, pamene amwa madzi obweretsa matemberero aja, nalowa mʼmimba mwake, adzamva ululu woopsa. Mimba yake idzatupa ndi ntchafu yake idzawonongeka ndipo adzakhala wotembereredwa pakati pa anthu ake. 28Koma ngati mkaziyo sanadzidetse ndi kuti alibe tchimo, adzakhala wopanda mlandu ndipo adzabereka ana.

29“ ‘Limeneli ndiye lamulo la nsanje pamene mkazi wayenda njira yoyipa ndi kudzidetsa ali pa ukwati ndi mwamuna wake, 30kapena pamene maganizo a nsanje abwera kwa mwamuna wake chifukwa chokayikira mkazi wakeyo. Wansembe azitenga mkazi wotere ndi kumuyimiritsa pamaso pa Yehova ndipo agwiritse ntchito lamulo lonseli kwa mkaziyo. 31Mwamunayo adzakhala wopanda tchimo lililonse, koma mkaziyo adzasenza zotsatira za tchimo lake.’ ”

New International Version

Numbers 5:1-31

The Purity of the Camp

1The Lord said to Moses, 2“Command the Israelites to send away from the camp anyone who has a defiling skin disease5:2 The Hebrew word for defiling skin disease, traditionally translated “leprosy,” was used for various diseases affecting the skin. or a discharge of any kind, or who is ceremonially unclean because of a dead body. 3Send away male and female alike; send them outside the camp so they will not defile their camp, where I dwell among them.” 4The Israelites did so; they sent them outside the camp. They did just as the Lord had instructed Moses.

Restitution for Wrongs

5The Lord said to Moses, 6“Say to the Israelites: ‘Any man or woman who wrongs another in any way5:6 Or woman who commits any wrong common to mankind and so is unfaithful to the Lord is guilty 7and must confess the sin they have committed. They must make full restitution for the wrong they have done, add a fifth of the value to it and give it all to the person they have wronged. 8But if that person has no close relative to whom restitution can be made for the wrong, the restitution belongs to the Lord and must be given to the priest, along with the ram with which atonement is made for the wrongdoer. 9All the sacred contributions the Israelites bring to a priest will belong to him. 10Sacred things belong to their owners, but what they give to the priest will belong to the priest.’ ”

The Test for an Unfaithful Wife

11Then the Lord said to Moses, 12“Speak to the Israelites and say to them: ‘If a man’s wife goes astray and is unfaithful to him 13so that another man has sexual relations with her, and this is hidden from her husband and her impurity is undetected (since there is no witness against her and she has not been caught in the act), 14and if feelings of jealousy come over her husband and he suspects his wife and she is impure—or if he is jealous and suspects her even though she is not impure— 15then he is to take his wife to the priest. He must also take an offering of a tenth of an ephah5:15 That is, probably about 3 1/2 pounds or about 1.6 kilograms of barley flour on her behalf. He must not pour olive oil on it or put incense on it, because it is a grain offering for jealousy, a reminder-offering to draw attention to wrongdoing.

16“ ‘The priest shall bring her and have her stand before the Lord. 17Then he shall take some holy water in a clay jar and put some dust from the tabernacle floor into the water. 18After the priest has had the woman stand before the Lord, he shall loosen her hair and place in her hands the reminder-offering, the grain offering for jealousy, while he himself holds the bitter water that brings a curse. 19Then the priest shall put the woman under oath and say to her, “If no other man has had sexual relations with you and you have not gone astray and become impure while married to your husband, may this bitter water that brings a curse not harm you. 20But if you have gone astray while married to your husband and you have made yourself impure by having sexual relations with a man other than your husband”— 21here the priest is to put the woman under this curse—“may the Lord cause you to become a curse5:21 That is, may he cause your name to be used in cursing (see Jer. 29:22); or, may others see that you are cursed; similarly in verse 27. among your people when he makes your womb miscarry and your abdomen swell. 22May this water that brings a curse enter your body so that your abdomen swells or your womb miscarries.”

“ ‘Then the woman is to say, “Amen. So be it.”

23“ ‘The priest is to write these curses on a scroll and then wash them off into the bitter water. 24He shall make the woman drink the bitter water that brings a curse, and this water that brings a curse and causes bitter suffering will enter her. 25The priest is to take from her hands the grain offering for jealousy, wave it before the Lord and bring it to the altar. 26The priest is then to take a handful of the grain offering as a memorial5:26 Or representative offering and burn it on the altar; after that, he is to have the woman drink the water. 27If she has made herself impure and been unfaithful to her husband, this will be the result: When she is made to drink the water that brings a curse and causes bitter suffering, it will enter her, her abdomen will swell and her womb will miscarry, and she will become a curse. 28If, however, the woman has not made herself impure, but is clean, she will be cleared of guilt and will be able to have children.

29“ ‘This, then, is the law of jealousy when a woman goes astray and makes herself impure while married to her husband, 30or when feelings of jealousy come over a man because he suspects his wife. The priest is to have her stand before the Lord and is to apply this entire law to her. 31The husband will be innocent of any wrongdoing, but the woman will bear the consequences of her sin.’ ”