Masalimo 17 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 17:1-15

Salimo 17

Pemphero la Davide.

1Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo;

mverani kulira kwanga.

Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa

popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.

2Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu;

maso anu aone chimene ndi cholungama.

3Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku,

ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu;

Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.

4Kunena za ntchito za anthu,

monga mwa mawu a pakamwa panu,

Ine ndadzisunga ndekha

posatsata njira zachiwawa.

5Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu;

mapazi anga sanaterereke.

6Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha;

tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.

7Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu,

Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja

iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.

8Mundisunge ine ngati mwanadiso;

mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,

9kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine,

kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.

10Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo,

ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.

11Andisaka, tsopano andizungulira

ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.

12Iwo ali ngati mkango wofuna nyama;

ngati mkango waukulu wokhala mobisala.

13Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi;

landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.

14Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere,

kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno.

Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu;

ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri,

ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.

15Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu;

pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 17:1-15

Zaburi 17

Sala Ya Mtu Asiye Na Hatia

Sala ya Daudi.

117:1 Za 30:10; 64:1; 80:1; 140:6; 5:1, 2; 39:12; 142:6; 143:1; Isa 29:13Sikia, Ee Bwana, kusihi kwangu kwa haki,

sikiliza kilio changu.

Tega sikio kwa ombi langu,

halitoki kwenye midomo ya udanganyifu.

217:2 Za 24:5; 26:1; 99:4; Isa 46:13; 50:8-9; 54:17Hukumu yangu na itoke kwako,

macho yako na yaone yale yaliyo haki.

317:3 Za 139:1; Yak 3:2; Ay 7:18; 23:10; Yer 12:3; 50:20Ingawa unauchunguza moyo wangu na kunikagua usiku,

ingawa umenijaribu, hutaona chochote.

Nimeamua kwamba kinywa changu

hakitatenda dhambi.

417:4 Rum 12:2Kuhusu matendo ya wanadamu:

kwa neno la midomo yako,

nimejiepusha

na njia za wenye jeuri.

517:5 Ay 23:11; Za 44:18; 73:2; 121:3; Kum 32:35Hatua zangu zimeshikamana na njia zako;

nyayo zangu hazikuteleza.

617:6 Za 84:7; 116:2; 4:1Ee Mungu, ninakuita, kwa kuwa utanijibu,

nitegee sikio lako na usikie ombi langu.

717:7 Za 31:21; 69:13; 106:45; 107:43; 117:2; 10:12; 2:12Uonyeshe ajabu ya upendo wako mkuu,

wewe uokoaye kwa mkono wako wa kuume

wale wanaokukimbilia kutokana na adui zao.

817:8 Hes 6:24; Isa 34:15; Kum 32:10; Mit 7:2; Za 27:5; 31:20; 32:7; 36:7; 63:7; Rum 2:12Nilinde kama mboni ya jicho lako,

unifiche chini ya kivuli cha mbawa zako

917:9 Za 109:3kutokana na waovu wanaonishambulia,

kutokana na adui wauaji wanaonizunguka.

1017:10 Za 73:7; 119:70; Isa 6:10; 2:3Huifunga mioyo yao iliyo migumu,

vinywa vyao hunena kwa majivuno.

1117:11 Za 88:17; 1Sam 23:26Wamenifuatia nyayo zangu, sasa wamenizingira,

wakiwa macho, waniangushe chini.

1217:12 Za 7:2; Yer 5:6; 12:8; Mao 3:10; Mwa 49:9Wamefanana na simba mwenye njaa awindaye,

kama simba mkubwa anyemeleaye mafichoni.

1317:13 Za 35:8; 55:23; 73:18; Hes 10:3Inuka, Ee Bwana, pambana nao, uwaangushe,

niokoe kutokana na waovu kwa upanga wako.

1417:14 Za 49:17; Lk 16:8, 25; Isa 2:7; 57:17Ee Bwana, mkono wako uniokoe na watu wa jinsi hii,

kutokana na watu wa ulimwengu huu

ambao fungu lao liko katika maisha haya.

Na wapate adhabu ya kuwatosha.

Watoto wao na wapate zaidi ya hayo,

hukumu na iendelee kwa watoto wa watoto wao.

1517:15 Za 3:5; Hes 12:2; Mt 5:8; 1Yn 3:2Na mimi katika haki nitauona uso wako,

niamkapo, nitaridhika kwa kuona sura yako.