Mika 3 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 3:1-12

Atsogoleri ndi Aneneri Adzudzulidwa

1Ndipo ine ndinati,

“Tamverani, inu atsogoleri a Yakobo,

inu olamulira nyumba ya Israeli.

Kodi sindinu oyenera kudziwa kuweruza molungama,

2inu amene mumadana ndi zabwino ndi kukonda zoyipa;

inu amene mumasenda khungu la anthu anga,

ndipo mumakungunula mnofu pa mafupa awo;

3inu amene mumadya anthu anga,

mumasenda khungu lawo

ndi kuphwanya mafupa awo;

inu amene mumawadula nthulinthuli

ngati nyama yokaphika?”

4Pamenepo adzalira kwa Yehova,

koma Iye sadzawayankha.

Nthawi imeneyo Iye adzawabisira nkhope yake

chifukwa cha zoyipa zimene anazichita.

5Yehova akuti,

“Aneneri amene

amasocheretsa anthu anga,

ngati munthu wina awapatsa chakudya

amamufunira ‘mtendere;’

ngati munthu wina sawapatsa zakudya

amamulosera zoyipa.

6Nʼchifukwa chake kudzakuderani,

simudzaonanso masomphenya,

mdima udzakugwerani ndipo simudzawombezanso.

Dzuwa lidzawalowera aneneriwo, ndipo mdima udzawagwera.

7Alosi adzachita manyazi

ndipo owombeza mawula adzanyazitsidwa.

Onse adzaphimba nkhope zawo

chifukwa Mulungu sakuwayankha.”

8Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu,

ndi Mzimu wa Yehova,

ndi kulungama, ndi kulimba mtima,

kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo,

kwa Israeli za tchimo lake.

9Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo,

inu olamulira nyumba ya Israeli,

inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama;

ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;

10inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi,

ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.

11Atsogoleri ake amalandira chiphuphu kuti aweruze,

ansembe ake amalandira malipiro kuti alalikire,

ndipo aneneri ake amanenera kuti alandire ndalama.

Komatu amatsamira pa Yehova nʼkumanena kuti,

“Kodi Yehova sali pakati pathu?

Palibe tsoka limene lidzatigwere.”

12Choncho chifukwa cha inu,

Ziyoni adzatipulidwa ngati munda,

Yerusalemu adzasanduka bwinja,

ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.

Luganda Contemporary Bible

Mikka 3:1-12

Ekibi kya Isirayiri

1Ne ndyoka ŋŋamba nti,

“Muwulire mmwe abakulembeze ba Yakobo,

mmwe abafuzi b’ennyumba ya Isirayiri.

Si mmwe mwandisaanidde okumanya obwenkanya,

2mmwe abakyawa ekirungi ne mwagala ekibi;

mmwe ababaagako abantu bange eddiba

ne mubaggyako ennyama ku magumba?

3Mulya ennyama yaabwe,

ne mubabaagako eddiba,

amagumba gaabwe ne mugamenyaamenya,

era ne mubasalaasala ng’ennyama

eneefumbibwa mu nsaka.”

4Balikoowoola Mukama,

naye talibaanukula.

Mu biro ebyo alibakweka amaaso ge

olw’ebibi bye bakoze.

5Bw’atyo bw’ayogera Mukama nti,

“Bannabbi ababuzaabuza abantu

balangirira nti, ‘Mirembe,’ eri oyo abaliisa,

naye oyo atabaliisa bamuggulako olutalo.

6Noolwekyo ekiro kiribajjira, awatali kwolesebwa,

n’enzikiza ebajjire awatali kulagulwa.

Enjuba erigwa nga bannabbi balaba,

n’obudde bubazibirire.

7Abalabi baliswazibwa

n’abalaguzi bakwatibwe ensonyi.

Bonna balibikka amaaso gaabwe

kubanga Katonda tabaanukula.”

8Naye nze, nzijjudde amaanyi

n’Omwoyo wa Mukama,

okwekaliriza ensonga n’obuvumu,

njasanguze eri Yakobo olw’ebikolwa bye ebibi by’akola,

olw’ekibi kya Isirayiri.

9Mumpulirize mmwe abakulembeze b’ennyumba ya Yakobo,

Mmwe abafuzi b’ennyumba ya Isirayiri,

Mmwe abanyooma obwenkanya

Ne mukyusa ekituufu ne mukifuula ekikyamu;

10mmwe abazimbidde Sayuuni ku musaayi,

Ne Yerusaalemi ne mugizimbira ku butali butuukirivu.

11Abakulembeze be, balya enguzi ne basala omusango nga beekubiira,

bakabona be, baggya ensimbi ku bantu balyoke bayigirize,

ne bannabbi be, baagala okuwa obunnabbi nga bamaze kusasulwa.

Kyokka bajuliza Mukama nga boogera nti,

Mukama tali naffe?

Tewali kinaatutuukako.”

12Noolwekyo ku lwammwe,

Sayuuni eririmibwa ng’ennimiro,

ne Yerusaalemi erifuuka ntuumu ya bifunfugu,

n’akasozi okuli yeekaalu kafuuke ng’akabira akakutte.