Masalimo 96 – CCL & AKCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 96:1-13

Salimo 96

1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano;

Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.

2Imbirani Yehova, tamandani dzina lake;

lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

3Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko,

ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.

4Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda;

ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.

5Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano,

koma Yehova analenga mayiko akumwamba.

6Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake,

mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.

7Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

8Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake;

bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.

9Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake;

njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.

10Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.”

Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe;

Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.

11Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere;

nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;

12minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo.

Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;

13idzayimba pamaso pa Yehova,

pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi;

adzaweruza dziko lonse mwachilungamo

ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 96:1-13

Dwom 96

1Monto dwom foforo mma Awurade;

asase nyinaa monto dwom mma Awurade.

2Monto dwom mma Awurade, monkamfo ne din;

mompae mu nka ne nkwagye no daa daa.

3Monka nʼanuonyam wɔ amanaman mu,

monka nʼanwonwade a wayɛ wɔ nnipa mu.

4Awurade yɛ ɔkɛse na nkamfo fata no;

ɛsɛ sɛ wosuro no sen anyame nyinaa.

5Aman so anyame nyinaa yɛ ahoni bi kwa,

nanso Awurade na ɔbɔɔ ɔsoro.

6Anuonyam ne kɛseyɛ wɔ nʼanim;

ahoɔden ne anuonyam wɔ ne kronkronbea hɔ.

7Momfa mma Awurade, amanaman mmusuakuw,

momfa anuonyam ne tumi mma Awurade.

8Momfa anuonyam ne din a ɛfata mma Awurade;

momfa afɔrebɔde nhyɛn nʼadiwo hɔ.

9Monsɔre Awurade wɔ ne kronkronyɛ fɛfɛ mu;

asase nyinaa momma mo ho mpopo wɔ nʼanim.

10Monka nkyerɛ aman nyinaa se, “Awurade di hene.”

Wɔabɔ asase atim hɔ pintinn, wɔrentumi ntutu;

ɔde pɛpɛyɛ bebu nnipa atɛn.

11Momma ɔsorosoro ani nnye, na asase nni ahurusi;

momma po ne mu nneɛma nyinaa nworo;

12Momma mfuw ne so nneɛma nyinaa mmɔ ose;

momma kwae mu nnua nyinaa mfa ahosɛpɛw nto nnwom.

13Momma abɔde nyinaa nni ahurusi wɔ Awurade anim, efisɛ ɔreba,

ɔreba abebu asase no atɛn.

Ɔde trenee bebu wiase atɛn

na woabu nnipa nso atɛn wɔ ne nokware mu.