Masalimo 28 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 28:1-9

Salimo 28

Salimo la Davide.

1Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa;

musakhale osamva kwa ine.

Pakuti mukapitirira kukhala chete,

ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

2Imvani kupempha chifundo kwanga

pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize,

pomwe ndikukweza manja anga

kuloza ku malo anu oyeretsetsa.

3Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa,

pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa,

amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo

koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.

4Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo

ndi ntchito zawo zoyipa;

abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita

ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.

5Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova,

ndi zimene manja ake anazichita,

Iye adzawakhadzula

ndipo sadzawathandizanso.

6Matamando apite kwa Yehova,

popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.

7Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa;

mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.

Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe

ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.

8Yehova ndi mphamvu ya anthu ake,

linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.

9Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu;

mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.

New Russian Translation

Псалтирь 28:1-11

Псалом 28

1Псалом Давида.

Хвалите Господа, о Божьи сыны28:1 Божьи сыны – возможное значение: «ангелы».,

хвалите Господа за славу Его и мощь.

2Воздайте славу имени Господа,

поклонитесь Господу в красоте Его святости28:2 Или: «в храме Его прекрасном»..

3Голос Господень – над водами,

гремит Бог славы,

Господь гремит над могучими водами.

4Голос Господа полон мощи,

голос Господа величественен.

5Голос Господа кедры сокрушает,

Господь сокрушает кедры Ливана.

6Он велит Ливану скакать, подобно теленку,

Сириону28:6 То есть горе Хермон. – подобно молодому дикому быку.

7Голос Господа как молния разит.

8Голос Господа сотрясает пустыню,

Господь сотрясает пустыню Кадеш.

9Голос Господа гнет дубы28:9 Или: «рожать заставляет ланей».

и нагим оставляет лес.

В Его храме все восклицают: «Слава!»

10Господь восседал над потопом;

Господь восседает как Царь вовеки.

11Господь дает силу Своему народу;

Господь благословляет Свой народ миром.