Masalimo 28 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 28:1-9

Salimo 28

Salimo la Davide.

1Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa;

musakhale osamva kwa ine.

Pakuti mukapitirira kukhala chete,

ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

2Imvani kupempha chifundo kwanga

pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize,

pomwe ndikukweza manja anga

kuloza ku malo anu oyeretsetsa.

3Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa,

pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa,

amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo

koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.

4Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo

ndi ntchito zawo zoyipa;

abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita

ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.

5Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova,

ndi zimene manja ake anazichita,

Iye adzawakhadzula

ndipo sadzawathandizanso.

6Matamando apite kwa Yehova,

popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.

7Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa;

mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.

Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe

ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.

8Yehova ndi mphamvu ya anthu ake,

linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.

9Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu;

mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.

Het Boek

Psalmen 28:1-9

1Van David. Tot U roep ik, Jahweh, mijn Rots! Ach, houd U voor mij niet doof: Opdat ik, als Gij blijft zwijgen, Niet gelijk word aan hen, die in het graf zijn gedaald. 2Hoor, Jahweh, mijn zuchten, Nu ik tot U smeek, En mijn handen hef Naar uw heilige woning. 3Werp mij niet weg met de bozen, Niet weg met de zondaars, Die lief doen tegen hun naaste, Maar met venijn in het hart. 4Zet ze hun werken betaald, En hun schandelijk gedrag; Vergeld ze het werk hunner handen, En geef hun wat ze verdienen. 5Want ze begrijpen niets van Jahweh’s daden, Niets van wat door zijn hand werd verricht; Daarom breekt Hij ze af, En bouwt ze niet op! 6Geprezen zij Jahweh! Want Hij heeft mijn smeken gehoord; 7Jahweh is mijn schuts en mijn schild. Als mijn hart op Hem hoopt, word ik zeker geholpen; Daarom jubelt mijn hart, en zegen ik Hem met mijn lied! 8Jahweh is een schuts voor zijn volk, En voor zijn Gezalfde een machtige hulp. 9Red dus uw volk en zegen uw erfdeel; Weid hen en leid hen voor eeuwig!