Miyambo 27 – CCL & JCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 27:1-27

1Usamanyadire za mawa,

pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.

2Munthu wina akutamande, koma osati wekha;

mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.

3Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri,

koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.

4Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa.

Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.

5Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino

kuposa chikondi chobisika.

6Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino,

koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.

7Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi,

koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.

8Munthu amene wasochera ku nyumba kwake,

ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.

9Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima,

ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.

10Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako,

ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto;

mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.

11Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga;

pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.

12Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala,

koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.

13Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole;

ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.

14Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri,

anthu adzamuyesa kuti akutemberera.

15Mkazi wolongolola ali ngati

mvula yamvumbi.

16Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo

kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.

17Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake,

chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.

18Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake,

ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.

19Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi,

chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.

20Manda sakhuta,

nawonso maso a munthu sakhuta.

21Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo,

chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.

22Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo

ndi musi ngati chimanga,

uchitsiru wakewo sudzachoka.

23Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili.

Kodi usamalire bwino ziweto zako?

24Paja chuma sichikhala mpaka muyaya,

ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.

25Pamene udzu watha, msipu nʼkumera;

ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,

26ana ankhosa adzakupatsani chovala

ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.

27Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri

kuti muzidya inuyo ndi banja lanu

ndi kudyetsa antchito anu aakazi.

Japanese Contemporary Bible

箴言 知恵の泉 27:1-27

27

1今日一日、何が起こるかわからないのに、

明日の予定を得意になって話してはいけません。

2自分で自分をほめるより、

人からほめられるようにしなさい。

3神に背く者は、思いどおりにならないと

腹を立て、手のつけようがありません。

4怒られるよりも、嫉妬されるほうが怖いものです。

5愛するあまり、

悪いことをしても何も注意しないより、

しかるときははっきりしかるほうがよいのです。

6敵にうわべだけ親切にされるより、

友に傷つけられるほうがましです。

7腹がいっぱいだと、

どんなごちそうもまずく感じますが、

腹がすいていると何でもおいしく食べられます。

8家を離れてあちこち渡り歩く人は、

巣を離れてさまよう鳥のようです。

9友に励まされるのは、

香水をつけたように気持ちのよいものです。

10自分の友でも父の友人でも、

彼らを大事にしなさい。

いざというとき、

遠くの親類よりあてになります。

11わが子よ。知恵のある人間になりなさい。

そうすれば、

私もどんなに鼻が高いことでしょう。

12何かを始めるとき、

思慮深い人はきちんと見通しを立てますが、

考えの足りない人は

向こう見ずに手をつけて失敗します。

13見ず知らずの人の借金を立て替える以上に

危ない賭けはありません。

14朝まだ暗いうちに大声であいさつすると、

いやがられます。

15気むずかしい女は、

いつまでもしたたり続ける雨もりのようです。

16風を止めることも、油でぬるぬるした手で

物をつかむこともできないように、

彼女のぐちを止めることはできません。

17鉄が鉄によって研がれるように、

友との熱のこもった議論は、

互いを研ぎ合います。

18果樹園の番人がそこの果物を頂けるように、

主人のために働く者が報酬を受けるのは当然です。

19顔を映すのは鏡ですが、

人のほんとうの心は、

その人がどんな友を選ぶかでわかります。

20野心と死には終わりがありません。

21銀と金の純度はるつぼで試され、

人は、称賛を浴びるときに試されます。

22神の教えに背く愚か者につける薬はありません。

23-24財産はすぐになくなり、

王位はいつまでも続きません。

だから自分の収入や、家畜の状態を知っておきなさい。

25-27牧草を刈り取り、二番草も刈り取ったあと、

山の草を集めなさい。

そうすれば、子羊の毛もやぎの乳も十分に取れ、

家族の生活に困りません。