Masalimo 68 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 68:1-35

Salimo 68

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane;

adani ake athawe pamaso pake.

2Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali.

Monga phula limasungunukira pa moto,

oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.

3Koma olungama asangalale

ndi kukondwera pamaso pa Mulungu;

iwo akondwere ndi kusangalala.

4Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando,

mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo;

dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.

5Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye,

ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.

6Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja,

amatsogolera amʼndende ndi kuyimba;

koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.

7Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu,

pamene munayenda kudutsa chipululu,

8dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula,

pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai.

Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.

9Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu;

munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.

10Anthu anu anakhala mʼmenemo

ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.

11Ambuye analengeza mawu,

ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;

12“Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro;

mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.

13Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto,

mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva,

nthenga zake ndi golide wonyezimira.”

14Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko,

zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.

15Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero;

mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.

16Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri,

pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira,

kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?

17Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka,

ndi miyandamiyanda;

Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.

18Pamene Inu munakwera mmwamba,

munatsogolera a mʼndende ambiri;

munalandira mphatso kuchokera kwa anthu,

ngakhale kuchokera kwa owukira,

kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.

19Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu

amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.

20Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa;

Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.

21Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake,

zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.

22Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani;

ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.

23Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu,

pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”

24Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu;

mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.

25Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo;

pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.

26Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu;

tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.

27Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera,

pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda,

ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.

28Kungani mphamvu zanu Mulungu;

tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.

29Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu,

mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.

30Dzudzulani chirombo pakati pa mabango,

gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu.

Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva.

Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.

31Nthumwi zidzachokera ku Igupto;

Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.

32Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi

imbirani Ambuye matamando.

Sela

33Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba

amene amabangula ndi mawu amphamvu.

34Lengezani za mphamvu za Mulungu,

amene ulemerero wake uli pa Israeli

amene mphamvu zake zili mʼmitambo.

35Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika;

Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake.

Matamando akhale kwa Mulungu!

New International Version

Psalms 68:1-35

Psalm 68In Hebrew texts 68:1-35 is numbered 68:2-36.

For the director of music. Of David. A psalm. A song.

1May God arise, may his enemies be scattered;

may his foes flee before him.

2May you blow them away like smoke—

as wax melts before the fire,

may the wicked perish before God.

3But may the righteous be glad

and rejoice before God;

may they be happy and joyful.

4Sing to God, sing in praise of his name,

extol him who rides on the clouds68:4 Or name, / prepare the way for him who rides through the deserts;

rejoice before him—his name is the Lord.

5A father to the fatherless, a defender of widows,

is God in his holy dwelling.

6God sets the lonely in families,68:6 Or the desolate in a homeland

he leads out the prisoners with singing;

but the rebellious live in a sun-scorched land.

7When you, God, went out before your people,

when you marched through the wilderness,68:7 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verses 19 and 32.

8the earth shook, the heavens poured down rain,

before God, the One of Sinai,

before God, the God of Israel.

9You gave abundant showers, O God;

you refreshed your weary inheritance.

10Your people settled in it,

and from your bounty, God, you provided for the poor.

11The Lord announces the word,

and the women who proclaim it are a mighty throng:

12“Kings and armies flee in haste;

the women at home divide the plunder.

13Even while you sleep among the sheep pens,68:13 Or the campfires; or the saddlebags

the wings of my dove are sheathed with silver,

its feathers with shining gold.”

14When the Almighty68:14 Hebrew Shaddai scattered the kings in the land,

it was like snow fallen on Mount Zalmon.

15Mount Bashan, majestic mountain,

Mount Bashan, rugged mountain,

16why gaze in envy, you rugged mountain,

at the mountain where God chooses to reign,

where the Lord himself will dwell forever?

17The chariots of God are tens of thousands

and thousands of thousands;

the Lord has come from Sinai into his sanctuary.68:17 Probable reading of the original Hebrew text; Masoretic Text Lord is among them at Sinai in holiness

18When you ascended on high,

you took many captives;

you received gifts from people,

even from68:18 Or gifts for people, / even the rebellious—

that you,68:18 Or they Lord God, might dwell there.

19Praise be to the Lord, to God our Savior,

who daily bears our burdens.

20Our God is a God who saves;

from the Sovereign Lord comes escape from death.

21Surely God will crush the heads of his enemies,

the hairy crowns of those who go on in their sins.

22The Lord says, “I will bring them from Bashan;

I will bring them from the depths of the sea,

23that your feet may wade in the blood of your foes,

while the tongues of your dogs have their share.”

24Your procession, God, has come into view,

the procession of my God and King into the sanctuary.

25In front are the singers, after them the musicians;

with them are the young women playing the timbrels.

26Praise God in the great congregation;

praise the Lord in the assembly of Israel.

27There is the little tribe of Benjamin, leading them,

there the great throng of Judah’s princes,

and there the princes of Zebulun and of Naphtali.

28Summon your power, God68:28 Many Hebrew manuscripts, Septuagint and Syriac; most Hebrew manuscripts Your God has summoned power for you;

show us your strength, our God, as you have done before.

29Because of your temple at Jerusalem

kings will bring you gifts.

30Rebuke the beast among the reeds,

the herd of bulls among the calves of the nations.

Humbled, may the beast bring bars of silver.

Scatter the nations who delight in war.

31Envoys will come from Egypt;

Cush68:31 That is, the upper Nile region will submit herself to God.

32Sing to God, you kingdoms of the earth,

sing praise to the Lord,

33to him who rides across the highest heavens, the ancient heavens,

who thunders with mighty voice.

34Proclaim the power of God,

whose majesty is over Israel,

whose power is in the heavens.

35You, God, are awesome in your sanctuary;

the God of Israel gives power and strength to his people.

Praise be to God!