Masalimo 45 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 45:1-17

Salimo 45

Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati.

1Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma

pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu;

lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.

2Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse

ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika,

popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.

3Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu;

mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.

4Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso

mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo;

dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.

5Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu,

mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.

6Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi;

ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.

7Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;

choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu

pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.

8Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya;

kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu

nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.

9Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka;

ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.

10Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu;

iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.

11Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako;

mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.

12Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso,

amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.

13Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake,

chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.

14Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu;

anamwali okhala naye akumutsatira

ndipo abweretsedwa kwa inu.

15Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo;

akulowa mʼnyumba yaufumu.

16Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako;

udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.

17Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse;

choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.

Slovo na cestu

Žalmy 45:1-18

1Přednímu kantoru z synů Chóre, na šošannim, vyučující. Píseň o lásce. 2Vyneslo srdce mé slovo dobré, vypravovati budu písně své o králi, jazyk můj jako péro hbitého písaře. 3Krásnější jsi nad všecky syny lidské, rozlita jest i milost ve rtech tvých, proto že jest tobě požehnal Bůh až na věky. 4Připaš meč svůj na bedra, ó reku udatný, prokaž důstojnost a slávu svou. 5A v té slávě své šťastně vyjížděj s slovem pravdy, tichosti a spravedlnosti, a dokáže pravice tvá hrozných věcí. 6Střely tvé jsou ostré, padati budou od nich před tebou národové, proniknou až k srdci nepřátel královských. 7Trůn tvůj, ó Bože, jest věčný a stálý, berla království tvého jestiť berla nejupřímější. 8Miluješ spravedlnost, a nenávidíš bezbožnosti, protož pomazal tě, Bože, Bůh tvůj olejem veselé nad účastníky tvé. 9Mirra, aloe a kassia, všecka roucha tvá voní z paláců, z kostí slonových vzdělaných, nad ty, jenž tě obveselují. 10Dcery králů jsou mezi vzácnými tvými, přístojíť i manželka tobě po pravici v ryzím zlatě. 11Slyšiž, dcerko, a viz, a nakloň ucha svého, a zapomeň na lid svůj a na dům otce svého. 12I zalíbí se králi tvá krása; onť jest zajisté Pán tvůj, protož skláněj se před ním. 13Tuť i Tyrští s dary, před oblíčejem tvým kořiti se budou bohatí národové. 14Všecka slavná jest dcera královská u vnitřku, roucho zlatem vytkávané jest oděv její. 15V rouše krumpovaném přivedena bude králi, i panny za ní, družičky její, přivedeny budou k tobě. 16Přivedeny budou s radostí velikou a plésáním, a vejdou na palác královský. 17Místo otců svých budeš míti syny své, kteréž postavíš za knížata po vší zemi. 18V pamět uvoditi budu jméno tvé po všecky věky, pročež oslavovati tě budou národové na věky věků.