Masalimo 15 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 15:1-5

Salimo 15

Salimo la Davide.

1Yehova, ndani angathe kukhala mʼmalo anu opatulika?

Kodi ndani angathe kukhala mʼphiri lanu loyera?

2Munthu wa makhalidwe abwino,

amene amachita zolungama,

woyankhula choonadi chochokera mu mtima mwake,

3ndipo mʼkamwa mwake simutuluka mawu osinjirira,

amene sachitira choyipa mnansi wake

kapena kufalitsa mbiri yoyipa ya munthu mnzake,

4amene sapereka ulemu kwa munthu woyipa.

Koma amalemekeza amene amaopa Yehova,

amene amakwaniritsa zomwe walonjeza

ngakhale pamene zikumupweteka,

5amene amakongoletsa ndalama zake popanda chiwongoladzanja

ndipo salandira chiphuphu pofuna kutsutsa anthu osalakwa.

Iye amene amachita zinthu zimenezi

sadzagwedezeka konse.

Swedish Contemporary Bible

Psaltaren 15:1-5

Psalm 15

Ett rättfärdigt liv

1En psalm av David.

Herre, vem får bo i ditt tält?

Vem får vistas uppe på ditt heliga berg?

2Den som lever ett oklanderligt liv,

gör det som är rättfärdigt

och talar sanning av hjärtat,

3den som inte förtalar andra,

den som inte skadar sin granne

eller vanärar sin medmänniska,

4den som föraktar den förkastlige

men ärar dem som fruktar Herren,

den som håller sin ed även om det skulle skada honom,

5den som inte lånar ut pengar mot ränta

och vägrar att ta emot mutor för att fälla en oskyldig.

Den som gör så kommer aldrig att vackla.