Mateyu 15 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 15:1-39

Miyambo ya Makolo

1Pamenepo Afarisi ena ndi aphunzitsi amalamulo anabwera kwa Yesu kuchokera ku Yerusalemu ndipo anamufunsa kuti, 2“Chifukwa chiyani ophunzira anu amaphwanya mwambo wa akuluakulu? Iwo sasamba mʼmanja pakudya!”

3Yesu anayankha kuti, “Nanga chifukwa chiyani inu mumaphwanya lamulo la Mulungu chifukwa cha mwambo wa makolo anu? 4Pakuti Mulungu anati, ‘Lemekeza abambo ako ndi amayi ako’ ndipo ‘aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.’ 5Koma inu mumati, ngati munthu anena kwa abambo ake kapena amayi ake kuti, ‘Thandizo lililonse mukalirandira kuchokera kwa ine ndi mphatso yoperekedwa kwa Mulungu,’ 6iye sakulemekeza nayo abambo ake ndipo ndi khalidwe lotere inu mumapeputsa nalo Mawu a Mulungu chifukwa cha mwambo wanu. 7Inu anthu achiphamaso, Yesaya ananenera za inu kuti,

8“ ‘Anthu awa amandilemekeza Ine ndi milomo yawo,

koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.

9Amandilambira Ine kwachabe

ndi kuphunzitsa malamulo ndi malangizo a anthu.’ ”

10Yesu anayitana gulu la anthu nati, “Mverani ndipo zindikirani. 11Chimene chimalowa mʼkamwa mwa munthu sichimuchititsa kukhala woyipa, koma chimene chimatuluka mʼkamwa mwake, icho ndi chimene chimamuchititsa kukhala woyipa.”

12Pamenepo ophunzira anabwera kwa Iye ndipo anamufunsa kuti, “Kodi mukudziwa kuti Afarisi anakhumudwa pamene anamva mawu aja?”

13Iye anayankha kuti, “Mbewu iliyonse imene Atate anga akumwamba sanadzale idzazulidwa ndi mizu yomwe. 14Alekeni, ndi atsogoleri osaona. Ngati munthu wosaona atsogolera wosaona mnzake, onse awiri adzagwera mʼdzenje.”

15Petro anati, “Timasulireni fanizoli.”

16Yesu anawafunsa kuti, “Kani ngakhale inunso simumvetsa? 17Kodi inu simudziwa kuti chilichonse cholowa mʼkamwa chimapita mʼmimba ndipo kenaka chimatuluka kunja kwa thupi? 18Koma zinthu zimene zituluka mʼkamwa zimachokera mu mtima ndipo zimenezi zimamuchititsa munthu kukhala woyipa. 19Pakuti mu mtima mumatuluka maganizo oyipa, zakupha, zachigololo, zadama, zakuba, zaumboni wonama ndi zachipongwe. 20Izi ndi zimene zimachititsa munthu kukhala woyipa; koma kudya ndi mʼmanja mosasamba sikumuchititsa munthu kukhala woyipa.”

Mayi wa ku Kanaani

21Yesu atachoka kumalo amenewo anapita kudera la ku Turo ndi ku Sidoni. 22Mayi wa Chikanaani wochokera dera la komweko anabwera kwa Iye akulira, nati, “Ambuye, Mwana wa Davide, ndichitireni chifundo! Mwana wanga wamkazi akuzunzika kwambiri ndi chiwanda.”

23Yesu sanayankhe kanthu. Ndipo ophunzira ake anabwera namupempha Iye kuti, “Muwuzeni achoke chifukwa akulira mofuwula pambuyo pathu.”

24Iye anayankha kuti, “Ine ndinatumidwa kwa nkhosa zotayika za Israeli zokha.”

25Mayiyo anabwera ndi kugwada pamaso pake, nati, “Ambuye ndithandizeni!”

26Iye anayankha kuti, “Sibwino kutenga chakudya cha ana ndi kuponyera agalu.”

27Mayiyo anati, “Inde Ambuye. Komatu ngakhale agalu amadya nyenyeswa zimene zimagwa kuchokera pa tebulo la mbuye wawo.”

28Pomwepo Yesu anayankha kuti, “Mayi iwe uli ndi chikhulupiriro chachikulu! Pempho lako lamveka.” Ndipo mwana wake wamkazi anachira nthawi yomweyo.

Yesu Adyetsa Anthu 4,000

29Yesu anachoka kumeneko napita mʼmbali mwa nyanja ya Galileya. Ndipo anakwera ku phiri nakhala pansi. 30Gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Iye ndi anthu olumala, osaona, ofa ziwalo, osayankhula ndi ena ambiri nawagoneka pa mapazi ake ndipo Iye anawachiritsa. 31Anthu ataona osayankhula akuyankhula, ofa ziwalo akuchira, olumala miyendo akuyenda ndi osaona akuona anadabwa kwambiri. Ndipo analemekeza Mulungu wa Israeli.

32Yesu anayitana ophunzira ake nati, “Ndili ndi chifundo ndi anthu awa; akhala kale ndi Ine masiku atatu ndipo alibe chakudya. Ine sindifuna kuti apite kwawo ndi njala chifukwa angakomoke pa njira.”

33Ophunzira anayankha kuti, “Ndikuti kumene tingakapeze buledi mʼtchire muno okwanira kudyetsa gulu lotere?”

34Yesu anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati?”

Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri ndi tinsomba pangʼono.”

35Iye anawuza gululo kuti likhale pansi. 36Kenaka anatenga malofu asanu ndi awiri aja ndi tinsombato ndipo atayamika anagawa napatsa ophunzira ake ndipo iwo anagawira anthuwo. 37Onse anadya ndipo anakhuta. Pomaliza ophunzira anatolera zotsalira nadzaza madengu asanu ndi awiri. 38Chiwerengero cha anthu amene anadya chinali 4,000 kupatula amayi ndi ana. 39Yesu atatha kuwuza gululo kuti lipite kwawo, analowa mʼbwato ndipo anapita kudera la Magadala.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Матай 15:1-39

О внутренней чистоте

(Мк. 7:1-23)

1Затем пришли к Исе из Иерусалима блюстители Закона и учители Таурата и сказали:

2– Почему Твои ученики нарушают обычаи наших предков? Они не омывают рук перед едой!15:2 У древних иудеев существовал особый ритуал омовения рук перед приёмом пищи, подобный тому, что можно наблюдать среди народов Востока.

3Иса ответил:

– А почему вы ради соблюдения своего обычая нарушаете повеление Аллаха?15:3 Духовные учители иудеев разработали целую систему обрядового очищения, намного превосходящую по своим требованиям то, что Аллах предписал в Таурате. Эти установления передавались из поколения в поколение в устной форме. 4Ведь Аллах сказал: «Почитай отца и мать»15:4 Исх. 20:12; Втор. 5:16. и «Кто злословит отца или мать, тот должен быть предан смерти»15:4 Исх. 21:17; Лев. 20:9.. 5Вы же говорите, что если человек скажет отцу или матери: «Отдаю Аллаху то, чем я мог бы тебе помочь», 6то ему уже не обязательно помогать отцу15:5-6 Произнеся эти слова, человек, по мнению духовных учителей, освобождался от обязанности помогать своим нуждающимся родителям. И в данном случае никого не интересовало, будут ли эти средства потрачены на нужды храма или нет.. Тем самым вы ради своего обычая отменяете слово Аллаха. 7Лицемеры! Прав был Исаия, когда пророчествовал о вас:

8«Этот народ чтит Меня на словах,

но сердца их далеки от Меня.

9Они поклоняются Мне впустую,

потому что их учение состоит из человеческих предписаний»15:8-9 Ис. 29:13..

10Иса подозвал к Себе народ и сказал:

– Выслушайте и постарайтесь понять. 11Не то, что входит в человека через рот, оскверняет его; оскверняет человека то, что исходит из его уст.

12Позже ученики сказали Исе:

– Ты знаешь, что Твои слова обидели блюстителей Закона?

13Иса ответил:

– Каждое растение, посаженное не Моим Небесным Отцом, будет вырвано с корнем. 14Оставьте их, они слепые поводыри слепых. А если слепой поведёт слепого, то оба упадут в яму.

15Петир же попросил:

– Объясни нам эту притчу.

16– Так и вы тоже до сих пор не понимаете? – сказал Иса. – 17Неужели вы не понимаете, что всё, что входит в человека через рот, проходит через желудок, а потом выходит вон? 18Но то, что исходит из уст, исходит из сердца, это и оскверняет человека. 19Потому что из сердца исходят злые мысли, убийства, супружеская неверность, разврат, воровство, лжесвидетельство, клевета. 20Именно это оскверняет человека, а не то, что он не омывает рук перед едой.

Вера язычницы

(Мк. 7:24-30)

21Покинув это место, Иса отправился в окрестности Тира и Сидона. 22Там к Нему с плачем подошла местная женщина-хананеянка и стала кричать:

– Повелитель, Сын Давуда, сжалься надо мной! Моя дочь одержима демоном и ужасно мучается!

23Иса не отвечал ей ни слова. Тогда Его ученики стали просить:

– Отошли её, а то она идёт за нами и кричит.

24Иса сказал женщине:

– Я послан только к народу Исраила, к заблудшим овцам.

25Женщина подошла и поклонилась Ему:

– Повелитель, помоги мне!

26Иса ответил:

– Нехорошо будет забрать хлеб у детей и бросить собакам15:26 Букв.: «собачкам». Для иудеев собака считалась нечистым животным. Исраильтяне часто называли язычников собаками, но в данном случае Иса не желал кого-либо обидеть, Он просто привёл иллюстрацию из жизни..

27– Да, Повелитель, – ответила женщина, – но ведь и собаки едят крошки, которые падают со стола хозяев.

28Тогда Иса сказал ей:

– Женщина, у тебя великая вера! Пусть будет так, как ты хочешь.

И в тот же час её дочь исцелилась.

Народ восхваляет Аллаха за исцеления

(Мк. 7:31-37)

29Иса ушёл оттуда и пошёл вдоль Галилейского озера. В одном месте Он поднялся на склон горы и сел там. 30К Нему пришло множество людей, среди которых были хромые, слепые, калеки, немые и многие другие больные. Этих несчастных клали к ногам Исы, и Он исцелял их. 31Люди удивлялись, когда видели немых говорящими, калек здоровыми, хромых ходящими и слепых зрячими, и славили Бога Исраила.

Насыщение более четырёх тысяч человек

(Мк. 8:1-10)

32Иса подозвал Своих учеников и сказал:

– Мне жаль этих людей, они со Мной вот уже три дня, и у них не осталось еды. Я не хочу отпускать их голодными, ведь они могут ослабеть в дороге.

33Ученики ответили:

– Где же мы возьмём здесь, в этой пустыне, столько хлеба, чтобы накормить всё это множество людей?

34– Сколько у вас лепёшек? – спросил Иса.

– Семь лепёшек и несколько рыбок, – ответили они.

35Иса велел людям возлечь на землю. 36Затем Он взял семь лепёшек и рыбу и, поблагодарив за них Аллаха, стал разламывать на куски, передавая ученикам, а те, в свою очередь, – народу. 37Все ели и насытились, а когда собрали оставшиеся куски, то их набралось семь полных корзин. 38Всего ело четыре тысячи одних только мужчин, не считая женщин и детей.

39Отпустив народ, Иса сел в лодку и отправился в окрестности Магадана15:39 Точное местоположение этого города в Палестине не известно. Многие толкователи считают, что это другое название города Магдалы, откуда была родом Марьям, одна из последовательниц Исы (см. 27:56)..