Masalimo 99 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 99:1-9

Salimo 99

1Yehova akulamulira,

mitundu ya anthu injenjemere;

Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi,

dziko lapansi ligwedezeke.

2Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova;

Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.

3Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri,

Iye ndi woyera.

4Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo

Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera;

mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.

5Kwezani Yehova Mulungu wathu

ndipo mulambireni pa mapazi ake;

Iye ndi woyera.

6Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake,

Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake;

iwo anayitana Yehova

ndipo Iyeyo anawayankha.

7Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo;

iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.

8Inu Yehova Mulungu wathu,

munawayankha iwo;

Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka,

ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.

9Kwezani Yehova Mulungu wathu

ndipo mumulambire pa phiri lake loyera,

pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.

Persian Contemporary Bible

مزامير 99:1-9

خدای مقدس

1ای قومها بترسيد، زيرا خداوند سلطنت می‌كند! ای تمام زمين بلرزيد، زيرا خداوند بر تخت خود كه بر بالای سر فرشتگان قرار دارد نشسته است!

2خداوند در اورشليم جلوس فرموده و بر تمام قومها مسلط است. 3همهٔ مردم نام بزرگ او را گرامی بدارند، زيرا او مقدس است.

4ای خدا، ای «پادشاه» مقدر (توانا)، تو انصاف را دوست داری. تو در اسرائيل عدالت و برابری را بنياد نهاده‌ای.

5خداوند، خدای ما را ستايش كنيد و در پيشگاه او به خاک بيفتيد زيرا او مقدس است.

6وقتی موسی و هارون و سموئيل، مردان خدا، از خداوند كمک خواستند، او درخواست ايشان را مستجاب فرمود. 7او از ميان ستون ابر با آنان سخن گفت و آنان احكام و دستورات او را اطاعت كردند.

8ای خداوند، خدای ما، تو دعای قوم خود را مستجاب نمودی و به آنها نشان دادی كه خدايی بخشنده هستی؛ اما در عين حال آنها را به خاطر گناهانشان تنبيه نمودی.

9خداوند، خدای ما را حمد گوييد و او را نزد كوه مقدسش در اورشليم عبادت كنيد، زيرا او مقدس است.