Masalimo 43 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 43:1-5

Salimo 43

1Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu;

ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza;

mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.

2Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga.

Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine?

Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,

woponderezedwa ndi mdani?

3Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu

kuti zinditsogolere;

mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera,

kumalo kumene inu mumakhala.

4Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu,

kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa.

Ndidzakutamandani ndi zeze,

Inu Mulungu wanga.

5Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga?

Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?

Khulupirira Mulungu,

pakuti ndidzamutamandabe Iye,

Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 43:1-5

1Gud, tag dig af min sag,43,1 Denne sang har ingen overskrift og har oprindeligt været en del af den foregående sang.

red mig fra ugudelige mennesker.

Frels mig fra falske og onde folk.

2For du er min tilflugt, Gud!

Hvorfor har du forkastet mig?

Hvorfor skal jeg plages af mine fjender?

3Send dit lys og din sandhed,

så de kan lede mig frem

og føre mig til din bolig,

til Zions hellige bjerg.

4Så vil jeg gå hen til dit alter, Gud,

du, som fylder mig med glæde,

og dér vil jeg takke dig med harpespil.

Oh, Gud, min Gud!

5Jeg siger til mig selv:

„Vær ikke mismodig og nedtrykt.

Vent tålmodigt på, at Gud griber ind.”

Når Gud har reddet mig,

vil jeg synge en takkesang til ham.