Mlaliki 9 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 9:1-18

Mathero a Zinthu Zonse ndi Wofanana

1Ndinalingalira zonse ndanenazi ndipo ndinapeza kuti anthu olungama ndi anthu anzeru ali mʼmanja mwa Mulungu pamodzi ndi zimene amachita, koma palibe amene amadziwa zimene zikumudikira mʼtsogolo mwake, kaya chikondi kapena chidani. 2Onsewa mathero awo ndi amodzi, anthu olungama ndi anthu oyipa, abwino ndi oyipa, oyera ndi odetsedwa, amene amapereka nsembe ndi amene sapereka nsembe.

Zomwe zimachitikira munthu wabwino,

zimachitikiranso munthu wochimwa,

zomwe zimachitikira amene amalumbira,

zimachitikiranso amene amaopa kulumbira.

3Choyipa chimene chili mʼzonse zochitika pansi ndi ichi: Mathero a zonse ndi amodzi. Ndithu, mitima ya anthu ndi yodzaza ndi zoyipa, ndipo mʼmitima mwawo muli zamisala pamene ali ndi moyo, potsiriza pake iwo amakakhala pamodzi ndi anthu akufa. 4Aliyense amene ali ndi moyo amakhala ndi chiyembekezo, pajatu galu wamoyo aposa mkango wakufa!

5Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa,

koma akufa sadziwa kanthu;

alibe mphotho ina yowonjezera,

ndipo palibe amene amawakumbukira.

6Chikondi chawo, chidani chawo

ndiponso nsanje yawo, zonse zinatha kalekale;

sadzakhalanso ndi gawo

pa zonse zochitika pansi pano.

7Pita, kadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala, pakuti tsopano Mulungu akukondwera ndi zochita zako. 8Uzivala zovala zoyera nthawi zonse, uzidzola mafuta mʼmutu mwako nthawi zonse. 9Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi wako amene umamukonda, masiku onse a moyo uno wopanda phindu, amene Mulungu wakupatsa pansi pano. Pakuti mkaziyo ndiye gawo la moyo wako pa ntchito yako yolemetsa pansi pano. 10Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru.

11Ine ndinaonanso chinthu china pansi pano:

opambana pa kuthamanga si aliwiro,

kapena opambana pa nkhondo si amphamvu,

ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru,

kapena okhala ndi chuma si odziwa zambiri,

kapena okomeredwa mtima si ophunzira;

koma mwayi umangowagwera onsewa pa nthawi yake.

12Kungoti palibe munthu amene amadziwa kuti nthawi yake idzafika liti:

monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde,

kapena mmene mbalame zimakodwera mu msampha,

chimodzimodzinso anthu amakodwa mu msampha pa nthawi yoyipa,

pamene tsoka limawagwera mosayembekezera.

Nzeru Iposa Uchitsiru

13Ine ndinaonanso pansi pano chitsanzo ichi cha nzeru chimene chinandikhudza kwambiri: 14Panali mzinda waungʼono umene unali ndi anthu owerengeka. Ndipo mfumu yamphamvu inabwera kudzawuthira nkhondo, inawuzungulira ndi kumanga mitumbira yankhondo. 15Tsono mu mzindamo munali munthu wosauka koma wanzeru, ndipo anapulumutsa mzindawo ndi nzeru zakezo. Koma palibe amene anakumbukira munthu wosaukayo. 16Choncho ine ndinati, “Nzeru ndi yopambana mphamvu.” Koma nzeru ya munthu wosauka imanyozedwa, ndipo palibe amene amalabadirako za mawu ake.

17Mawu oyankhula mofatsa a munthu wanzeru, anthu amawasamalira kwambiri

kupambana kufuwula kwa mfumu ya zitsiru.

18Nzeru ndi yabwino kupambana zida zankhondo,

koma wochimwa mmodzi amawononga zinthu zambiri zabwino.

New Serbian Translation

Књига проповедникова 9:1-18

Једнака судбина за све

1Дакле, свему томе сам се срцем предао, да све то разјасним. Јер, и праведан и мудар су са својим делима у Божијој руци. Вољен или омражен – човек не зна ништа од онога што га чека. 2Свима је иста судбина: праведном као и неправедном, добром и чистом као и нечистом, ономе који жртвује, као и ономе који не жртвује,

доброме као и грешноме,

ономе који се заклиње,

као и ономе који се боји заклињања.

3Ово је зло у свему што се чини под капом небеском: свима је иста судбина, а и срце људи је пуно зла. Лудост је у њиховом срцу док год су живи, а након тога умиру. 4Ко год је међу свим живима има наду, јер је и живом псу боље него угинулом лаву.

5Живи знају да ће умрети,

а умрли не знају ништа;

награде за њих више нема

јер је ишчезнуо спомен на њих.

6Одавно су пропале њихове љубави,

мржње и зависти,

немају више удела довека

у свему што се дешава под капом небеском.

7Хајде, радосно хлеб свој једи, пиј своје вино с милином у срцу, јер је Бог већ прихватио дела твоја! 8Нека ти одећа увек бела буде и нека ти уља на глави увек буде. 9Са женом коју волиш уживај кроз све дане свог пролазног живота који ти је дан под капом небеском у свим твојим пролазним данима. Јер ти је то награда у животу за твој труд који улажеш под капом небеском. 10Чега год ти латиле се руке, чини колико можеш, јер нема деловања и расуђивања, знања и мудрости у Свету мртвих9,10 У изворном тексту Шеол, или подземље, где пребивају душе умрлих. у који идеш.

11Размишљао сам и видео да под капом небеском:

брзи не побеђује у трци

ни јаки у боју;

мудар не добија хлеба

ни паметан богатство;

најученијем не следује наклоност.

Сваког стигну и време и догађаји.

12Човек не зна своје време,

попут рибе ухваћене у мрежу зла

и попут птице ухваћене у замку.

Да, попут њих су заробљени људи,

у зао час који се на њих ненадано спушта.

Мудрост је боља од лудости

13Елем, под капом небеском видео сам и ову мудрост која ми се учинила важном: 14Мали град, у њему тек нешто житеља, а велики цар га напада, опкољава и против њега диже велике насипе. 15Тек, у граду се нашао сиромашан, али мудар човек, који је мудрошћу спасао град. Па опет нико не памти тог сиромаха. 16Зато сам рекао да је мудрост боља од силе, али мудрост сиромаха је презрена и његове речи нису послушали.

17Боље се чују тихе речи мудрих

од владаревог повика међу безумницима.

18Мудрост је боља од ратног оружја,

а један грешник може да упропасти много доброг.