Masalimo 71 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 71:1-24

Salimo 71

1Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo;

musalole kuti ndichititsidwe manyazi.

2Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu,

mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.

3Mukhale thanthwe langa lothawirapo,

kumene ine nditha kupita nthawi zonse;

lamulani kuti ndipulumuke,

pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.

4Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa,

kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.

5Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse,

chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.

6Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu;

Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga,

ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.

7Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri

koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.

8Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu,

kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.

9Musanditaye pamene ndakalamba;

musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.

10Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane;

iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.

11Iwo amati, “Mulungu wamusiya;

mutsatireni ndi kumugwira,

pakuti palibe amene adzamupulumutse.”

12Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu,

bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.

13Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi,

iwo amene akufuna kundipweteka

avale chitonzo ndi manyazi.

14Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse,

ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.

15Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu,

za chipulumutso chanu tsiku lonse,

ngakhale sindikudziwa muyeso wake.

16Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse.

Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.

17Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa,

ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa

18Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu

musanditaye Inu Mulungu,

mpaka nditalengeza mphamvu zanu

kwa mibado yonse yakutsogolo.

19Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba.

Ndani wofanana nanu Inu Mulungu,

amene mwachita zazikulu?

20Ngakhale mwandionetsa mavuto

ambiri owawa,

mudzabwezeretsanso moyo wanga;

kuchokera kunsi kwa dziko lapansi,

mudzandiukitsanso.

21Inu mudzachulukitsa ulemu wanga

ndi kunditonthozanso.

22Ndidzakutamandani ndi zeze

chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu,

ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe,

Inu Woyera wa Israeli.

23Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe

pamene ndidzayimba matamando kwa Inu

amene mwandiwombola.

24Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo

tsiku lonse,

pakuti iwo amene amafuna kundipweteka

achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.

Asante Twi Contemporary Bible

Nnwom 71:1-24

Dwom 71

1Ao Awurade, wo mu na me dwane hinta;

mma mʼanim ngu ase da.

2Wo tenenee no enti, yi me na gye me;

tie me na gye me nkwa.

3Yɛ me nkwagyeɛ botan

faako a mɛtumi akɔ daa;

hyɛ ma wɔmmɛgye me nkwa,

na wo ne me botan ne mʼaban.

4Ao me Onyankopɔn, gye me firi amumuyɛfoɔ nsam,

gye me firi nnebɔneyɛfoɔ ne atirimuɔdenfoɔ nsam.

5Na woayɛ mʼanidasoɔ, Ao Asafo Awurade,

mʼahotɔsoɔ firi mʼababunu berɛ mu.

6Ɛfiri awoɔ mu, mede me ho ato wo so;

wo na woyii me firii me maame yafunu mu.

Mɛkamfo wo daa.

7Mayɛ nhwɛsodeɛ ama bebree,

nanso wo ne me dwanekɔbea denden.

8Wo nkamfo ahyɛ mʼanom ma,

mekamfo wʼanimuonyam da mu nyinaa.

9Nto me ntwene ɛberɛ a mabɔ akɔkoraa;

mʼahoɔden sa me mu a, nnya me.

10Ɛfiri sɛ mʼatamfoɔ kasa tia me

wɔn a wɔtwɛn sɛ wɔbɛkum me no bom pam me tiri so.

11Wɔka sɛ, “Onyankopɔn agya no mu;

momma yɛnti no na yɛnkyere no,

na obiara nni hɔ a ɔbɛgye no.”

12Ao Onyankopɔn, mfiri me nkyɛn nkɔ akyiri;

Ao me Onyankopɔn, yɛ ntɛm bɛboa me.

13Ma wɔn a wɔbɔ me soboɔ no nsɛe animguaseɛ mu;

wɔn a wɔpɛ sɛ wɔpira me no

ma ahohora ne animguaseɛ nkata wɔn so.

14Nanso me deɛ, mɛnya anidasoɔ daa;

mɛkɔ so makamfo wo.

15Mɛka wo tenenee ho asɛm,

ne wo nkwagyeɛ da mu nyinaa,

nanso mennim ano.

16Ao Otumfoɔ Awurade, mɛba abɛpae mu aka wo nnwuma akɛseɛ no;

mɛpae mu aka wo nko ara tenenee akyerɛ.

17Ao Onyankopɔn, ɛfiri mʼababunu berɛ na wokyerɛkyerɛɛ me,

na ɛbɛsi ɛnnɛ yi, meka wʼanwanwadeɛ a woayɛ kyerɛ.

18Mpo sɛ mebɔ akɔkoraa na mefu dwono a,

Ao Onyankopɔn, nnya me,

kɔsi sɛ mɛka wo tumi ho asɛm akyerɛ nkyirimma,

ne wo kɛseyɛ akyerɛ wɔn a wɔbɛba nyinaa.

19Ao Onyankopɔn, wo tenenee duru sorosoro,

wo a woayɛ nneɛma akɛseɛ.

Ao Onyankopɔn, hwan na ɔte sɛ wo?

20Mmom woama mahunu ɔhaw bebree a ɛyɛ yea;

nanso wobɛma me nkwa bio;

na wobɛyi me bio

afiri asase ase.

21Wobɛhyɛ me animuonyam bebree

na woakyekye me werɛ bio.

22Mede sankuo bɛkamfo wo

Ao me Onyankopɔn, wo tenenee enti

mɛto wʼayɛyi dwom wɔ sankuten so

Ao Israel Kronkronni.

23Mʼanofafa de anigyeɛ bɛteam

ɛberɛ a meto dwom kamfo woɔ,

me a woagye me no.

24Me tɛkrɛma bɛka wo tenenee nnwuma

da mu nyinaa,

ɛfiri sɛ wɔn a wɔpɛ sɛ wɔha me no

kɔ animguaseɛ ne basabasayɛ mu.