Masalimo 49 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 49:1-20

Salimo 49

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.

1Imvani izi anthu a mitundu yonse;

mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,

2anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika,

olemera pamodzinso ndi osauka:

3Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru;

mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.

4Ndidzatchera khutu langa ku mwambo,

ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.

5Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika,

pamene achinyengo oyipa andizungulira.

6Iwo amene adalira kulemera kwawo

ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?

7Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake

kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.

8Dipo la moyo ndi la mtengowapatali,

palibe malipiro amene angakwanire,

9kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya

ndi kusapita ku manda.

10Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira;

opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka

ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.

11Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya,

malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo,

ngakhale anatchula malo mayina awo.

12Ngakhale munthu akhale wachuma chotani,

adzafa ngati nyama.

13Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha,

ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula.

Sela

14Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda,

ndipo imfa idzawadya.

Olungama adzawalamulira mmawa;

matupi awo adzavunda mʼmanda,

kutali ndi nyumba zawo zaufumu.

15Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda;

ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini.

16Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera,

pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;

17Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira,

ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.

18Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala,

ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,

19iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake,

amene sadzaonanso kuwala.

20Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru

adzafa ngati nyama yakuthengo.

Luganda Contemporary Bible

Zabbuli 49:1-20

Zabbuli 49

Ya Mukulu wa Bayimbi. Zabbuli ya Batabani ba Koola.

1Muwulire mmwe amawanga gonna,

mutege amatu mmwe mwenna abali mu nsi.

2Ab’ekitiibwa n’abakopi, abagagga n’abaavu, mwenna;

muwulirize ebigambo byange.

3Kubanga ebigambo by’omu kamwa kange bya magezi,

ebiva mu mutima gwange bijjudde okutegeera.

4Nnaakozesanga ebikwata ku ngero,

nga nnyinnyonnyola amakulu gaazo n’oluyimba ku nnanga.

5Siityenga ne bwe nnaabanga mu buzibu;

newaakubadde ng’abalabe bange banneetoolodde,

6abantu abeesiga obugagga bwabwe

beenyumiririza mu bintu ebingi bye balina.

7Ddala ddala, tewali muntu ayinza kununula bulamu bwa munne,

wadde okwegula okuva eri Katonda.

8Kubanga omuwendo ogununula obulamu munene nnyo,

tewali n’omu agusobola;

9alyoke awangaale ennaku zonna

nga tatuuse magombe.

10Kubanga n’abantu abagezi bafa;

abasirusiru n’abatalina magezi bonna baaggwaawo,

obugagga bwabwe ne babulekera abalala.

11Entaana zaabwe ge ganaabanga amaka gaabwe ennaku zonna;

nga bye bisulo ebya buli mulembe oguliddawo;

baafuna ettaka mu mannya gaabwe.

12Omuntu tabeerera mirembe gyonna, ne bw’aba mugagga atya,

alifa ng’ensolo bwe zifa.

13Ako ke kabi akatuuka ku beesiga ebitaliimu,

era ye nkomerero y’abo abeesiga obugagga bwabwe.

14Okufaanana ng’endiga, bateekwa kufa;

olumbe ne lubalya.

Bakka butereevu emagombe,

obulungi bwabwe ne bubula,

amagombe ne gafuuka amaka gaabwe.

15Naye Katonda alinunula emmeeme yange mu magombe,

ddala ddala alintwala gy’ali.

16Omuntu bw’agaggawalanga n’ekitiibwa ky’ennyumba ye nga kyeyongedde,

tomutyanga,

17kubanga bw’alifa taliiko ky’alitwala, wadde n’ekitiibwa kye tekirigenda naye.

18Newaakubadde nga mu bulamu yeerowoozaako ng’aweereddwa omukisa

kubanga omugagga abantu bamugulumiza,

19kyokka alikka emagombe eri bajjajjaabe,

n’ayingira mu kizikiza ekikutte.

20Omuntu omugagga naye nga simutegeevu tabeerera mirembe gyonna,

alizikirira ng’ensolo ez’omu nsiko.