Mateyu 21 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 21:1-46

Yesu Alowa mu Yerusalemu

1Akuyandikira ku Yerusalemu anafika ku Betifage pa phiri la Olivi, Yesu anatumiza ophunzira awiri, 2nawawuza kuti, “Pitani ku mudzi uli patsogolo panu, ndipo mukakangolowa mʼmenemo mukapeza bulu womangidwa ali ndi mwana pa mbali pake. Mukawamasule ndipo mubwere nawo kwa Ine. 3Wina akakayankhula, mukamuwuze kuti Ambuye akuwafuna, ndipo adzawatumiza nthawi yomweyo.”

4Izi zinachitika kukwaniritsa zimene zinayankhulidwa ndi mneneri:

5“Uza mwana wamkazi wa Ziyoni,

taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe,

yofatsa ndi yokwera pa bulu,

pa kamwana ka bulu, mwana wa nyama yonyamula katundu.”

6Ophunzirawo anapita nachita monga Yesu anawalamulira. 7Anabweretsa bulu ndi mwana wake, nayala zovala zawo pa abuluwo, ndipo Yesu anakwerapo. 8Gulu lalikulu la anthu linayala zovala zawo mu msewu pamene ena anadula nthambi zamitengo ndi kuziyala mu msewumo. 9Magulu amene anali patsogolo pake ndi amene amamutsatira anafuwula kuti,

“Hosana Mwana wa Davide!”

“Wodala Iye amene abwera mʼdzina la Ambuye!”

“Hosana mmwambamwamba!”

10Yesu atalowa mu Yerusalemu, mzinda wonse unatekeseka ndipo anthu anafunsa kuti, “Ndani ameneyu?”

11Magulu a anthu anayankha kuti, “Uyu ndi Yesu, mneneri wochokera ku Nazareti.”

Yesu mʼNyumba ya Mulungu

12Yesu analowa mʼdera lina la Nyumba ya Mulungu ndipo anatulutsa kunja anthu onse amene ankachita malonda. Anagubuduza matebulo a osinthira ndalama ndi mipando ya ogulitsa nkhunda. 13Iye anawawuza kuti, “Zinalembedwa kuti Nyumba yanga idzatchedwa Nyumba ya mapemphero koma inu mwayisandutsa phanga la anthu achifwamba.”

14Anthu osaona ndi olumala anabwera kwa Iye mʼNyumba ya Mulungu ndipo anawachiritsa. 15Koma akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo ataona zodabwitsa zimene anachita, komanso ana akufuwula mʼNyumbayo kuti, “Hosana kwa Mwana wa Davide,” anapsa mtima.

16Anamufunsa kuti, “Kodi mukumva zimene anawa akunena?”

Yesu anayankha nati, “Inde. Kodi simunawerenge kuti,

“Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda

mwatuluka mayamiko?”

17Ndipo anawasiya natuluka mu mzindawo ndi kupita ku Betaniya, kumene anakagona.

Yesu Atemberera Mtengo wa Mkuyu

18Mmamawa, pamene amabwera ku mzinda, anamva njala. 19Ataona mtengo wamkuyu mʼmbali mwa msewu, anapitapo koma sanapeze kanthu koma masamba okhaokha. Pamenepo anati kwa mtengowo, “Usadzabalenso chipatso!” Nthawi yomweyo mtengowo unafota.

20Ophunzira ataona zimenezi, anadabwa nafunsa kuti, “Kodi mtengo wamkuyuwu wauma msanga bwanji?”

21Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti ngati muli ndi chikhulupiriro ndipo simukayika, simudzangochita zokha zachitika kwa mkuyuzi, koma mudzatha kuwuza phiri ili kuti, ‘Pita, kadziponye wekha mʼnyanja,’ ndipo zidzachitikadi. 22Ngati mukhulupirira, mudzalandira chilichonse chimene muchipempha mʼpemphero.”

Amufunsa Yesu za Ulamuliro Wake

23Yesu analowa mʼNyumba ya Mulungu, ndipo pamene ankaphunzitsa, akulu a ansembe ndi akuluakulu anabwera kwa Iye namufunsa kuti, “Muchita izi ndi ulamuliro wanji ndipo anakupatsani ndani ulamuliro umenewu?”

24Yesu anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani funso limodzi, mukandiyankha, Inenso ndikukuwuzani ndi ulamuliro wa yani umene ndikuchitira izi. 25Ubatizo wa Yohane unachokera kuti? Kumwamba kapena kwa anthu?”

Anakambirana pakati pawo ndipo anati, “Tikati, ‘Kuchokera kumwamba,’ Iye adzafunsa kuti, ‘Bwanji simunakhulupirire?’ 26Koma tikati, ‘Kuchokera kwa anthu,’ ife tikuopa anthuwa, pakuti onse amakhulupirira kuti Yohane anali mneneri.”

27Choncho anamuwuza Yesu kuti, “Sitikudziwa.”

Pamenepo Iye anati, “Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wa yani umene ndichitira izi.”

Fanizo la Ana Amuna Awiri

28“Kodi muganiza bwanji? Panali munthu wina anali ndi ana aamuna awiri. Anapita kwa woyamba nati, ‘Mwanawe pita kagwire ntchito lero mʼmunda wamphesa.’

29“Iye anayankha kuti, ‘Sindipita,’ koma pambuyo pake anasintha maganizo napita.

30“Kenaka abambowo anapita kwa mwana winayo nanena chimodzimodzi. Iye anayankha kuti, ‘Ndipita abambo,’ koma sanapite.

31“Ndani wa awiriwa anachita chimene abambo ake amafuna?”

Anamuyankha nati, “Woyambayo.”

Yesu anawawuza kuti, “Ndikuwuzani zoonadi, kuti amisonkho ndi adama akulowa mu ufumu wa Mulungu inu musanalowemo.” 32Pakuti Yohane anabwera kwa inu kuti akuonetseni njira yachilungamo, koma inu simunakhulupirire iye, koma amisonkho ndi adama anamukhulupirira. Koma ngakhale munaona izi, simunatembenuke mtima ndi kumukhulupirira iye.

Fanizo la Alimi

33“Tamverani fanizo lina: Panali mwini munda amene anadzala mphesa. Anamanga mpanda kuzungulira mundawo, nakumba moponderamo mphesa ndipo anamanga nsanja. Kenaka anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi ena napita pa ulendo. 34Pamene nthawi yokolola inakwana, anatumiza antchito ake kwa matenanti aja kuti akatenge zipatso zake.

35“Alimi aja anagwira antchito ake; namenya mmodzi, napha wina, ndi kumuponya miyala wachitatuyo. 36Kenaka anatumiza antchito ena oposa oyambawo ndipo matenantiwo anawachitira chimodzimodzi. 37Pomalizira anatumiza mwana wake. Anati adzamuchitira ulemu mwana wanga.

38“Koma alimiwo ataona mwanayo anati kwa wina ndi mnzake, ‘Uyu ndiye olowa mʼmalo mwa abambo ake. Tiyeni timuphe ndipo titenge cholowa chake.’ 39Pamenepo anamutenga namuponyera kunja kwa munda wamphesa namupha.

40“Tsono akabwera mwini munda wamphesa adzachita nawo chiyani matenantiwo?”

41Iwo anayankha kuti, “Adzawapha moyipa alimi oyipawo ndipo adzabwereketsa mundawo kwa alimi ena amene adzamupatsa gawo lake la mbewu pa nthawi yokolola.”

42Yesu anawawuza kuti, “Kodi simunawerenge mʼmalemba kuti:

“ ‘Mwala umene omanga nyumba anawukana,

womwewo wasanduka mwala wofunika kwambiri wa pa ngodya.

Ambuye wachita izi,

ndipo ndi zodabwitsa mʼmaso mwathu.’

43“Nʼchifukwa chake ndi kukuwuzani kuti ufumu wa Mulungu udzalandidwa kwa inu ndipo udzapatsidwa kwa anthu amene adzabereka chipatso chake. 44Amene agwa pa mwalawu adzadukaduka, ndipo amene udzamugwere udzamuthudzula.”

45Akulu a ansembe ndi Afarisi atamva mafanizo a Yesu, anadziwa kuti ankanena iwo. 46Pamenepo anafuna njira yoti amugwirire, koma anaopa gulu la anthu chifukwa anthu onse ankakhulupirira kuti Iye anali mneneri.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Матто 21:1-46

Торжественный въезд в Иерусалим

(Мк. 11:1-10; Лк. 19:28-38; Ин. 12:12-15)

1Когда они приблизились к Виффагии, что расположена на Оливковой горе неподалёку от Иерусалима, Исо послал вперёд двух учеников, 2сказав им:

– Идите в селение, которое перед вами, там вы сразу же найдёте привязанную ослицу и рядом с ней ослёнка. Отвяжите их и приведите ко Мне. 3Если кто-нибудь вам что-то скажет, то отвечайте, что они нужны Повелителю, и вам тут же дадут их.

4Это произошло для того, чтобы исполнилось сказанное через пророка:

5«Скажите дочери Сиона21:5 То есть жителям Иерусалима.:

вот Царь твой идёт к тебе,

кроткий, верхом на ослице и ослёнке,

сыне вьючного животного»21:5 Зак. 9:9 (см. Ис. 62:11). Исо въехал в Иерусалим на осле, как миролюбивый и смиренный царь, а не на боевом коне с мечом, как это делали цари того времени..

6Ученики пошли и сделали всё так, как велел им Исо. 7Они привели ослицу и ослёнка, положили на них свои плащи, и Исо сел поверх их. 8Большинство собравшихся начало расстилать свои плащи на дороге, другие срезали ветви с деревьев и тоже расстилали их. 9Толпы людей, что шли впереди и позади Него, громко кричали:

– Хвала21:9 Хвала (букв.: «Осанна» («Спаси нас»)) – выражение, ставшее возгласом хвалы; также в ст. 15. Сыну Довуда!

Благословен Тот, Кто приходит во имя Вечного!21:9 Заб. 117:25-26.

Хвала Царю в небесах!

10И когда Исо вошёл в Иерусалим, весь город пришёл в волнение, и все спрашивали:

– Кто это?

11А из толпы отвечали:

– Это пророк Исо из Назарета, что в Галилее!

Изгнание торговцев из храма

(Мк. 11:15-19; Лк. 19:45-47; Ин. 2:13-16)

12Исо вошёл во двор храма и выгнал оттуда всех, кто там продавал и покупал. Он опрокинул столы менял и прилавки торговцев голубями.

13– Написано, – говорил Он, – «Дом Мой будет назван домом молитвы»21:13 Ис. 56:7., а вы превратили его в разбойничье логово21:13 См. Иер. 7:11..

14В храме к Нему подошли слепые и хромые, и Он исцелил их. 15Главные священнослужители и учители Таврота, увидев чудеса, которые совершал Исо, и услышав, как дети кричат в храме: «Хвала Сыну Довуда»21:15 См. Заб. 117:25., сильно рассердились.

16– Ты слышишь, что кричат эти дети? – спросили они Его.

– Да, – ответил Исо, – разве вы не читали, что написано:

«Из уст младенцев и грудных детей

Ты вызовешь Себе хвалу»?21:16 Заб. 8:3.

17Он оставил их и пошёл из города в Вифанию, где и заночевал.

Исо Масех проклинает бесплодный инжир

(Мк. 11:12-14, 20-24)

18Возвращаясь рано утром в город, Исо почувствовал голод. 19Увидев у дороги инжир, Он подошёл к нему, но не нашёл на нём ничего, кроме листьев. Тогда Исо сказал дереву:

– Пусть же от тебя никогда больше не будет плодов!

Инжир сразу же засох21:19 Этим примером Исо хотел показать ученикам, насколько важна вера (см. 21:21-22). Кроме того, это могло быть пророчеством о будущем народа Исроила. Но также это и предостережение всем тем, кто ведёт внешне благопристойную и религиозную жизнь, но по сути не приносит никакого духовного плода.. 20Когда ученики это увидели, то удивились:

– Как это инжир мог так быстро засохнуть?

21Исо ответил им:

– Говорю вам истину: если вы будете верить, не сомневаясь, то сможете сделать не только то, что было сделано с инжиром, но даже если вы скажете этой горе: «Поднимись и бросься в море!» – то так и будет. 22Если вы верите, то получите всё, о чём бы вы ни попросили в молитве.

Вопрос о власти Исо Масеха

(Мк. 11:27-33; Лк. 20:1-8)

23Когда Исо вошёл в храм и стал учить народ, к Нему подошли главные священнослужители и старейшины народа с вопросом:

– По какому праву Ты всё это делаешь, и кто дал Тебе такое право?

24Исо ответил им:

– Я тоже задам вам вопрос, и если вы Мне ответите, то и Я скажу вам, по какому праву Я это делаю. 25Обряд погружения в воду21:25 Или: «обряд омовения»., который совершал Яхьё, был от Всевышнего или от людей?

Они стали рассуждать между собой:

– Если мы скажем: «От Всевышнего», то Он спросит: «Так почему же вы ему не поверили?» 26Сказать «От людей» нельзя – боимся народа, ведь все считают, что Яхьё был пророком.

27И они ответили:

– Мы не знаем.

– Тогда и Я вам не скажу, по какому праву Я всё это делаю, – сказал им Исо.

Притча о двух сыновьях

28– Что вы скажете на такое: у одного человека было два сына. Как-то он подошёл к одному из них и говорит: «Сын, пойди поработай сегодня в винограднике». 29«Не хочу», – ответил сын, но потом передумал и всё же пошёл. 30Подойдя и к другому сыну, отец попросил его о том же. Сын ответил: «Иду, господин», а сам не пошёл. 31Кто из них исполнил волю отца?

– Первый, – ответили они.

Тогда Исо сказал им:

– Говорю вам истину: сборщики налогов и блудницы впереди вас идут в Царство Всевышнего. 32Ведь Яхьё пришёл к вам показать путь праведности, и вы не поверили ему, а они поверили. Вы же, даже после того, как это увидели, не раскаялись и не поверили.

Притча о злых виноградарях

(Мк. 12:1-12; Лк. 20:9-19)

33– Послушайте ещё одну притчу: один землевладелец посадил виноградник, обнёс его забором, выкопал яму для давильни21:33 Давильня – в те времена виноград давили в особых углублениях, высеченных в скале, откуда сок вытекал через специальное отверстие. и построил сторожевую башню21:33 Ср. Ис. 5:1-7.. Он отдал виноградник внаём виноградарям, а сам уехал в далёкую страну. 34Когда пришло время сбора винограда, он послал своих рабов к виноградарям, чтобы забрать свою часть урожая. 35Те же схватили рабов и кого избили, кого убили, а кого закидали камнями. 36Тогда хозяин послал других рабов, их было больше, чем в первый раз, но виноградари и с теми поступили так же. 37В конце концов он послал своего сына. «Сына-то моего они устыдятся», – думал он. 38Но когда виноградари увидели сына, они решили: «Это наследник. Давайте убьём его и завладеем его наследством». 39Они схватили его, выбросили из виноградника и убили. 40Итак, когда придёт хозяин виноградника, что он сделает с этими виноградарями?

41– Он жестоко казнит злодеев, – ответили они, – и сдаст виноградник другим виноградарям, которые отдадут ему его долю урожая в условленный срок.

42Исо сказал им:

– Разве вы никогда не читали в Писании:

«Камень, Который отвергли строители,

стал краеугольным.

Это совершил Вечный,

и как это удивительно для нас!»?21:42 Заб. 117:22-23.

43Поэтому Я и говорю вам, что Царство Всевышнего будет отнято у вас и отдано народу, который приносит плод. 44Кто упадёт на Этот Камень, разобьётся вдребезги, а на кого Он упадёт, того раздавит.

45Выслушав притчи Исо, главные священнослужители и блюстители Закона поняли, что Он говорит о них. 46Они хотели арестовать Исо, но боялись народа, потому что люди считали Исо пророком.