Miyambo 13 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 13:1-25

1Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake,

koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.

2Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake,

koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.

3Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake,

koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.

4Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu,

koma munthu wakhama adzalemera.

5Munthu wolungama amadana ndi zabodza,

koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.

6Chilungamo chimateteza munthu wangwiro,

koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.

7Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse;

munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.

8Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake,

koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.

9Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa,

koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.

10Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano,

koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.

11Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono

koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.

12Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima,

koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.

13Amene amanyoza malangizo adzawonongeka,

koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.

14Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo;

amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.

15Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu,

koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.

16Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru,

koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.

17Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto,

koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.

18Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa,

koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.

19Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima,

koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.

20Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru;

koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.

21Choyipa chitsata mwini,

koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.

22Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa,

koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.

23Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri,

koma anthu opanda chilungamo amachilanda.

24Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda,

koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.

25Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta,

koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.

Asante Twi Contemporary Bible

Mmɛbusɛm 13:1-25

1Ɔba nyansafoɔ tie nʼagya nkyerɛkyerɛ;

na ɔfɛdifoɔ ntie animka.

2Nneɛma pa a ɛfiri onipa anom no ma no anigyeɛ,

na wɔn a wɔnni nokorɛ no kɔn dɔ basabasayɛ.

3Deɛ ɔkora nʼano no kora ne nkwa so,

nanso deɛ ɔkasa a ɔnsusu ho no bɛba ɔsɛeɛ mu.

4Onihafoɔ pere hwehwɛ nanso ɔnnya hwee,

na deɛ ɔyɛ adwuma no nya deɛ ɔpɛ biara.

5Teneneefoɔ kyiri deɛ ɛnyɛ nokorɛ,

nanso amumuyɛfoɔ de aniwuo ne ahohora ba.

6Tenenee bɔ ɔnokwafoɔ ho ban,

na amumuyɛsɛm tu ɔbɔnefoɔ gu.

7Obi yɛ ne ho sɛ ɔdefoɔ, a nso ɔnni hwee,

ɔfoforɔ yɛ ne ho sɛ ohiani, a nso ɔwɔ ahonya bebree.

8Obi ahonya bɛtumi agye no nkwa,

nanso ohiani nte ahunahuna biara.

9Teneneefoɔ kanea hyerɛn pa ara,

nanso wɔdum amumuyɛfoɔ kanea.

10Ahantan de ntɔkwa nko ara na ɛba,

na wɔhunu nyansa wɔ wɔn a wɔtie afutuo mu.

11Ahonya a ɛnam kwammɔne soɔ no hwere ntɛm so,

na deɛ ɔboa sika ano nkakrankakra no ma ɛdɔɔso.

12Anidasoɔ a wɔtu hyɛ da no bɔ akoma yadeɛ,

nanso anigyinadeɛ a nsa aka no yɛ nkwa dua.

13Deɛ ɔtwiri ahyɛdeɛ no bɛtua so ka,

nanso deɛ ɔde obuo ma mmara no, wɔma no akatua.

14Onyansafoɔ nkyerɛkyerɛ te sɛ nkwa asutire,

ɛyi onipa firi owuo afidie mu.

15Nhunumu pa de adom ba,

nanso atorofoɔ ɛkwan so yɛ den.

16Ɔbadwemma biara yɛ nʼadeɛ wɔ nimdeɛ mu,

nanso ɔkwasea da nʼagyimisɛm adi.

17Ɔsomafoɔ mumuyɛfoɔ tɔ amaneɛ mu,

nanso ɔnanmusini nokwafoɔ de abodwoɔ ba.

18Deɛ ɔpo ntenesoɔ no kɔ ohia ne animguaseɛ mu,

na deɛ ɔtie ntenesoɔ no, wɔhyɛ no animuonyam.

19Akɔnnɔdeɛ a nsa aka ma ɔkra ani gye,

nanso nkwaseafoɔ kyiri sɛ wɔtwe wɔn ho firi bɔne ho.

20Deɛ ɔne onyansafoɔ nante no hunu nyansa,

na deɛ ɔne nkwaseafoɔ bɔ no hunu amane.

21Ɔhaw di ɔbɔnefoɔ akyi,

na nkɔsoɔ yɛ teneneeni akatua.

22Onipa pa de agyapadeɛ gya ne nananom,

na wɔkora ɔbɔnefoɔ ahonyadeɛ so ma ɔteneneeni.

23Ohiani afuom nnɔbaeɛ tumi ba pii,

nanso ntɛnkyea pra kɔ.

24Deɛ ɔkyɛe nʼabaa so no tane ne ba,

na deɛ ɔdɔ no no hwɛ sɛ ɔbɛtene no.

25Teneneefoɔ didi ma wɔn akoma mee

nanso, ɛkɔm de amumuyɛfoɔ.