Masalimo 90 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 90:1-17

BUKU LACHINAYI

Masalimo 90–106

Salimo 90

Pemphero la Mose munthu wa Mulungu.

1Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo

pa mibado yonse.

2Mapiri asanabadwe,

musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse,

kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.

3Inu mumabwezera anthu ku fumbi,

mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”

4Pakuti zaka 1,000 pamaso panu

zili ngati tsiku limene lapita

kapena ngati kamphindi ka usiku.

5Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa,

iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,

6ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano,

pofika madzulo wauma ndi kufota.

7Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu;

ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.

8Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu,

machimo athu obisika poonekera pamaso panu.

9Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu;

timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.

10Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70,

kapena 80 ngati tili ndi mphamvu;

komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa,

zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.

11Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu?

Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.

12Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola,

kuti tikhale ndi mtima wanzeru.

13Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?

Achitireni chifundo atumiki anu.

14Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha,

kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.

15Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa,

kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.

16Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu,

kukongola kwanu kwa ana awo.

17Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife;

tikhazikitsireni ntchito ya manja athu;

inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.