Masalimo 83 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 83:1-18

Salimo 83

Nyimbo. Salimo la Asafu.

1Inu Mulungu musakhale chete;

musangoti phee, Mulungu musangoti duu.

2Onani adani anu akuchita chiwawa,

amene amadana nanu autsa mitu yawo.

3Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu;

Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.

4Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu

kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”

5Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu;

Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:

6Matenti a Edomu ndi Aismaeli,

Mowabu ndi Ahagiri,

7Agebala, Aamoni ndi Aamaleki,

Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.

8Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo

kupereka mphamvu kwa ana a Loti.

Sela

9Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani,

monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.

10Amene anawonongedwa ku Endori

ndi kukhala ngati zinyalala.

11Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu

ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,

12amene anati, “Tiyeni tilande dziko

la msipu la Mulungu.”

13Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga,

ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.

14Monga moto umatentha nkhalango,

kapena malawi a moto kuyatsa phiri,

15kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho,

ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.

16Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi

kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.

17Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse;

awonongeke mwa manyazi.

18Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova,

ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Забур 83:1-13

Песнь 83

1Дирижёру хора. Под гиттит83:1 Гиттит – см. сноску на 80:1.. Песнь потомков Кораха.

2Как прекрасно Твоё жилище,

Вечный, Повелитель Сил!

3Истомилась моя душа,

стремясь во дворы храма Вечного;

сердце моё и плоть

поют Богу живому.

4Даже воробей находит себе дом,

и ласточка – гнездо,

чтобы вывести своих птенцов,

у Твоего жертвенника,

о Вечный, Повелитель Сил,

Царь мой и Бог мой.

5Благословенны живущие в доме Твоём;

они непрестанно будут восхвалять Тебя. Пауза

6Благословен человек, сила которого в Тебе,

в чьём сердце есть желание отправиться в Иерусалим.

7Проходя долиною Плача83:7 Или: «долиною Баха».,

они открывают в ней источники,

и дождь покрывает её водоёмами83:7 Или: «благословением»..

8Они крепнут всё больше и больше,

и каждый предстаёт перед Аллахом на Сионе.

9Вечный, Бог Сил, услышь мою молитву;

внемли мне, Бог Якуба. Пауза

10Взгляни, Аллах, на царя, на щит наш83:10 Или: «Взгляни, Аллах, Щит наш».;

посмотри с благоволением на помазанника Своего.

11Один день во дворах Твоего храма

лучше тысячи вне его стен.

Лучше быть у порога дома Аллаха,

чем жить в шатрах у нечестивых.

12Потому что Вечный Бог – наше солнце и щит;

Вечный даёт благодать и славу.

Тех, кто ходит непорочно,

Он не лишает благ.

13О Вечный, Повелитель Сил,

благословен человек, надеющийся на Тебя.