Nahumu 1 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nahumu 1:1-15

1Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.

Mkwiyo wa Yehova pa Ninive

2Yehova ndi Mulungu wansanje

ndiponso wobwezera;

Yehova amabwezera ndipo ndi waukali.

Yehova amabwezera adani ake

ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.

3Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu;

ndipo sadzalola kuti munthu

wolakwa asalangidwe.

Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe,

ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.

4Amalamulira nyanja ndipo imawuma;

amawumitsa mitsinje yonse.

Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma

ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.

5Mapiri amagwedera pamaso pake

ndipo zitunda zimasungunuka.

Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake,

dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.

6Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa?

Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa?

Ukali wake ukuyaka ngati moto;

matanthwe akunyeka pamaso pake.

7Yehova ndi wabwino,

ndiye kothawirako nthawi ya masautso.

Amasamalira amene amamudalira,

8koma ndi madzi achigumula choopsa

Iye adzawononga adani ake (Ninive);

adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.

9Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova

adzachiwononga kotheratu;

msautso sudzabweranso kachiwiri.

10Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga

ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo;

adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.

11Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa,

wofuna kuchitira Yehova chiwembu,

amene amapereka uphungu woyipa.

12Yehova akuti,

“Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi,

kaya iwowo ndi ambiri,

koma adzawonongedwa ndi kutheratu.

Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda,

sindidzakuzunzanso.

13Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako

ndipo ndidzadula maunyolo ako.”

14Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti,

“Sudzakhala ndi zidzukulu

zimene zidzadziwike ndi dzina lako.

Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba

amene ali mʼnyumba ya milungu yako.

Ine ndidzakukumbira manda

chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”

15Taonani, pa phiripo,

mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino,

amene akulengeza za mtendere!

Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu

ndipo kwaniritsani malumbiro anu.

Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo;

iwo adzawonongedwa kotheratu.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Наум 1:1-15

1Пророчество о Ниневии. Книга видений Наума из Елкоша.

Гнев Вечного против Ниневии

2Вечный1:2 Вечный – на языке оригинала: «Яхве». Под этим именем Всевышний открылся Мусе и народу Исраила (см. Исх. 3:13-15). См. пояснительный словарь. – ревнивый и мстительный Бог;

Вечный мстительный и гневливый.

Вечный мстит Своим врагам

и помнит зло недругов Своих.

3Вечный долготерпелив и велик в Своём могуществе;

Вечный не оставит виновных без наказания.

Его шествие – в буре и вихре,

облака – пыль от Его ног.

4Он приказывает морю, и оно высыхает,

рекам – и они иссякают.

Богатые пастбища Башана и Кармила увядают,

блёкнут цветы на Ливане1:4 Башан, Кармил, Ливан – эти земли славились своим плодородием..

5Сотрясаются перед Ним горы,

и тают холмы.

Земля трепещет перед Его лицом,

трепещет мир и всё живущее в нём.

6Кто устоит перед Его негодованием?

И кто сможет выдержать Его пылающий гнев?

Подобно огню разливается Его гнев,

скалы рассыпаются перед Ним.

7Вечный благ,

Он – убежище в дни бедствий.

Он заботится о тех, кто Ему доверяет,

8но всепотопляющим наводнением

Он разрушит Ниневию до основания;

мрак настигнет Его врагов.

9Что бы они ни замышляли против Вечного1:9 Или: «Что они замышляют против Вечного?»,

Он истребит их до конца,

и бедствие уже не повторится.

10Они запутаются в терновнике

и будут пьяны от вина;

они будут уничтожены, как сухое жнивьё.

11Из тебя, Ниневия, вышел тот,

кто замышляет злое против Вечного,

кто советует беззаконное.

12Так говорит Вечный:

– Хотя они сильны и многочисленны,

они будут уничтожены и исчезнут,

а тебя, Иудея, раньше Я отягощал,

но впредь уже не стану.

13И теперь Я сокрушу их ярмо, что на твоей шее,

и разорву твои оковы.

14Вечный дал следующее повеление о тебе, Ниневия:

– Не станет у тебя потомков,

носящих твоё имя.

Я разрушу твоих идолов и уничтожу истуканы,

что находятся в храмах твоих богов.

Я приготовлю тебе могилу,

потому что ты проклята.

15Смотри, идёт по горам гонец, несущий радостную весть,

провозглашающий мир!

Отмечай свои праздники, Иудея,

исполняй свои обещания.

Не вторгнется больше беззаконный в твои владения,

потому что будет полностью уничтожен.