Masalimo 86 – CCL & HCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 86:1-17

Salimo 86

Pemphero la Davide.

1Ndimvereni Yehova ndipo mundiyankhe,

pakuti ndine wosauka ndi wosowa.

2Yangʼanirani moyo wanga, pakuti ndine wodzipereka kwa Inu.

Inu ndinu Mulungu wanga;

pulumutsani mtumiki wanu amene amadalira Inu.

Inu ndinu Mulungu wanga.

3Mundichitire chifundo, Inu Ambuye,

pakuti ndikuyitana Inu tsiku lonse.

4Bweretsani chimwemwe kwa mtumiki wanu, Ambuye,

pakuti ndimadalira Inu.

5Inu Ambuye, ndinu wokhululuka ndi wabwino,

wodzaza ndi chikondi kwa onse amene amayitana Inu.

6Yehova imvani pemphero langa;

mvetserani kulira kwanga kofuna chifundo.

7Pa tsiku la mavuto anga ndidzayitana Inu,

pakuti Inu mudzandiyankha.

8Pakati pa milungu palibe wina wofanana nanu Ambuye;

palibe ntchito zolingana ndi ntchito zanu.

9Mitundu yonse ya anthu imene munayipanga

idzabwera ndi kudzalambira pamaso panu Ambuye;

iwo adzabweretsa ulemerero pa dzina lanu.

10Pakuti ndinu wamkulu ndipo mumachita zodabwitsa;

Inu nokha ndiye Mulungu.

11Ndiphunzitseni njira yanu Yehova,

ndipo ndidzayenda mʼchoonadi chanu;

patseni mtima wosagawikana

kuti ndilemekeze dzina lanu.

12Ndidzakutamandani Ambuye Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse;

ndidzalemekeza dzina lanu kwamuyaya.

13Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu kwa ine;

mwandipulumutsa ku malo ozama a manda.

14Inu Mulungu wanga, anthu odzikuza akundithira nkhondo;

anthu ankhanza akufuna kundipha,

amene salabadira za Inu.

15Koma Ambuye ndinu Mulungu wachifundo ndi wokoma mtima,

wosakwiya msanga, wodzaza ndi chikondi ndi wokhulupirika.

16Tembenukirani kwa ine ndipo ndichitireni chifundo;

perekani mphamvu zanu kwa mtumiki wanu

ndipo pulumutsani mwana wa mdzakazi wanu.

17Mundionetse chizindikiro cha ubwino wanu

kuti adani achione ndi kuchititsidwa manyazi,

pakuti Yehova mwandithandiza ndi kunditonthoza.

Hindi Contemporary Version

स्तोत्र 86:1-17

स्तोत्र 86

दावीद की एक प्रार्थना

1याहवेह, मेरी बिनती सुनकर मुझे उत्तर दीजिए,

क्योंकि मैं दरिद्र तथा दीन हूं.

2मेरे प्राणों की रक्षा कीजिए, क्योंकि मैं आपके प्रति समर्पित हूं;

अपने इस सेवक को बचा लीजिए, जिसने आप पर भरोसा रखा है.

आप मेरे परमेश्वर हैं; 3प्रभु, मुझ पर कृपा कीजिए,

क्योंकि मैं सारा दिन आपको पुकारता रहता हूं.

4अपने सेवक के प्राणों में आनंद का संचार कीजिए,

क्योंकि, प्रभु, मैं अपना प्राण आपकी ओर उठाता हूं.

5प्रभु, आप कृपानिधान एवं क्षमा शील हैं, उन सभी के प्रति,

जो आपको पुकारते हैं, आपका करुणा-प्रेम महान है.

6याहवेह, मेरी प्रार्थना सुनिए;

कृपा कर मेरी पुकार पर ध्यान दीजिए.

7संकट के अवसर पर मैं आपको पुकारूंगा,

क्योंकि आप मुझे उत्तर देंगे.

8प्रभु, देवताओं में कोई भी आपके तुल्य नहीं है;

आपके कृत्यों की तुलना किसी अन्य से नहीं की जा सकती.

9आपके द्वारा बनाए गए समस्त राष्ट्रों के लोग,

हे प्रभु, आपके सामने आकर आपकी वंदना करेंगे;

वे आपकी महिमा का आदर करेंगे.

10क्योंकि आप महान हैं और अद्भुत हैं आपके कृत्य;

मात्र आप ही परमेश्वर हैं.

11हे याहवेह, मुझे अपनी राह की शिक्षा दीजिए,

कि मैं आपके सत्य का आचरण करूं;

मुझे एकचित्त हृदय प्रदान कीजिए,

कि मैं आपकी महिमा के प्रति श्रद्धा बनाए रखूं.

12मेरे प्रभु परमेश्वर, मैं संपूर्ण हृदय से आपका स्तवन करूंगा;

मैं आपकी महिमा का आदर सदैव करता रहूंगा.

13क्योंकि मेरे प्रति आपका करुणा-प्रेम अधिक है;

अधोलोक के गहरे गड्ढे से,

आपने मेरे प्राण छुड़ा लिए हैं.

14परमेश्वर, अहंकारी मुझ पर आक्रमण कर रहे हैं;

क्रूर पुरुषों का समूह मेरे प्राणों का प्यासा है,

ये वे हैं, जिनके हृदय में आपके लिए कोई सम्मान नहीं है.

15किंतु प्रभु, आप कृपालु और दयालु परमेश्वर हैं,

आप विलंब से क्रोध करनेवाले तथा अति करुणामय एवं सत्य से परिपूर्ण हैं.

16मेरी ओर फिरकर मुझ पर कृपा कीजिए;

अपने सेवक को अपनी ओर से शक्ति प्रदान कीजिए;

अपनी दासी के पुत्र को बचा लीजिए.

17मुझे अपनी खराई का चिन्ह दिखाइए, कि इसे देख मेरे शत्रु लज्जित हो सकें,

क्योंकि वे देखेंगे, कि याहवेह, आपने मेरी सहायता की है,

तथा आपने ही मुझे सहारा भी दिया है.