Zapansipano Nʼzopandapake
1Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
2“Zopandapake! Zopandapake!”
atero Mlaliki.
“Zopandapake kotheratu!
Zopandapake.”
3Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse
zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
4Mibado imabwera ndipo mibado imapita,
koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
5Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa
ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
6Mphepo imawombera cha kummwera
ndi kukhotera cha kumpoto;
imawomba mozungulirazungulira,
kumangobwererabwerera komwe yachokera.
7Mitsinje yonse imakathira ku nyanja,
koma nyanjayo sidzaza;
kumene madziwo amachokera,
amabwereranso komweko.
8Zinthu zonse ndi zotopetsa,
kutopetsa kwake ndi kosaneneka.
Maso satopa ndi kuona
kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
9Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso,
zomwe zinachitika kale zidzachitikanso.
Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
10Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti,
“Taona! Ichi ndiye chatsopano?”
Chinalipo kale, kalekale;
chinalipo ife kulibe.
11Anthu akale sakumbukiridwa,
ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu
sadzakumbukiridwa ndi iwo
amene adzabwere pambuyo pawo.
Nzeru Nʼzopandapake
12Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu. 13Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu! 14Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
15Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa;
chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
16Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.” 17Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
18Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso:
chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.
بيهودگی زندگی
1اينها سخنان پسر داوود است كه در اورشليم سلطنت میكرد و به «حكيم» معروف بود:
2بيهودگی است! بيهودگی است! زندگی، سراسر بيهودگی است! 3آدمی از تمامی زحماتی كه در زير آسمان میكشد چه نفعی عايدش میشود؟ 4نسلها يكی پس از ديگری میآيند و میروند، ولی دنيا همچنان باقی است. 5آفتاب طلوع میكند و غروب میكند و باز با شتاب به جايی باز میگردد كه بايد از آن طلوع كند. 6باد به طرف جنوب میوزد، و از آنجا به طرف شمال دور میزند. میوزد و میوزد و باز به جای اول خود باز میگردد. 7آب رودخانهها به دريا میريزد، اما دريا هرگز پر نمیشود. آبها دوباره به رودخانهها باز میگردند و باز روانه دريا میشوند.
8همه چيز خسته كننده است. آنقدر خسته كننده كه زبان از وصف آن قاصر است. نه چشم از ديدن سير میشود و نه گوش از شنيدن. 9آنچه بوده باز هم خواهد بود، و آنچه شده باز هم خواهد شد. زير آسمان هيچ چيز تازهای وجود ندارد. 10آيا چيزی هست كه دربارهاش بتوان گفت: «اين تازه است»؟ همه چيز پيش از ما، از گذشتههای دور وجود داشته است. 11يادی از گذشتگان نيست. آيندگان نيز از ما ياد نخواهند كرد.
بيهودگی حكمت
12من كه «حكيم»1:12 «حکيم» نگاه کنيد به آيهٔ 1. هستم، در اورشليم بر اسرائيل سلطنت میكردم. 13با حكمت خود، سخت به مطالعه و تحقيق دربارهٔ هر چه در زير آسمان انجام میشود پرداختم. اين چه كار سخت و پرزحمتی است كه خدا به عهدهٔ انسان گذاشته است!
14هر چه را كه زير آسمان انجام میشود ديدهام. همه چيز بيهوده است، درست مانند دويدن به دنبال باد! 15كج را نمیتوان راست كرد و چيزی را كه نيست نمیتوان به شمار آورد.
16با خود فكر كردم: «من از همهٔ پادشاهانی كه پيش از من در اورشليم بودهاند، حكيمتر هستم و حكمت و دانش بسيار كسب كردهام.» 17در صدد برآمدم فرق بين حكمت و حماقت، و دانش و جهالت را بفهمم؛ ولی دريافتم كه اين نيز مانند دويدن به دنبال باد، كار بيهودهای است. 18انسان هر چه بيشتر حكمت میآموزد محزونتر میشود و هر چه بيشتر دانش میاندوزد، غمگينتر میگردد.