Masalimo 87 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 87:1-7

Salimo 87

Salimo la Ana a Kora.

1Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;

2Yehova amakonda zipata za Ziyoni

kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.

3Za ulemerero wako zimakambidwa,

Iwe mzinda wa Mulungu:

Sela

4“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni

pakati pa iwo amene amandidziwa.

Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi,

ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’ ”

5Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti,

“Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye,

ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”

6Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina:

“Uyu anabadwira mʼZiyoni.”

Sela

7Oyimba ndi ovina omwe adzati,

“Akasupe anga onse ali mwa iwe.”