Zapansipano Nʼzopandapake
1Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
2“Zopandapake! Zopandapake!”
atero Mlaliki.
“Zopandapake kotheratu!
Zopandapake.”
3Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse
zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
4Mibado imabwera ndipo mibado imapita,
koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
5Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa
ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
6Mphepo imawombera cha kummwera
ndi kukhotera cha kumpoto;
imawomba mozungulirazungulira,
kumangobwererabwerera komwe yachokera.
7Mitsinje yonse imakathira ku nyanja,
koma nyanjayo sidzaza;
kumene madziwo amachokera,
amabwereranso komweko.
8Zinthu zonse ndi zotopetsa,
kutopetsa kwake ndi kosaneneka.
Maso satopa ndi kuona
kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
9Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso,
zomwe zinachitika kale zidzachitikanso.
Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
10Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti,
“Taona! Ichi ndiye chatsopano?”
Chinalipo kale, kalekale;
chinalipo ife kulibe.
11Anthu akale sakumbukiridwa,
ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu
sadzakumbukiridwa ndi iwo
amene adzabwere pambuyo pawo.
Nzeru Nʼzopandapake
12Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu. 13Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu! 14Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
15Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa;
chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
16Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.” 17Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
18Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso:
chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.
Nada Tem Sentido
1As palavras do mestre, filho de Davi, rei em Jerusalém:
2“Que grande inutilidade!”,
diz o mestre.
“Que grande inutilidade!
Nada faz sentido!”
3O que o homem ganha com todo o seu trabalho
em que tanto se esforça debaixo do sol?
4Gerações vêm e gerações vão,
mas a terra permanece para sempre.
5O sol se levanta e o sol se põe e depressa volta
ao lugar de onde se levanta.
6O vento sopra para o sul
e vira para o norte;
dá voltas e voltas,
seguindo sempre o seu curso.
7Todos os rios vão para o mar,
contudo, o mar nunca se enche;
ainda que sempre corram para lá,
para lá voltam a correr.
8Todas as coisas trazem canseira.
O homem não é capaz de descrevê-las;
os olhos nunca se saciam de ver,
nem os ouvidos de ouvir.
9O que foi tornará a ser,
o que foi feito se fará novamente;
não há nada novo debaixo do sol.
10Haverá algo de que se possa dizer:
“Veja! Isto é novo!”?
Não! Já existiu há muito tempo,
bem antes da nossa época.
11Ninguém se lembra dos que viveram na antiguidade,
e aqueles que ainda virão
tampouco serão lembrados
pelos que vierem depois deles.1.11 Ou Não há lembrança do que aconteceu, e mesmo o que ainda acontecerá não será lembrado pelos que vierem depois disso.
A Sabedoria Não Tem Sentido
12Eu, o mestre, fui rei de Israel em Jerusalém. 13Dediquei-me a investigar e a usar a sabedoria para explorar tudo o que é feito debaixo do céu. Que fardo pesado Deus pôs sobre os homens! 14Tenho visto tudo o que é feito debaixo do sol; tudo é inútil, é correr atrás do vento!
15O que é torto não pode ser endireitado;
o que está faltando não pode ser contado.
16Fiquei pensando: Eu me tornei famoso e ultrapassei em sabedoria todos os que governaram Jerusalém antes de mim; de fato adquiri muita sabedoria e conhecimento.
17Por isso me esforcei para compreender a sabedoria, bem como a loucura e a insensatez, mas aprendi que isso também é correr atrás do vento.
18Pois quanto maior a sabedoria, maior o sofrimento;
e quanto maior o conhecimento, maior o desgosto.