Masalimo 67 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 67:1-7

Salimo 67

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo.

1Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa,

achititse kuti nkhope yake itiwalire.

2Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi,

chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.

3Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;

mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.

4Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe,

pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo

ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.

5Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;

mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.

6Nthaka yabereka zokolola zake;

tidalitseni Mulungu wathu.

7Mulungu atidalitse

kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.

Asante Twi Contemporary Bible

Nnwom 67:1-7

Dwom 67

Dwom.

1Onyankopɔn nnom yɛn na ɔnhyira yɛn

ɔmma nʼanim nhyerɛn wɔ yɛn so,

2na ɔmma wɔnhunu nʼakwan wɔ asase so,

ne ne nkwagyeɛ wɔ amanaman no nyinaa mu.

3Ma adasamma nyi wo ayɛ, Ao Onyankopɔn;

ma nnipa nyinaa nkamfo wo.

4Ma amanaman ani nnye na wɔnto ahosɛpɛ dwom,

ɛfiri sɛ wodi nnipa no so tenenee mu

na woma asase so amanaman no akwankyerɛ.

5Ma adasamma nyi wo ayɛ, Ao Onyankopɔn;

ma nnipa nyinaa nkamfo wo!

6Afei asase no bɛbɔ ne nnɔbaeɛ,

na Onyankopɔn, yɛn Onyankopɔn ahyira yɛn.

7Onyankopɔn bɛhyira yɛn,

na wɔn a wɔte asase ano nyinaa bɛsuro no.