Miyambo 8 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 8:1-36

Nzeru Ikuyitana

1Kodi nzeru sikuyitana?

Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?

2Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira,

imayima pa mphambano ya misewu.

3Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda,

pa makomo olowera imafuwula kuti,

4Inu anthu, ndikuyitana inu;

ndikuyitanatu anthu onse.

5Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera;

inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.

6Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri;

ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.

7Pakamwa panga pamayankhula zoona

ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.

8Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama;

mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.

9Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona;

kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.

10Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva,

nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.

11Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali,

ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.

12Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera.

Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.

13Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa.

Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama,

kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.

14Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino;

ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.

15Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira.

Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.

16Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula.

Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.

17Ndimakonda amene amandikonda,

ndipo amene amandifunafuna amandipeza.

18Ine ndili ndi chuma ndi ulemu,

chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.

19Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala;

zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.

20Ndimachita zinthu zolungama.

Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.

21Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda

ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.

22“Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba.

Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.

23Ndinapangidwa kalekalelo,

pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.

24Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi,

zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.

25Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo,

mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,

26lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake;

lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.

27Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga,

pamene ankalemba malire a nyanja yozama,

28pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga

ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,

29pamene anayikira nyanja malire

kuti madzi asadutse malirewo,

ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.

30Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri;

ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku,

kusangalala nthawi zonse pamaso pake.

31Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse

ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”

32“Ndiye tsono ana inu, ndimvereni;

odala anthu amene amasunga njira zanga.

33Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru;

musanyozere mawu anga.

34Wodala munthu amene amandimvera,

amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku,

kudikirira pa chitseko changa.

35Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo

ndipo Yehova amamukomera mtima.

36Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha;

onse amene amandida amakonda imfa.”

Hoffnung für Alle

Sprüche 8:1-36

Die Weisheit ruft

1Hört! Die Weisheit ruft, und die Einsicht lässt ihre Stimme erschallen! 2-3Man sieht sie auf allen Straßen und Plätzen, an den Toren der Stadt – dort, wo jeder sie sehen kann – steht sie und ruft:

4»Hört her, ja, ich meine euch alle!

5Ihr Unerfahrenen, werdet reif und vernünftig!

Ihr Dummköpfe, nehmt doch endlich Verstand an!

6Hört auf mich, denn von mir bekommt ihr guten Rat.

Auf meine Worte ist Verlass.

7Ich halte mich immer an die Wahrheit,

denn gottloses Gerede ist mir zuwider.

8Alles, was ich sage, ist ehrlich;

Hinterlist oder Betrug sind mir fremd.

9Meine Worte sind klar und deutlich

für jeden, der sie verstehen will.

10Darum nehmt meine Ermahnung an,

achtet sie mehr als Silber oder Gold.

11Weisheit ist wertvoller als die kostbarste Perle,

sie übertrifft alles, was ihr euch erträumt.

12Ich bin die Weisheit,

und zu mir gehört die Klugheit.

Ich handle überlegt und besonnen.

13Wer Ehrfurcht vor dem Herrn hat, der hasst das Böse.

Ich verachte Stolz und Hochmut,

ein Leben voller Bosheit und Lüge ist mir ein Gräuel!

14Ich stehe euch mit Rat und Tat zur Seite,

ich verleihe Klugheit und Macht.

15Mit meiner Hilfe regieren Könige

und erlassen Staatsmänner gerechte Gesetze.

16Alle Machthaber der Welt, alle, die für das Recht sorgen,

können nur durch mich regieren.

17Ich liebe den, der mich liebt;

wer sich um mich bemüht, der wird mich finden.

18Ansehen und Reichtum biete ich an,

bleibenden Besitz und Erfolg.

19Was ihr von mir bekommt,

ist wertvoller als das feinste Gold,

besser als das reinste Silber.

20Wo Menschen gerecht miteinander umgehen

und nach Gottes Willen fragen, da bin ich zu Hause;

21alle, die mich lieben, beschenke ich mit Reichtum;

ja, es fehlt ihnen an nichts!

22Der Herr schuf mich vor langer Zeit,

ich war sein erstes Werk, noch vor allen anderen.

23In grauer Vorzeit hat er mich gebildet;

und so war ich schon da, als es die Erde noch gar nicht gab.

24Lange bevor das Meer entstand, wurde ich geboren.

Zu dieser Zeit gab es noch keine Quellen,

25und es standen weder Berge noch Hügel.

26Ich war schon da,

bevor Gott die Erde mit ihren Wiesen und Feldern erschuf,

ja, noch vor dem ersten Staubkorn.

27Ich war dabei,

als Gott den Himmel formte,

als er den Horizont aufspannte über dem Ozean,

28als die Wolken entstanden

und die Quellen aus der Tiefe hervorsprudelten,

29als er das Meer in die Schranken wies,

die das Wasser nicht überschreiten durfte,

als er das Fundament der Erde legte –

30da war ich ständig an seiner Seite.

Tag für Tag erfreute ich mich an Gott und seinen Werken,

31ich tanzte vor Freude auf seiner Erde

und war glücklich über die Menschen.

32Darum hört auf mich, ihr jungen Männer!

Richtet euch nach mir, und ihr werdet glücklich.

33Nehmt Belehrung an

und weist sie nicht zurück, dann werdet ihr klug!

34Glücklich ist, wer auf mich hört

und jeden Tag erwartungsvoll vor meiner Tür steht!

35Wer mich findet, der findet das Leben,

und an einem solchen Menschen hat der Herr Gefallen.

36Wer mich aber verachtet,

der zerstört sein Leben;

wer mich hasst, der liebt den Tod.«