Masalimo 37 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 37:1-40

Salimo 37

Salimo la Davide.

1Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa

kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;

2pakuti monga udzu iwo adzafota msanga,

ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.

3Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino;

khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.

4Udzikondweretse wekha mwa Yehova

ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.

5Pereka njira yako kwa Yehova;

dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:

6Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha,

chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.

7Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa;

usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo,

pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.

8Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali,

usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.

9Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa,

koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.

10Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso;

ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.

11Koma ofatsa adzalandira dziko

ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.

12Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama

ndipo amawakukutira mano;

13koma Ambuye amaseka oyipa

pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.

14Oyipa amasolola lupanga

ndi kupinda uta

kugwetsa osauka ndi osowa,

kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.

15Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe,

ndipo mauta awo anathyoka.

16Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo

ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;

17pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka,

koma Yehova amasunga olungama.

18Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova,

ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.

19Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota;

mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.

20Koma oyipa adzawonongeka;

adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo,

iwo adzazimirira ngati utsi.

21Oyipa amabwereka ndipo sabweza

koma olungama amapereka mowolowamanja.

22Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko,

koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.

23Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu,

amakhazikitsa mayendedwe ake;

24ngakhale atapunthwa sadzagwa,

pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.

25Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba

koma sindinaonepo olungama akusiyidwa

kapena ana awo akupempha chakudya.

26Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu;

ana awo adzadalitsika.

27Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino;

pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.

28Pakuti Yehova amakonda wolungama

ndipo sadzasiya okhulupirika ake.

Iwo adzatetezedwa kwamuyaya,

koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;

29olungama adzalandira dziko

ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.

30Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru,

ndipo lilime lake limayankhula zolungama.

31Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake;

mapazi ake saterereka.

32Oyipa amabisala kudikira olungama;

kufunafuna miyoyo yawoyo;

33koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo

kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.

34Khulupirira Yehova,

ndipo sunga njira yake;

Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako;

udzaona anthu oyipa akuwonongeka.

35Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo

akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.

36Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso;

ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.

37Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama;

udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.

38Koma anthu ochimwa adzawonongeka;

iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.

39Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova;

Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.

40Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa;

Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa,

pakuti amathawira kwa Iye.

Slovo na cestu

Žalmy 37:1-40

1Žalm Davidův. Nehněvej se příčinou zlostníků, nechtěj záviděti těm, kteříž páší nepravost. 2Nebo jako tráva v náhle podťati budou, a jako zelená bylina uvadnou. 3Doufej v Hospodina, a 4Těš se v Hospodinu, a dá tobě žádosti srdce tvého. 5Uval na Hospodina cestu svou, a slož v něm naději, onť zajisté všecko spraví. 6A vyvedeť spravedlnost tvou jako světlo, a nevinu tvou jako poledne. 7Mlčelivě se měj k Hospodinu, a očekávej na něj pečlivě. Nekormuť se příčinou toho, jemuž se daří na cestě jeho, příčinou člověka, kterýž provodí, cožkoli umyslil. 8Pusť mimo sebe hněv, a zanech prchlivosti; nezpouzej se tak, abys zle činiti chtěl. 9Nebo zlostníci vypléněni budou, ale ti, kteříž očekávají na Hospodina, dědičně zemí vládnouti budou. 10Po malé chvíli zajisté, anť bezbožníka nebude, a pohledíš na místo jeho, anť ho již není. 11Ale tiší dědičně obdrží zemi, a rozkoš míti budou ve množství pokoje. 12Zle myslí bezbožník o spravedlivém, a škřipí na něj zuby svými, 13Ale Hospodin směje se jemu; nebo vidí, že se přibližuje den jeho. 14Vytrhujíť bezbožníci meč, a natahují lučiště své, aby porazili chudého a nuzného, aby hubili ty, kteříž jsou ctného obcování; 15Ale meč jejich vejde v jejich srdce, a lučiště jejich budou polámána. 16Lepší jest málo, což má spravedlivý, než veliká bohatství bezbožníků mnohých. 17Nebo ramena bezbožných polámána budou, spravedlivé pak zdržuje Hospodin. 18Znáť Hospodin dny upřímých, protož dědictví jejich na věky zůstane. 19Nebudouť zahanbeni v čas zlý, a ve dnech hladu nasyceni budou; 20Ale bezbožníci zahynou, a nepřátelé Hospodinovi, jak tuk beranů s dymem mizí, tak zmizejí. 21Vypůjčuje bezbožník, a nemá co oplatiti, ale spravedlivý milost činí, a rozdává. 22Nebo požehnaní ode Pána zemí vládnouti budou, ale zlořečení od něho budou vypléněni. 23Krokové člověka spravedlivého od Hospodina spravováni bývají, a cestu jeho libuje. 24Jestliže by upadl, neurazí se; nebo Hospodin drží jej za ruku jeho. 25Mlad jsem byl, a sstaral jsem se, a neviděl jsem spravedlivého opuštěného, ani semene jeho žebrati chleba. 26Každého dne milost činí, i půjčuje, a však símě jeho jest v požehnání. 27Odstup od zlého, a čiň dobré, a bydliti budeš na věky. 28Nebo Hospodin miluje soud, a neopouští svatých svých, na věky v stráži jeho budou; símě pak bezbožníků bude vypléněno. 29Ale spravedliví ujmou zemi dědičně, a na věky v ní přebývati budou. 30Ústa spravedlivého mluví moudrost, a jazyk jeho vynáší soud. 31Zákon Boha jeho jest v srdci jeho, pročež nepodvrtnou se nohy jeho. 32Špehujeť bezbožník po spravedlivém, a hledá ho zahubiti; 33Ale Hospodin ho nenechá v ruce jeho, aniž ho dopustí potupiti, když by souzen byl. 34Očekávejž tedy na Hospodina, a ostříhej cesty jeho, a on tě povýší, abys dědičně obdržel zemi, z níž že vykořeněni budou bezbožníci, uhlédáš. 35Viděl jsem bezbožníka hrozné síly, an se rozložil jako zelený samorostlý strom. 36Ale tudíž pominul, a aj nebylo ho; nebo hledal jsem ho, a není nalezen. 37Pozor měj na pobožného, a viz upřímého, žeť takového člověka poslední věci jsou potěšené, 38Přestupníci pak že tolikéž vyhlazeni budou, a bezbožníci naposledy vyťati. 39Ale spasení spravedlivých jest od Hospodina, onť jest síla jejich v času ssoužení. 40Spomáháť jim Hospodin, a je vytrhuje, vytrhuje je od bezbožníků, a zachovává je; nebo doufají v něho.