Masalimo 96 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 96:1-13

Salimo 96

1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano;

Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.

2Imbirani Yehova, tamandani dzina lake;

lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

3Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko,

ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.

4Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda;

ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.

5Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano,

koma Yehova analenga mayiko akumwamba.

6Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake,

mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.

7Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

8Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake;

bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.

9Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake;

njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.

10Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.”

Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe;

Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.

11Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere;

nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;

12minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo.

Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;

13idzayimba pamaso pa Yehova,

pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi;

adzaweruza dziko lonse mwachilungamo

ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.

Het Boek

Psalmen 96:1-13

1Zingt een nieuw lied ter ere van Jahweh, Heel de aarde, zingt Jahweh ter eer! 2Zingt voor Jahweh, en zegent zijn Naam, Verkondigt zijn heil iedere dag; 3Meldt aan de naties zijn glorie, Aan alle volkeren zijn wonderen! 4Want groot is Jahweh, hoog te prijzen, En boven alle goden te vrezen! 5Ja, alle goden der volkeren zijn niets, Maar Jahweh heeft de hemel gemaakt; 6Glans en glorie zijn voor zijn aanschijn, Kracht en luister in zijn heilige woning. 7Brengt Jahweh, geslachten der volken, Brengt Jahweh glorie en lof. 8Brengt Jahweh de eer van zijn Naam, En treedt met offers zijn voorhoven binnen; 9Werpt u neder voor Jahweh in zijn heilige woning, Heel de aarde, beef voor zijn aanschijn! 10Roept het onder de volkeren uit, “Jahweh is Koning! Hij houdt de weegschaal der wereld, zodat ze niet schommelt, En de volkeren richt Hij naar recht!” 11Laat de hemelen juichen, de aarde jubelen, Laat bulderen de zee met wat ze bevat. 12Laat jubelen het veld, met wat er op groeit, In het woud alle bomen juichen 13Voor het aanschijn van Jahweh, want Hij komt, Hij komt, om de aarde te richten! Met rechtvaardigheid richt Hij de wereld, En de volkeren naar zijn trouw.