Miyambo 10 – CCL & AKCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 10:1-32

Miyambo ya Solomoni

1Miyambo ya Solomoni:

Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake,

koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.

2Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa,

koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.

3Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala;

koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.

4Wochita zinthu mwaulesi amasauka,

koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.

5Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru,

koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.

6Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama,

koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.

7Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso,

koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.

8Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo,

koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.

9Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka;

koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.

10Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto,

koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.

11Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo,

koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.

12Udani umawutsa mikangano,

koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.

13Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu,

koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.

14Anzeru amasunga chidziwitso

koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.

15Chuma cha munthu wolemera

ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.

16Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama,

koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.

17Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo,

koma wonyoza chidzudzulo amasochera.

18Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama,

ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.

19Mawu akachuluka zolakwa sizisowa,

koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.

20Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri,

koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.

21Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri;

koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.

22Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma,

ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.

23Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa,

koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.

24Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira;

chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.

25Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa,

koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.

26Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso,

ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.

27Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo;

koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.

28Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe,

koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.

29Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino,

koma wochita zoyipa adzawonongeka.

30Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake

koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.

31Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru,

koma lilime lokhota lidzadulidwa.

32Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula,

koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

Akuapem Twi Contemporary Bible

Mmebusɛm 10:1-32

Salomo Mmebusɛm

1Salomo mmebusɛm:

Ɔba nyansafo ma nʼagya ani gye,

na ɔba kwasea brɛ ne na awerɛhow.

2Ɔkwan bɔne so ahonya nni bo,

nanso trenee gye onipa fi owu mu.

3Awurade remma ɔkɔm nne ɔtreneeni

na omumɔyɛfo de, ɔka nʼadepa gu.

4Nsa a ɛnyɛ adwuma ma onipa di hia,

nanso nsiyɛfo nsa de ahonya ba.

5Nea ɔboaboa nnɔbae ano wɔ ahuhurubere no yɛ ɔba nyansafo

na nea ɔda wɔ twabere mu no yɛ ɔba nimguaseni.

6Atreneefo hyɛ nhyira kyɛw

na akakabensɛm ayɛ omumɔyɛfo anom ma.

7Ɔtreneeni nkae yɛ nhyira,

na omumɔyɛfo din bɛporɔw.

8Koma mu nyansafo tie ɔhyɛ nsɛm,

na ɔkwasea kasafo hwe ase.

9Ɔnokwafo nantew dwoodwoo,

na nea ɔfa akwan kɔntɔnkye so no ho bɛda adi.

10Nea ɔde nitan bu nʼani no de ɔhaw ba,

na ɔkwasea kasafo hwe ase.

11Ɔtreneeni anom yɛ nkwa asuti,

na akakabensɛm ayɛ omumɔyɛfo anom ma.

12Ɔtan kanyan mpaapaemu,

nanso ɔdɔ kata mfomso nyinaa so.

13Wohu nyansa wɔ nhumufo anom,

na abaa fata nea onni adwene akyi.

14Anyansafo kora nimdeɛ,

nanso ɔkwasea ano frɛfrɛ ɔsɛe.

15Adefo ahonya yɛ wɔn kuropɔn a wɔabɔ ho ban,

nanso ahiafo hia yɛ wɔn asehwe.

16Atreneefo akatua de nkwa brɛ wɔn,

na nea amumɔyɛfo nya no de asotwe brɛ wɔn.

17Nea otie ntetew pa no kyerɛ nkwa kwan,

na nea ɔpo nteɛso no di afoforo anim yera kwan.

18Nea ɔkata nitan so no yɛ ɔtorofo,

na nea odi nseku no yɛ ɔkwasea.

19Mfomso mpa ɔkasa bebree mu,

na nea ɔkora ne tɛkrɛma no yɛ onyansafo.

20Ɔtreneeni tɛkrɛma yɛ dwetɛ ankasa

nanso omumɔyɛfo koma nni bo.

21Atreneefo ano ma bebree aduan,

na atemmu a nkwaseafo nni nti wowuwu.

22Awurade nhyira de ahonya ba,

na ɔmfa ɔbrɛ mmata ne nya ho.

23Bɔneyɛ yɛ anigyede ma ɔkwasea,

nanso nea ɔwɔ nimdeɛ anigye wɔ nyansa mu.

24Nea amumɔyɛfo suro no bɛba wɔn so;

na nea atreneefo pɛ no, wɔde bɛma wɔn.

25Sɛ ahum no betwa mu a, amumɔyɛfo yera,

nanso atreneefo gyina hɔ pintinn afebɔɔ.

26Sɛnea nsa keka ɛse, na wusiw kɔ aniwa no,

saa ara na ɔkwadwofo yɛ ma wɔn a wɔsoma no.

27Awurade suro ma nkwa tenten,

nanso wotwa amumɔyɛfo nkwa so.

28Atreneefo anidaso de ahotɔ ba,

nanso amumɔyɛfo anidaso nkosi hwee.

29Awurade kwan yɛ guankɔbea ma ɔtreneeni,

nanso ɛyɛ ɔsɛe ma wɔn a wɔyɛ bɔne.

30Wɔrentɔre atreneefo ase da,

nanso amumɔyɛfo renka asase no so.

31Nyansa fi ɔtreneeni anom ba

nanso tɛkrɛma a ɛdaadaa no, wobetwa akyene.

32Ɔtreneeni ano nim ade a ɛfata

na omumɔyɛfo ano nim nea ɛyɛ nnaadaasɛm nko ara.