Masalimo 40 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 40:1-17

Salimo 40

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mofatsa ndinadikira Yehova

Iye anatembenukira kwa ine ndipo anamva kulira kwanga.

2Ananditulutsa mʼdzenje lachitayiko,

mʼthope ndi mʼchithaphwi;

Iye anakhazikitsa mapazi anga pa thanthwe

ndipo anandipatsa malo oyimapo olimba.

3Iye anayika nyimbo yatsopano mʼkamwa mwanga,

nyimbo yamatamando kwa Mulungu wanga.

Ambiri adzaona,

nadzaopa ndipo adzakhulupirira Yehova.

4Ndi wodala munthu

amakhulupirira Yehova;

amene sayembekezera kwa odzikuza,

kapena kwa amene amatembenukira kwa milungu yabodza.

5Zambiri, Yehova Mulungu wanga,

ndi zodabwitsa zimene Inu mwachita.

Zinthu zimene munazikonzera ife

palibe amene angathe kukuwerengerani.

Nditati ndiyankhule ndi kufotokozera,

zidzakhala zambiri kuzifotokoza.

6Nsembe ndi zopereka Inu simuzifuna,

koma makutu anga mwawatsekula;

zopereka zopsereza ndi zopereka chifukwa cha tchimo

Inu simunazipemphe.

7Kotero ndinati, “Ndili pano, ndabwera.

Mʼbuku mwalembedwa za ine.

8Ndikufuna kuchita chifuniro chanu, Inu Mulungu wanga;

lamulo lanu lili mu mtima mwanga.”

9Ndikulalikira uthenga wa chilungamo chanu mu msonkhano waukulu;

sinditseka milomo yanga

monga mukudziwa Inu Yehova.

10Sindibisa chilungamo chanu mu mtima mwanga;

ndinayankhula za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu.

Ine sindiphimba chikondi chanu ndi choonadi chanu

pa msonkhano waukulu.

11Musandichotsere chifundo chanu Yehova;

chikondi chanu ndi choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.

12Pakuti mavuto osawerengeka andizungulira;

machimo anga andigonjetsa, ndipo sindingathe kuona.

Alipo ambiri kuposa tsitsi la mʼmutu mwanga,

ndipo mtima wanga ukufowoka mʼkati mwanga.

13Pulumutseni Yehova;

Bwerani msanga Yehova kudzandithandiza.

14Onse amene akufunafuna kuchotsa moyo wanga

achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;

onse amene amakhumba chiwonongeko changa

abwezedwe mwamanyazi.

15Iwo amene amanena kwa ine kuti, “Hee! Hee!”

abwerere akuchita manyazi.

16Koma iwo amene amafunafuna Inu

akondwere ndi kusangalala mwa Inu;

iwo amene amakonda chipulumutso chanu

nthawi zonse anene kuti, “Yehova akwezeke!”

17Komabe Ine ndine wosauka ndi wosowa;

Ambuye andiganizire.

Inu ndinu thandizo langa ndi wondiwombola wanga;

Inu Mulungu wanga, musachedwe.

Korean Living Bible

시편 40:1-17

시련 가운데서 인내하는 믿음

(다윗의 시. 성가대 지휘자를 따라 부른 노래)

1내가 여호와의 도움을

끈기 있게 기다렸더니

그가 귀를 기울이시고

나의 부르짖음을 들으셨다.

2여호와께서 나를

40:2 또는 ‘기가 막힐 웅덩이와 수렁에서’절망의 웅덩이와 진흙탕 속에서

끌어내시고

나를 반석 위에 세우셔서

안전하게 걸어다니도록 하셨다.

3그가 새 노래를

나에게 가르쳐 주셨으니

우리 하나님께 불러 드릴

찬송이라네.

많은 사람들이

이것을 보고 두려워하여

여호와를 신뢰하리라.

4여호와를 의지하고

교만한 자와

거짓된 신을 좇는 자를

우러러보지 않는 사람은

복 있는 자이다.

5여호와 나의 하나님이시여,

주는 우리를 위해 수많은

기적을 행하셨습니다.

주께서 우리를 위해 생각하시고

계획하신 그 놀라운 일은

아무도 헤아릴 수가 없습니다.

내가 그 모든 것을

말하려고 하지만

너무 많아 일일이 다

열거할 수가 없습니다.

6주께서는 제사와 예물을

원하지 않으시며

또 불로 태워 바치는 번제나

죄를 씻는 속죄제를

요구하시지 않으시고

40:6 70인역에는 ‘나를 위해 한 몸을 예비하셨다’ 로 되어 있음.내 귀를 열어 주셨습니다.

7그때 내가 말하였습니다.

“보십시오. 내가 왔습니다.

나에 관한 것이

40:7 또는 ‘두루마리책에’율법책에 기록되어 있습니다.

8나의 하나님이시여,

주의 뜻을 행하는 일을

내가 기쁘게 여기고

내가 항상 주의 법을

마음에 간직하고 있습니다.”

9내가 많은 군중 앞에서

40:9 또는 ‘의의 기쁜 소식을’구원의 기쁜 소식을 전하였습니다.

여호와여, 내가 입을 다물지 않고

계속 이것을 말하리라는 것은

주께서도 아십니다.

10내가 이 구원의 소식을

내 마음에 숨기지 않았습니다.

나는 항상 주의 신실하심과

구원을 선포하였으며

주의 한결같은 사랑과 진리를

대중 앞에서 숨기지 않았습니다.

11여호와여, 주의 자비를

내게서 거두지 마시고

주의 사랑과 진리로

나를 항상 보호하소서.

12헤아릴 수 없는 수많은 문제들이

나를 둘러싸고 있으며

내 죄가 나를 덮치므로

내가 볼 수 없고

내 죄가 머리털보다 많으므로

내 기가 꺾였습니다.

13여호와여,

기꺼이 나를 구하소서.

속히 와서 나를 도우소서.

14나를 죽이려 하는 자들이

수치를 당하고

당황하게 하시며

내가 패망하기를

바라는 자들이

망신을 당하고 물러가게 하소서.

15나를 보고 야유하는 자들이

자기들의 수치에 놀라게 하소서.

16그러나 주를 찾는 자들은

모두 주 안에서

기뻐하고 즐거워하게 하시며

주의 구원을

사모하는 자들은 항상

“여호와는 위대하시다!”

하고 말하게 하소서.

1740:17 또는 ‘나는 가난하고 궁핍하오나’내가 고난을 당하고 가난하지만

주께서 항상 나를 생각하시니

주는 나의 도움이시요

나를 건지는 자이십니다.

나의 하나님이시여,

지체하지 마소서.