Zapansipano Nʼzopandapake
1Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
2“Zopandapake! Zopandapake!”
atero Mlaliki.
“Zopandapake kotheratu!
Zopandapake.”
3Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse
zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
4Mibado imabwera ndipo mibado imapita,
koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
5Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa
ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
6Mphepo imawombera cha kummwera
ndi kukhotera cha kumpoto;
imawomba mozungulirazungulira,
kumangobwererabwerera komwe yachokera.
7Mitsinje yonse imakathira ku nyanja,
koma nyanjayo sidzaza;
kumene madziwo amachokera,
amabwereranso komweko.
8Zinthu zonse ndi zotopetsa,
kutopetsa kwake ndi kosaneneka.
Maso satopa ndi kuona
kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
9Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso,
zomwe zinachitika kale zidzachitikanso.
Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
10Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti,
“Taona! Ichi ndiye chatsopano?”
Chinalipo kale, kalekale;
chinalipo ife kulibe.
11Anthu akale sakumbukiridwa,
ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu
sadzakumbukiridwa ndi iwo
amene adzabwere pambuyo pawo.
Nzeru Nʼzopandapake
12Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu. 13Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu! 14Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
15Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa;
chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
16Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.” 17Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
18Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso:
chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.
Всё – пустое
1Слова Учителя1:1 Букв.: «Екклесиаста». Слово «екклесиаст» с языка оригинала можно перевести и как «возглавляющий собрание» или «проповедник»., сына Давуда, царя в Иерусалиме.
2«Пустое!1:2 Слово, стоящее здесь в оригинале, переводится как «дуновение ветра», «выдох» и означает что-то бессмысленное, ничтожное и мимолётное. Пустое! –
сказал Учитель. –
Всё бессмысленно,
всё пустое!»
3Что приобретает человек от всех трудов своих,
которые он делает под солнцем?
4Поколения приходят и уходят,
а земля остаётся навеки.
5Солнце всходит, и солнце заходит,
и вновь спешит к месту своего восхода.
6Летит ветер на юг,
потом направляется к северу,
кружится, кружится
и возвращается на свои круги.
7Все реки текут в море,
но море не переполняется.
И возвращаются реки к своим истокам,
чтобы течь снова.
8Все эти вещи утомляют:
человек не может всё пересказать,
глаз не насытится тем, что видит,
ухо не наполнится тем, что слышит.
9Что было, то и будет,
и что делалось, то и будет делаться опять.
Нет ничего нового под солнцем!
10Бывает такое, о чём говорят:
«Смотри, вот что-то новое!»
Но и это уже бывало в прежние времена,
ещё задолго до нас.
11Никто не помнит о живших прежде,
и о тех, кто ещё не родился,
не вспомнят те, кто будет жить после них.
Мудрость – пуста
12Я, Учитель, был царём над Исраилом в Иерусалиме. 13Я решил изучить и испытать мудростью всё, что делается под небом. Это тяжёлое бремя, которое Всевышний возложил на людей. 14Я видел всё, что делается под солнцем, и всё – пустое, всё – погоня за ветром1:14 Или: «томление духа». Также в остальных местах этой книги..
15Кривое не выпрямить,
а чего нет, того не сосчитать.
16Я сказал себе: «Величием и мудростью я превзошёл всех, кто правил Иерусалимом до меня. Я приобрёл много мудрости и знаний». 17Затем я решил узнать, в чём мудрость, а также в чём безумие и глупость, но понял, что и это погоня за ветром.
18Ведь с большой мудростью приходит много печали,
и чем больше знаний, тем больше скорбь.