Mateyu 9 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 9:1-38

Munthu Wakufa Ziwalo wa ku Kaperenawo

1Yesu analowa mʼbwato nawoloka, ndipo anabwera ku mudzi wa kwawo. 2Amuna ena anabwera ndi munthu wakufa ziwalo kwa Iye atamugoneka pa mphasa. Yesu ataona chikhulupiriro chawo anati kwa wakufa ziwaloyo, “Limba mtima mwana wanga, machimo ako akhululukidwa.”

3Pamenepo aphunzitsi ena amalamulo anaganiza mu mtima mwawo kuti, “Munthu uyu akuchitira Mulungu mwano.”

4Ndipo podziwa maganizo awo Yesu anati, “Bwanji mukuganiza zoyipa mʼmitima mwanu? 5Chapafupi ndi chiti kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa’ kapena kunena kuti, ‘Imirira ndipo yenda?’ 6Tsono kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko wokhululuka machimo, pamenepo anati kwa wakufa ziwaloyo, ‘Imirira, tenga mphasa yako kazipita kwanu.’ ” 7Ndipo munthuyo anayimirira napita kwawo. 8Gulu la anthu litaona izi, linadzazidwa ndi mantha ndipo linalemekeza Mulungu amene anapereka ulamuliro kwa anthu.

Kuyitanidwa kwa Mateyu

9Ndipo Yesu atachoka kumeneko, anaona munthu wina dzina lake Mateyu, atakhala mʼnyumba ya msonkho. Anati kwa iye, “Nditsate Ine.” Ndipo iye ananyamuka namutsata.

10Ndipo pamene Iye ankadya mʼnyumba, onani, amisonkho ndi ochimwa ambiri anabwera nakhala pansi pamodzi ndi Yesu ndi ophunzira ake. 11Ndipo Afarisi poona izi, anati kwa ophunzira ake, “Nʼchifukwa chiyani Aphunzitsi anu akudya pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”

12Yesu atamva, anati, “Munthu wamoyo safuna singʼanga ayi, koma wodwala. 13Koma pitani kaphunzireni tanthauzo la mawu awa: ‘Ndimafuna chifundo osati nsembe ayi.’ Pakuti sindinabwere kudzayitana olungama koma ochimwa.”

Za Kusala Kudya

14Ndipo ophunzira a Yohane anabwera namufunsa Iye kuti, “Bwanji ife ndi Afarisi timasala kudya koma ophunzira anu sasala kudya?”

15Yesu anayankha kuti, “Kodi oyitanidwa ku ukwati angamalire bwanji pamene mkwati ali naye pamodzi? Nthawi idzafika pamene mkwatiyo adzachotsedwa ndi pamene adzasala kudya.”

16Ndipo palibe munthu amasokerera chigamba chatsopano pa chovala chakale chifukwa chigambacho chidzachoka ndipo chibowocho chidzakula kuposa kale. 17Kapena sathira vinyo watsopano mʼmatumba akale; akatero, matumba akalewo adzaphulika ndipo vinyoyo adzatayika, matumbawo adzawonongeka; satero ayi. Amathira vinyo watsopano mʼmatumba atsopanonso ndipo zonse zimasungika.

Za Mwana Wamkazi wa Yairo ndi Mayi Wokhudza Chovala cha Yesu

18Pamene ankanena zimenezi, mkulu wa sunagoge anabwera namugwadira Iye nati, “Mwana wanga wamkazi wamwalira posachedwapa koma tiyeni mukasanjike dzanja lanu pa iye ndipo adzakhala ndi moyo.” 19Yesu ndi ophunzira ake ananyamuka napita naye pamodzi.

20Panali mayi wina amene ankadwala nthenda yotaya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri ndipo anadza mʼmbuyo mwake nakhudza mkanjo wake. 21Iyeyo anati mwa iye yekha, “Nditangokhudza kasonga ka mkanjo wake, ine ndidzachiritsidwa.”

22Ndipo Yesu anatembenuka namuona mayiyo nati, “Limbani mtima mayi iwe, chikhulupiriro chako chakuchiritsa.” Nthawi yomweyo mayiyo anachiritsidwa.

23Yesu atalowa mʼnyumba ya mkulu wa sunagoge ndi kuona oyimba zitoliro ndi gulu la anthu ochita phokoso, 24anati, “Tulukani, mtsikanayu sanafe koma ali mtulo.” Koma anamuseka Iye. 25Atangowatulutsa anthuwo, analowa mʼnyumba ndipo anagwira dzanja la mtsikanayo ndipo anauka. 26Mbiriyi inamveka mʼdera lonse.

Yesu Achiritsa Osaona ndi Osayankhula

27Yesu atapitirira ulendo wake, amuna awiri osaona anamutsatira Iye, akufuwula kuti, “Tichitireni chifundo, Mwana wa Davide!”

28Atalowa mʼnyumba, amuna awiri osaonawo anabwera kwa Iye ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukhulupirira kuti ndikhoza kukuchiritsani?”

Iwo anayankha kuti, “Inde Ambuye.”

29Pomwepo anakhudza maso awo nati, “Zichitike kwa inu monga mwachikhulupiriro chanu.” 30Ndipo anayamba kuona. Yesu anawachenjeza kwambiri nati, “Onani, wina aliyense asadziwe za zimenezi.” 31Koma iwo anatuluka mʼnyumbamo nafalitsa za Iye mʼchigawo chonse.

32Pamene iwo ankatuluka kunja, anthu anabwera kwa Iye ndi munthu wogwidwa ndi mzimu wosayankhula. 33Ndipo atatulutsa mzimuwo, munthuyo anayankhula. Gulu la anthuwo linadabwa ndipo linati, “Zinthu zotere sizinaonekepo mu Israeli.”

34Koma Afarisi anati, “Akutulutsa mizimu yoyipa ndi mphamvu ya mkulu wa ziwanda.”

Antchito ndi Ochepa

35Yesu anayendayenda mʼmizinda yonse ndi mʼmidzi, kuphunzitsa mʼmasunagoge awo, nalalikira Uthenga Wabwino wa ufumu ndi kuchiritsa nthenda zawo zonse ndi zofowoka za mʼmatupi mwawo. 36Ataona maguluwo, anagwidwa ndi chisoni chifukwa anali ozunzika ndi osowa chithandizo ngati nkhosa zopanda mʼbusa. 37Pamenepo anati kwa ophunzira ake, “Zokolola ndi zambiri koma antchito ndi ochepa. 38Nʼchifukwa chake, pemphani Ambuye mwini zokolola kuti atumize antchito ku munda wake.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Матай 9:1-38

Исцеление парализованного и прощение его грехов

(Мк. 2:3-12; Лк. 5:18-26)

1Иса вошёл в лодку, переправился на другую сторону озера и вернулся в город, где Он жил. 2Несколько человек принесли к Нему парализованного, лежащего на постели. Когда Иса увидел их веру, Он сказал парализованному:

– Не бойся, сын Мой, прощаются тебе твои грехи!

3Тогда некоторые из учителей Таурата подумали про себя: «Он кощунствует!»

4Зная, о чём они думают, Иса сказал:

– Почему у вас в сердце такие злые мысли? 5Вы, наверное, думаете, что сказать «Прощаются тебе грехи» намного легче, чем сказать «Встань и ходи»? 6Но чтобы вы знали, что Ниспосланный как Человек имеет власть на земле прощать грехи…

И Он обратился к парализованному:

– Вставай, возьми свою постель и иди домой.

7Человек встал и пошёл домой. 8Видевшие это исполнились благоговейного ужаса и стали славить Аллаха, давшего человеку такую власть.

Обед в доме у Матая

(Мк. 2:14-17; Лк. 5:27-32)

9Когда Иса шёл оттуда, Он увидел человека по имени Матай, сидевшего на месте сбора таможенных пошлин.

– Следуй за Мной, – сказал ему Иса.

Тот встал и пошёл за Ним. 10Позже, когда Иса возлежал за столом в доме у Матая, там собралось много сборщиков налогов и прочих грешников. Они возлегли с Исой и Его учениками. 11Когда блюстители Закона увидели это, они спросили учеников Исы:

– Почему ваш Учитель ест со сборщиками налогов и грешниками?

12Когда Иса услышал это, Он сказал:

– Не здоровым нужен врач, а больным. 13Попытайтесь вначале понять, что значат слова: «Милости хочу, а не жертвы»9:13 Ос. 6:6.. Я пришёл призвать не праведников, а грешников.

О посте

(Мк. 2:18-22; Лк. 5:33-39)

14Затем пришли ученики Яхии и спросили:

– Почему мы и блюстители Закона постимся, а Твои ученики – нет?

15Иса ответил им так:

– Разве могут гости на свадьбе печалиться, когда с ними жених? Но наступит время, когда жених будет взят от них, вот тогда они и будут поститься9:15 То есть пока Иса (жених) находился с верующими, им не нужно было печалиться и держать пост.. 16Никто не пришивает к старой одежде заплату из новой ткани: она, когда сядет, разорвёт дыру ещё больше. 17Никто не наливает молодое вино в старые бурдюки, иначе бурдюки прорвутся: и вино вытечет, и бурдюки пропадут. Нет, молодое вино наливают в новые бурдюки, тогда и то и другое будет цело.

Господство Исы аль-Масиха над болезнью и смертью

(Мк. 5:22-43; Лк. 8:41-56)

18Когда Иса ещё говорил, к Нему подошёл один начальник. Он поклонился Исе и сказал:

– Моя дочь только что умерла, но если Ты придёшь и возложишь на неё руку, она оживёт.

19Иса встал и пошёл с ним. Ученики тоже пошли за ними. 20В это время к Исе сзади подошла женщина, двенадцать лет страдавшая кровотечением, и прикоснулась к кисточке на краю Его одежды9:20 К краям верхней мужской одежды иудеи пришивали кисточки, в которые обязательно вплетались голубые нити. Эти кисточки должны были напоминать иудеям о необходимости исполнять повеления Аллаха (см. Чис. 15:38-40; Втор. 22:12).. 21Она думала про себя: «Если я только прикоснусь к Его одежде, то исцелюсь». 22Иса обернулся и увидел её.

– Не бойся, дочь Моя, – сказал Он, – твоя вера исцелила тебя.

И женщина в тот же момент выздоровела.

23Когда Иса вошёл в дом начальника и увидел свирельщиков, приглашённых для похорон, и смятение толпы, 24Он сказал:

– Выйдите, ведь девочка не умерла, а спит.

Но они лишь посмеялись над Ним. 25Когда людей всё-таки удалили, Иса вошёл, взял девочку за руку, и она встала. 26Слух об этом распространился по всей округе.

Исцеление двух слепых и немого

27Когда Иса вышел оттуда, за Ним пошли двое слепых, крича:

– Сжалься над нами, Сын Давуда!9:27 Сын Давуда – один из титулов аль-Масиха. Согласно Книге Пророков ожидаемый Масих (т. е. праведный Царь и Освободитель) должен был быть потомком царя Давуда (см. Ис. 11:1-5; Иер. 23:5-6).

28Когда Он вошёл в дом, слепые подошли к Нему, и Он спросил их:

– Вы верите, что Я могу это сделать?

– Да, Повелитель, – ответили те.

29Тогда Иса прикоснулся к их глазам и сказал:

– Пусть же с вами будет по вашей вере.

30И они тотчас прозрели. Иса же строго наказал им:

– Смотрите, чтобы никто не узнал об этом.

31Но они пошли и рассказали о Нём по всей округе. 32Не успели ещё они выйти, как к Исе привели немого человека, одержимого демоном. 33Когда демон был изгнан, человек, который был нем, заговорил. Люди удивлялись:

– Ничего подобного ещё не бывало в Исраиле.

34Блюстители же Закона говорили:

– Он изгоняет демонов силой повелителя демонов.

Жатвы много, а работников мало

35Иса ходил по всем городам и селениям, учил в молитвенных домах, возвещал Радостную Весть о Царстве и исцелял людей от всех болезней и немощей. 36Увидев толпы народа, Он сжалился над ними, потому что эти люди были измучены и беспомощны, как овцы без пастуха9:36 См. Чис. 27:17; 3 Цар. 22:17; Езек. 34:5.. 37Он говорил Своим ученикам:

– Жатвы много, а работников мало. 38Поэтому просите Хозяина жатвы, чтобы Он выслал работников на Свою жатву.