Mlaliki 6 – CCL & HCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 6:1-12

1Ine ndinaona choyipa china pansi pano, ndipo chimasautsa anthu kwambiri: 2Mulungu amapereka chuma, zinthu ndi ulemu kwa munthu, kotero kuti munthuyo sasowa kanthu kalikonse kamene akukalakalaka, koma Mulungu samulola kuti adyerere zinthuzo, ndipo mʼmalo mwake amadyerera ndi mlendo. Izi ndi zopandapake, ndi zoyipa kwambiri.

3Ngakhale munthu atabereka ana 100 ndi kukhala ndi moyo zaka zambiri; komatu ngakhale atakhala zaka zambiri chotani, ngati iye sangadyerere chuma chake ndi kuyikidwa mʼmanda mwaulemu, ine ndikuti mtayo umamuposa iyeyo. 4Mtayo umangopita pachabe ndipo umapita mu mdima, ndipo mu mdimamo dzina lake limayiwalika. 5Ngakhale kuti mtayowo sunaone dzuwa kapena kudziwa kanthu kalikonse, koma umapumula kuposa munthu uja, 6ngakhale munthuyo atakhala ndi moyo zaka 2,000, koma ndi kulephera kudyerera chuma chake. Kodi onsewa sapita malo amodzi?

7Ntchito yonse ya munthu imathera pakamwa pake,

komatu iye sakhutitsidwa ndi pangʼono pomwe.

8Kodi munthu wanzeru

amaposa motani chitsiru?

Kodi munthu wosauka amapindula chiyani

podziwa kukhala bwino pamaso pa anthu ena?

9Kuli bwino kumangoona zinthu ndi maso

kusiyana ndi kumangozilakalaka mu mtima.

Izinso ndi zopandapake,

nʼkungodzivuta chabe.

10Chilichonse chimene chilipo anachitchula kale dzina,

za mmene munthu alili nʼzodziwika;

sangathe kutsutsana ndi munthu

amene ali wamphamvu kupambana iyeyo.

11Mawu akachuluka

zopandapake zimachulukanso,

nanga munthu zimamupindulira chiyani?

12Pakuti ndani amene amadziwa chomwe ndi chabwino pa moyo wa munthu, pakuti moyo wake ndi wa masiku ochepa ndi opandapake, umangopitira ngati mthunzi. Ndani amene angamufotokozere zimene zidzachitika pansi pano iye atapita?

Hindi Contemporary Version

उद्बोधक 6:1-12

1मैंने सूरज के नीचे एक बुरी बात देखी जो मनुष्य पर बहुत अधिक हावी है. 2एक व्यक्ति जिसे परमेश्वर ने धन-संपत्ति और सम्मान दिया है जिससे उसे उस किसी भी वस्तु की कमी न हो जिसे उसका मन चाहता है; मगर परमेश्वर ने उसे उनको इस्तेमाल करने की समझ नहीं दी, उनका आनंद तो एक विदेशी लेता है. यह बेकार और बड़ी ही बुरी बात है.

3यदि एक व्यक्ति सौ पुत्रों का पिता है और वह बहुत साल जीवित रहता है, चाहे उसकी आयु के साल बहुत हों, पर अगर वह अपने जीवन भर में अच्छी वस्तुओं का इस्तेमाल नहीं करता और उसे क्रिया-कर्म ही नहीं किया गया तो मेरा कहना तो यही है कि एक मरा हुआ जन्मा बच्चा उस व्यक्ति से बेहतर है, 4क्योंकि वह बच्चा बेकार में आता है और अंधेरे में चला जाता है. अंधेरे में उसका नाम छिपा लिया जाता है. 5उस बच्‍चे ने सूरज को नहीं देखा और न ही उसे कुछ मालूम ही हुआ था. वह बच्चा उस व्यक्ति से कहीं अधिक बेहतर है. 6दो बार जिसका जीवन दो हज़ार साल का हो मगर उस व्यक्ति ने किसी अच्छी वस्तु का इस्तेमाल न किया हो, क्या सभी लोग एक ही जगह पर नहीं जाते?

7मनुष्य की सारी मेहनत उसके भोजन के लिए ही होती है,

मगर उसका मन कभी संतुष्ट नहीं होता.

8बुद्धिमान को निर्बुद्धि से क्या लाभ?

और गरीब को यह मालूम होने से

क्या लाभ कि उसे बुद्धिमानों के सामने कैसा व्यवहार करना है?

9आंखों से देख लेना

इच्छा रखने से कहीं अधिक बेहतर है.

मगर यह भी बेकार ही है,

सिर्फ हवा को पकड़ने की कोशिश.

10जो हो चुका है उसका नाम भी रखा जा चुका है,

और यह भी मालूम हो चुका है कि मनुष्य क्या है?

मनुष्य उस व्यक्ति पर हावी नहीं हो सकता

जो उससे बलवान है.

11शब्द जितना अधिक है,

अर्थ उतना कम होता है.

इससे मनुष्य को क्या फायदा?

12जिसे यह मालूम है कि उसके पूरे जीवन में मनुष्य के लिए क्या अच्छा है, अपने उस व्यर्थ जीवन के थोड़े से सालों में. वह एक परछाई के समान उन्हें बिता देगा. मनुष्य को कौन बता सकता है कि सूरज के नीचे उसके बाद क्या होगा?