Zapansipano Nʼzopandapake
1Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
2“Zopandapake! Zopandapake!”
atero Mlaliki.
“Zopandapake kotheratu!
Zopandapake.”
3Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse
zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
4Mibado imabwera ndipo mibado imapita,
koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
5Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa
ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
6Mphepo imawombera cha kummwera
ndi kukhotera cha kumpoto;
imawomba mozungulirazungulira,
kumangobwererabwerera komwe yachokera.
7Mitsinje yonse imakathira ku nyanja,
koma nyanjayo sidzaza;
kumene madziwo amachokera,
amabwereranso komweko.
8Zinthu zonse ndi zotopetsa,
kutopetsa kwake ndi kosaneneka.
Maso satopa ndi kuona
kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
9Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso,
zomwe zinachitika kale zidzachitikanso.
Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
10Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti,
“Taona! Ichi ndiye chatsopano?”
Chinalipo kale, kalekale;
chinalipo ife kulibe.
11Anthu akale sakumbukiridwa,
ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu
sadzakumbukiridwa ndi iwo
amene adzabwere pambuyo pawo.
Nzeru Nʼzopandapake
12Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu. 13Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu! 14Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
15Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa;
chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
16Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.” 17Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
18Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso:
chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.
ทุกสิ่งล้วนอนิจจัง
1ถ้อยคำของปัญญาจารย์1:1 หรือผู้นำของชุมชนเช่นเดียวกับข้อ 2 และ 12 กษัตริย์ในเยรูซาเล็ม เชื้อสายดาวิด
2ปัญญาจารย์กล่าวว่า
“อนิจจัง! อนิจจัง!
อนิจจังแท้ๆ!
ทุกสิ่งล้วนอนิจจัง”
3มนุษย์ได้ประโยชน์อะไรจากการงานทั้งสิ้น
ที่เขาตรากตรำภายใต้ดวงอาทิตย์?
4คนรุ่นหนึ่งผ่านมาแล้วอีกรุ่นหนึ่งผ่านไป
แต่โลกยังคงอยู่ตลอดกาล
5ดวงอาทิตย์ขึ้นแล้วก็ลับไป
และรีบวนมาขึ้นที่เดิมอีก
6ลมพัดไปทางใต้แล้ว
กลับมาทางเหนือ
มันพัดวนไปเวียนมา
เป็นวัฏจักร
7แม่น้ำไหลลงสู่ทะเล
แต่ทะเลก็ไม่เคยอิ่ม
และน้ำกลับไปสู่แม่น้ำอีกครั้ง
แล้วไหลลงสู่มหาสมุทรอยู่ร่ำไป
8ทุกสิ่งทุกอย่างอ่อนระโหย
เกินที่จะบรรยาย
ไม่ว่าเห็นสักเท่าไร เราก็ไม่อิ่ม
ไม่ว่าได้ยินสักแค่ไหน เราก็ไม่จุใจ
9อะไรที่เกิดขึ้นแล้วก็เกิดขึ้นอีก
สิ่งที่ทำไปแล้วก็ทำกันอีก
ไม่มีอะไรใหม่ภายใต้ดวงอาทิตย์
10อะไรบ้างที่เราจะบอกได้ว่า
“ดูเถิด นี่เป็นสิ่งใหม่”
เพราะมันมีมาตั้งนานแล้ว
มีมาตั้งแต่ก่อนยุคสมัยของเรา
11ไม่มีการระลึกถึงคนรุ่นก่อน
และแม้แต่คนรุ่นที่กำลังจะเกิดมา
คนรุ่นต่อจากเขา
ก็ยังไม่ระลึกถึงพวกเขา
สติปัญญาอนิจจัง
12ข้าพเจ้าปัญญาจารย์ เป็นกษัตริย์ปกครองอิสราเอลอยู่ในเยรูซาเล็ม 13ได้ทุ่มเทศึกษาและใช้สติปัญญาใคร่ครวญทุกสิ่งที่ทำกันใต้ฟ้าสวรรค์ พระเจ้าทรงวางภาระหนักแก่มนุษย์จริงๆ! 14ข้าพเจ้าได้เห็นทุกสิ่งซึ่งทำกันภายใต้ดวงอาทิตย์ ล้วนแต่อนิจจังเหมือนวิ่งไล่ตามลม
15สิ่งที่คดงอก็ทำให้เหยียดตรงไม่ได้
สิ่งที่ขาดอยู่ก็นับไม่ได้
16ข้าพเจ้ารำพึงว่า “ดูเถิด เรามีสติปัญญามากกว่ากษัตริย์องค์ก่อนๆ ที่ครองเยรูซาเล็ม เราเข้าถึงสติปัญญาและความรู้” 17แล้วข้าพเจ้าก็ทุ่มเทสุดตัวที่จะเข้าใจสติปัญญา ความบ้าคลั่ง และความโฉดเขลาด้วย แต่ได้เรียนรู้ว่านี่ก็วิ่งไล่ตามลมเช่นกัน
18เพราะยิ่งฉลาดมากก็ยิ่งโศกเศร้ามาก
ยิ่งรู้ก็ยิ่งทุกข์โศก