Mlaliki 4 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 4:1-16

Matsoka ndi Mavuto a Moyo Uno

1Ndinayangʼananso ndi kuona chipsinjo chimene chimachitika pansi pano:

ndinaona misozi ya anthu opsinjika,

ndipo iwo alibe owatonthoza;

mphamvu zinali ndi anthu owapsinjawo

ndipo iwonso analibe owatonthoza.

2Ndipo ndinanena kuti akufa,

amene anafa kale,

ndi osangalala kuposa amoyo,

amene akanalibe ndi moyo.

3Koma wopambana onsewa

ndi amene sanabadwe,

amene sanaone zoyipa

zimene chimachitika pansi pano.

4Ndipo ndinazindikira kuti ntchito zonse zolemetsa ndiponso ntchito zonse zaluso zimachitika chifukwa choti wina akuchitira nsanje mnzake. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.

5Chitsiru chimangoti manja ake lobodo

ndi kudzipha chokha ndi njala.

6Nʼkwabwino kukhala ndi dzanja limodzi lodzaza uli pa mtendere,

kuposa kukhala ndi manja awiri odzaza uli pa mavuto,

ndipo uku nʼkungodzivuta chabe.

7Ndinaonanso chinthu china chopanda phindu pansi pano:

8Panali munthu amene anali yekhayekha;

analibe mwana kapena mʼbale.

Ntchito yake yolemetsa sinkatha,

ndipo maso ake sankakhutitsidwa ndi chuma chake.

Iye anadzifunsa kuti, “Kodi ntchito yosautsayi ndikuyigwirira yani?

Nanga nʼchifukwa chiyani ndikudzimana chisangalalo?”

Izinso ndi zopandapake,

zosasangalatsa!

9Kukhala awiri nʼkwabwino kuposa kukhala wekha,

chifukwa ntchito ya anthu awiri ili ndi phindu:

10Ngati winayo agwa,

mnzakeyo adzamudzutsa.

Koma tsoka kwa munthu amene agwa

ndipo alibe wina woti amudzutse!

11Komanso ngati anthu awiri agona malo amodzi, adzafunditsana.

Koma nanga mmodzi angadzifunditse yekha?

12Munthu mmodzi angathe kugonjetsedwa,

koma anthu awiri akhoza kudziteteza.

Chingwe cha maulusi atatu sichidukirapo.

Kutukuka Nʼkopandapake

13Wachinyamata wosauka koma wanzeru aposa mfumu yokalamba koma yopusa imene simvanso malangizo. 14Wachinyamatayo angathe kuchokera ku ndende ndi kudzakhala mfumu, kapena angathe kubadwa wosauka mʼdziko la mfumuyo. 15Ndipo ndinaona kuti iwo onse amene anakhala ndi moyo ndi kuyenda pansi pano anatsatira wachinyamatayo, amene anatenga malo a mfumu. 16Mfumu ikhoza kulamulira anthu osawerengeka, komabe itamwalira, palibe amene adzayamikire zomwe mfumuyo inachita. Izinso ndi zopandapake, nʼkungozivuta chabe.

Persian Contemporary Bible

جامعه 4:1-16

ظلم، زحمت و تنهايی

1سپس ظلمهايی را که در زير اين آسمان می‌شد مشاهده كردم. اشكهای مظلومانی را ديدم كه فريادرسی نداشتند. قدرت در دست ظالمان بود و كسی نبود كه به داد مظلومان برسد. 2پس گفتم كسانی كه قبل از ما مرده‌اند از آنانی كه هنوز زنده‌اند خوشبخت‌ترند؛ 3و خوشبخت‌تر از همه كسانی هستند كه هنوز به دنيا نيامده‌اند، زيرا ظلمهايی را كه زير اين آسمان می‌شود نديده‌اند.

4همچنين متوجه شدم كه به سبب حسادت است كه مردم تلاش می‌كنند موفقيت كسب كنند. اين نيز مانند دويدن به دنبال باد، بيهوده است. 5كسی كه دست روی دست می‌گذارد و گرسنگی می‌كشد، احمق است؛ 6اما كسی هم كه دائم مشغول كار است و تلاش می‌كند ثروت بيشتری به دست آورد به دنبال باد می‌دود. بهتر است انسان يک لقمه نان به دست آورد و با آسودگی بخورد.

7و نيز در زير آسمان بيهودگی ديگری ديدم: 8مردی بود كه تنها زندگی می‌كرد؛ نه پسری داشت و نه برادری. با اين حال سخت تلاش می‌كرد و از اندوختن مال و ثروت سير نمی‌شد. او برای چه كسی زحمت می‌كشيد و خود را از لذات زندگی محروم می‌كرد؟ اين نيز رنج و زحمت بيهوده‌ای است.

9دو نفر از يک نفر بهترند، زيرا نفع بيشتری از كارشان عايدشان می‌شود. 10اگر يكی از آنها بيفتد، ديگری او را بلند می‌كند؛ اما چه بيچاره است شخصی كه می‌افتد ولی كسی را ندارد كه به او كمک كند. 11وقتی دو نفر كنار هم می‌خوابند، گرم می‌شوند؛ اما كسی كه تنهاست چطور می‌تواند خود را گرم كند؟ 12اگر شخص، تنها باشد و كسی بر او حمله كند، از پای درمی‌آيد، اما اگر دو نفر باشند می‌توانند از خود دفاع كنند. ريسمان سه لا به آسانی پاره نمی‌شود.

بيهودگی ترقی

13يک جوان فقير و حكيم بهتر از پادشاه پير و نادانی است كه نصيحت نمی‌پذيرد. 14چنين جوان فقيری حتی ممكن است از كنج زندان به تخت پادشاهی برسد. 15مردمی كه زير اين آسمان زندگی می‌كنند از چنين جوانی كه جانشين پادشاه شده است حمايت می‌نمايند. 16او می‌تواند بر عدهٔ زيادی حكومت كند؛ اما نسل بعدی، او را نيز بركنار می‌كند! اين نيز مانند دويدن به دنبال باد، بيهوده است.