Nehemiya 1 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 1:1-11

Pemphero la Nehemiya

1Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya:

Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa, 2Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.

3Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”

4Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba. 5Ndinkati:

“Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu. 6Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani. 7Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.

8“Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina. 9Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’

10“Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu. 11Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.”

Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.

New International Reader’s Version

Nehemiah 1:1-11

Nehemiah Prays to the Lord

1These are the words of Nehemiah. He was the son of Hakaliah.

I was in the fort of Susa. I was there in the 20th year that Artaxerxes was king. It was in the month of Kislev. 2At that time Hanani came from Judah with some other men. He was one of my brothers. I asked him and the other men about the Jews who were left alive in Judah. They had returned from Babylon. I also asked him about Jerusalem.

3He and the men with him said to me, “Some of the people who returned are still alive. They are back in the land of Judah. But they are having a hard time. They are ashamed. The wall of Jerusalem is broken down. Its gates have been burned with fire.”

4When I heard about these things, I sat down and wept. For several days I was very sad. I didn’t eat any food. And I prayed to the God of heaven. 5I said,

Lord, you are the God of heaven. You are a great and wonderful God. You keep the covenant you made with those who love you and obey your commandments. You show them your love. 6Please pay careful attention to my prayer. See how your people are suffering. Please listen to me. I’m praying to you day and night. I’m praying for the people of Israel. We Israelites have committed sins against you. All of us admit it. I and my family have also sinned against you. 7We’ve done some very evil things. We haven’t obeyed the commands, rules and laws you gave your servant Moses.

8“Remember what you told him. You said, ‘If you people are not faithful, I will scatter you among the nations. 9But if you return to me, I will bring you back. If you obey my commands, I will gather you together again. I will bring you back from the farthest places on earth. I will bring you to the special place where I have chosen to put my Name.’

10Lord, they are your people. They serve you. You used your great strength and mighty hand to set them free from Egypt. 11Lord, please pay careful attention to my prayer. Listen to the prayers of all of us. We take delight in bringing honor to your name. Give me success today when I bring my request to King Artaxerxes.”

I was the king’s wine taster.