Miyambo 25 – CCL & HCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 25:1-28

Miyambo Ina ya Solomoni

1Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.

2Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu;

ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.

3Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi,

ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.

4Chotsa zoyipa mʼsiliva

ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.

5Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu;

ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.

6Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu,

ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;

7paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,”

kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa.

Chimene wachiona ndi maso ako,

8usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu

nanga udzachita chiyani pa mapeto pake

ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?

9Kamba mlandu ndi mnansi wako,

koma osawulula chinsinsi cha munthu wina

10kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi

ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.

11Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera

ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.

12Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide

kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.

13Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola

kwa anthu amene amutuma;

iye amaziziritsa mtima bwana wake.

14Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka

ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.

15Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu,

ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.

16Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira,

kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.

17Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako

ukawirikiza kupita, udzadana naye.

18Munthu wochitira mnzake umboni wonama,

ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.

19Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto,

kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.

20Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni

kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira

kapena kuthira mchere pa chilonda.

21Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye;

ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.

22Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake,

ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.

23Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula,

chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.

24Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga

kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.

25Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali

ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.

26Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa

ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.

27Sibwino kudya uchi wambiri,

sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.

28Munthu amene samatha kudziretsa

ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.

Hindi Contemporary Version

सूक्ति संग्रह 25:1-28

शलोमोन के कुछ और नीति वाक्य

1ये भी राजा शलोमोन के ही कुछ और नीति वाक्य हैं, जिन्हें यहूदिया राज्य के राजा हिज़किय्याह के लोगों ने तैयार किया है:

2परमेश्वर की महिमा इसमें है कि वह किसी विषय को गुप्‍त रख देते हैं;

जबकि राजा की महिमा किसी विषय की गहराई तक खोजने में होती है.

3जैसे आकाश की ऊंचाई और पृथ्वी की गहराई,

उसी प्रकार राजाओं का हृदय भी रहस्यमय होता है.

4चांदी में से खोट दूर कर दो,

तो चांदीकार के लिए शुद्ध चांदी शेष रह जाती है.

5राजा के सामने से दुष्टों को हटा दो,

तो राज सिंहासन धर्म में प्रतिष्ठित हो जाएगा.

6न तो राजा के समक्ष स्वयं को सम्मान्य प्रमाणित करो,

और न ही किसी प्रतिष्ठित व्यक्ति का स्थान लेने का प्रयास करो;

7क्योंकि उत्तम तो यह होगा कि राजा ही तुम्हें आमंत्रित कर यह कहे, “यहां मेरे पास आओ,”

इसकी अपेक्षा कि तुम्हें सब की दृष्टि में निम्नतर स्थान पर जाने का आदेश दिया जाए.

8मात्र इसलिये कि तुमने कुछ देख लिया है,

मुकदमा चलाने की उतावली न करना.

9विवादास्पद विषय पर सीधा उसी व्यक्ति से विचार-विमर्श कर लो,

और किसी अन्य व्यक्ति का रहस्य प्रकाशित न करना,

10कहीं ऐसा न हो कि कोई इसे सुन ले, यह तुम्हारे ही लिए लज्जा का कारण हो जाए

और तुम्हारी प्रतिष्ठा स्थायी रूप से नष्ट हो जाए.

11उचित अवसर पर कहा हुआ वचन चांदी के पात्र में

प्रस्तुत स्वर्ण के सेब के समान होता है.

12तत्पर श्रोता के लिए ज्ञानवान व्यक्ति की चेतावनी वैसी ही होती है

जैसे स्वर्ण कर्णफूल अथवा स्वर्ण आभूषण.

13कटनी के समय की उष्णता में ठंडे पानी के पेय के समान होता है,

प्रेषक के लिए वह दूत, जो विश्वासयोग्य है;

वह अपने स्वामी के हृदय को प्रफुल्लित कर देता है.

14बारिश के बिना बादलों और हवा की तरह है जो व्यक्ति उपहार तो देता नहीं,

किंतु सबके समक्ष देने की डींग मारता रहता है.

15धैर्य के द्वारा शासक को भी मनाया जा सकता है,

और कोमलता में कहे गए वचन से हड्डी को भी तोड़ा जा सकता है.

16यदि तुम्हें कहीं मधु प्राप्‍त हो जाए, तो उतना ही खाना, जितना पर्याप्‍त है,

सीमा से अधिक खाओगे तो, तुम उसे उगल दोगे.

17उत्तम तो यह होगा कि तुम्हारे पड़ोसी के घर में

तुम्हारे पैर कम ही पडे़ं, ऐसा न हो कि वह तुमसे ऊब जाए और तुमसे घृणा करने लगे.

18वह व्यक्ति, जो अपने पड़ोसी के विरुद्ध झूठा साक्षी हो जाता है,

वह युद्ध के लिए प्रयुक्त लाठी, तलवार अथवा बाण के समान है.

19विपदा के अवसर पर ऐसे व्यक्ति पर भरोसा रखना, जिस पर विश्वास नहीं किया जा सकता,

वैसा ही होता है, जैसे सड़े दांत अथवा टूटे पैर पर भरोसा रखना.

20दुःख में डूबे व्यक्ति के समक्ष हर्ष गीत गाने का वैसा ही प्रभाव होता है,

जैसा शीतकाल में किसी को विवस्त्र कर देना

अथवा किसी के घावों पर सिरका मल देना.

21यदि तुम्हारा विरोधी भूखा है, उसे भोजन कराओ,

यदि प्यासा है, उसे पीने के लिए जल दो;

22इससे तुम उसके सिर पर प्रज्वलित कोयलों का ढेर लगा दोगे,

और तुम्हें याहवेह की ओर से पारितोषिक प्राप्‍त होगा.

23जैसे उत्तरी वायु प्रवाह वृष्टि का उत्पादक होता है,

वैसे ही पीठ पीछे पर निंदा करती जीभ शीघ्र क्रोधी मुद्रा उत्पन्‍न करती है.

24विवादी पत्नी के साथ घर में निवास करने से कहीं अधिक श्रेष्ठ है

छत के एक कोने में रह लेना.

25दूर देश से आया शुभ संदेश वैसा ही होता है,

जैसा प्यासी आत्मा को दिया गया शीतल जल.

26वह धर्मी व्यक्ति, जो दुष्टों के आगे झुक जाता है,

गंदले सोते तथा दूषित कुओं-समान होता है.

27मधु का अत्यधिक सेवन किसी प्रकार लाभकर नहीं होता,

ठीक इसी प्रकार अपने लिए सम्मान से और अधिक सम्मान का यत्न करना लाभकर नहीं होता.

28वह व्यक्ति, जिसका स्वयं पर कोई नियंत्रण नहीं है, वैसा ही है,

जैसा वह नगर, जिसकी सुरक्षा के लिए कोई दीवार नहीं है.