Masalimo 98 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 98:1-9

Salimo 98

Salimo.

1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,

pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa;

dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera

zamuchitira chipulumutso.

2Yehova waonetsa chipulumutso chake

ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.

3Iye wakumbukira chikondi chake

ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli;

malekezero onse a dziko lapansi aona

chipulumutso cha Mulungu wathu.

4Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi,

muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.

5Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze,

ndi zeze ndi mawu a kuyimba,

6ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna

fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.

7Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo,

dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.

8Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo,

mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;

9izo ziyimbe pamaso pa Yehova,

pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi.

Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo,

ndi mitundu ya anthu mosakondera.

New International Version

Psalms 98:1-9

Psalm 98

A psalm.

1Sing to the Lord a new song,

for he has done marvelous things;

his right hand and his holy arm

have worked salvation for him.

2The Lord has made his salvation known

and revealed his righteousness to the nations.

3He has remembered his love

and his faithfulness to Israel;

all the ends of the earth have seen

the salvation of our God.

4Shout for joy to the Lord, all the earth,

burst into jubilant song with music;

5make music to the Lord with the harp,

with the harp and the sound of singing,

6with trumpets and the blast of the ram’s horn—

shout for joy before the Lord, the King.

7Let the sea resound, and everything in it,

the world, and all who live in it.

8Let the rivers clap their hands,

let the mountains sing together for joy;

9let them sing before the Lord,

for he comes to judge the earth.

He will judge the world in righteousness

and the peoples with equity.